Masalimo 46 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 46:1-11

Salimo 46

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.

1Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,

thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.

2Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,

ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,

3ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,

ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.

4Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,

malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.

5Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;

Mulungu adzawuthandiza mmawa.

6Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;

Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.

7Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

8Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,

chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.

9Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;

Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo;

amatentha zishango ndi moto.

10Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;

ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu;

ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”

11Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

New International Version – UK

Psalms 46:1-11

Psalm 46In Hebrew texts 46:1-11 is numbered 46:2-12.

For the director of music. Of the Sons of Korah. According to alamoth.Title: Probably a musical term A song.

1God is our refuge and strength,

an ever-present help in trouble.

2Therefore we will not fear, though the earth give way

and the mountains fall into the heart of the sea,

3though its waters roar and foam

and the mountains quake with their surging.46:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 7 and 11.

4There is a river whose streams make glad the city of God,

the holy place where the Most High dwells.

5God is within her, she will not fall;

God will help her at break of day.

6Nations are in uproar, kingdoms fall;

he lifts his voice, the earth melts.

7The Lord Almighty is with us;

the God of Jacob is our fortress.

8Come and see what the Lord has done,

the desolations he has brought on the earth.

9He makes wars cease

to the ends of the earth.

He breaks the bow and shatters the spear;

he burns the shields46:9 Or chariots with fire.

10He says, ‘Be still, and know that I am God;

I will be exalted among the nations,

I will be exalted in the earth.’

11The Lord Almighty is with us;

the God of Jacob is our fortress.