Masalimo 60 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 60:1-12

第 60 篇

祈求上帝的帮助

大卫作的诗,交给乐长,叫人学习,调用“作证的百合花”。当时大卫跟美索不达米亚西北部和叙利亚中部的亚兰人打仗,约押在盐谷杀了一万两千以东人。

1上帝啊,

你遗弃了我们,

使我们一败涂地;

你曾向我们发怒,

求你现在复兴我们。

2你震动大地,将它撕裂。

求你修补裂口,

因为它要塌陷了。

3你叫我们——你的子民吃尽苦头,

喝了令我们东倒西歪的苦酒。

4但你赐给敬畏你的人旗帜,

可以挡住箭羽60:4 挡住箭羽”或译作“为真理飘扬”。(细拉)

5求你应允我们的祷告,

伸出右手帮助我们,

使你所爱的人获救。

6上帝在祂的圣所说:

“我要欢然划分示剑

丈量疏割谷。

7基列是我的,

玛拿西也是我的,

以法莲是我的头盔,

犹大是我的权杖。

8摩押是我的洗脚盆,

我要把鞋扔给以东

我要在非利士高唱凯歌。”

9谁能带我进入坚固的城池?

谁能领我到以东

10上帝啊,你抛弃了我们吗?

不再和我们的军队一同出战了吗?

11求你帮助我们攻打仇敌,

因为人的帮助徒然无益。

12我们依靠上帝才能取胜,

祂必把我们的敌人踩在脚下。