Salimo 45
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.
1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma
pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;
lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse
ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,
popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;
mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso
mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;
dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,
mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;
ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu
pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;
kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu
nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;
ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;
iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;
mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,
amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,
chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;
anamwali okhala naye akumutsatira
ndipo abweretsedwa kwa inu.
15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;
akulowa mʼnyumba yaufumu.
16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;
udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;
choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Psalm 45In Hebrew texts 45:1-17 is numbered 45:2-18.
For the director of music. To the tune of ‘Lilies’. Of the Sons of Korah. A maskil.Title: Probably a literary or musical term A wedding song.
1My heart is stirred by a noble theme
as I recite my verses for the king;
my tongue is the pen of a skilful writer.
2You are the most excellent of men
and your lips have been anointed with grace,
since God has blessed you for ever.
3Gird your sword on your side, you mighty one;
clothe yourself with splendour and majesty.
4In your majesty ride forth victoriously
in the cause of truth, humility and justice;
let your right hand achieve awesome deeds.
5Let your sharp arrows pierce the hearts of the king’s enemies;
let the nations fall beneath your feet.
6Your throne, O God,45:6 Here the king is addressed as God’s representative. will last for ever and ever;
a sceptre of justice will be the sceptre of your kingdom.
7You love righteousness and hate wickedness;
therefore God, your God, has set you above your companions
by anointing you with the oil of joy.
8All your robes are fragrant with myrrh and aloes and cassia;
from palaces adorned with ivory
the music of the strings makes you glad.
9Daughters of kings are among your honoured women;
at your right hand is the royal bride in gold of Ophir.
10Listen, daughter, and pay careful attention:
Forget your people and your father’s house.
11Let the king be enthralled by your beauty;
honour him, for he is your lord.
12The city of Tyre will come with a gift,45:12 Or A Tyrian robe is among the gifts
people of wealth will seek your favour.
13All glorious is the princess within her chamber;
her gown is interwoven with gold.
14In embroidered garments she is led to the king;
her virgin companions follow her –
those brought to be with her.
15Led in with joy and gladness,
they enter the palace of the king.
16Your sons will take the place of your fathers;
you will make them princes throughout the land.
17I will perpetuate your memory through all generations;
therefore the nations will praise you for ever and ever.