Masalimo 61 – CCL & NTLR

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 61:1-8

Salimo 61

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

1Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;

mvetserani pemphero langa.

2Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu

ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;

tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.

3Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,

nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

4Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya

ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.

5Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;

mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

6Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,

zaka zake kwa mibado yochuluka.

7Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;

ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

8Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu

ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

Nouă Traducere În Limba Română

Psalmii 61:1-8

Psalmul 61

Pentru dirijor. De cântat cu instrumente cu coarde. Al lui David.

1Ascultă, Dumnezeule, strigătul meu!

Ia aminte la rugăciunea mea!

2Te chem de la capătul pământului

cu inima mâhnită:

„Condu‑mă la stânca mai înaltă decât mine!“

3Căci Tu ești un adăpost pentru mine,

un turn tare împotriva dușmanului.

4Aș vrea să locuiesc în cortul Tău pe vecie,

să mă adăpostesc sub învelișul aripilor Tale. Selah

5Căci Tu, Dumnezeule, mi‑ai ascultat jurămintele;

Tu mi‑ai dat moștenirea celor ce se tem de Numele Tău.

6Adaugă zile la zilele regelui!

Anii lui să‑i fie ca ai multor generații!

7Fie să troneze veșnic în prezența lui Dumnezeu!

Pune îndurarea și credincioșia să vegheze asupra lui!

8Atunci voi cânta spre lauda Numelui Tău întotdeauna

și‑mi voi împlini jurămintele zi de zi.