Masalimo 49 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 49:1-20

Salimo 49

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Imvani izi anthu a mitundu yonse;

mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,

2anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika,

olemera pamodzinso ndi osauka:

3Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;

mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

4Ndidzatchera khutu langa ku mwambo,

ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

5Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika,

pamene achinyengo oyipa andizungulira.

6Iwo amene adalira kulemera kwawo

ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?

7Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake

kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.

8Dipo la moyo ndi la mtengowapatali,

palibe malipiro amene angakwanire,

9kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya

ndi kusapita ku manda.

10Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira;

opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka

ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.

11Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya,

malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo,

ngakhale anatchula malo mayina awo.

12Ngakhale munthu akhale wachuma chotani,

adzafa ngati nyama.

13Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha,

ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula.

Sela

14Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda,

ndipo imfa idzawadya.

Olungama adzawalamulira mmawa;

matupi awo adzavunda mʼmanda,

kutali ndi nyumba zawo zaufumu.

15Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda;

ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.

16Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera,

pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;

17Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira,

ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.

18Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala,

ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,

19iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake,

amene sadzaonanso kuwala.

20Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru

adzafa ngati nyama yakuthengo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 49:1-20

第 49 篇

财富的虚幻

可拉后裔的诗,交给乐长。

1万民啊,你们要听!

世人啊,

2不论贵贱贫富,都要留心听!

3因为我口出智慧,心思明智。

4我要侧耳听箴言,

弹琴解释人生之谜。

5危难来临,四面被奸诈之徒包围时,我何必惧怕?

6他们倚靠金钱、夸耀财富,

7却不能救赎自己的生命,

也无法向上帝付生命的赎价。

8因为生命的赎价高昂,

无人付得起,

9以致可以永远活着,不进坟墓。

10众所周知,即使智者也要死去,

愚人和庸者也要灭亡,

将他们的财富留给别人。

11尽管他们用自己的名字来为产业命名,

坟墓却是他们永远的归宿,

世代的住处。

12人不能长享富贵,

终必死去,与兽无异。

13这就是愚昧人及其追随者的下场!(细拉)

14他们注定要死,与羊无异,

死亡是他们的牧者;

到了早晨,

他们必被正直人管辖。

他们的躯体必朽烂在坟墓里,

远离自己的豪宅。

15但上帝必救赎我的生命脱离死亡的权势,

接我到祂身边。(细拉)

16因此,见他人财富增多,

日益奢华,

不要害怕。

17因为他们死后什么也带不走,

再不能拥有荣华富贵。

18他们活着时自以为有福,

人们都赞扬他们的成就,

19到头来他们还是要归到祖先那里,

再也看不见光明。

20人有财富,却无明智的心,

无异于必死的兽类。