Salimo 47
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.
1Ombani mʼmanja, inu anthu onse;
fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba;
Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu;
anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4Iye anatisankhira cholowa chathu,
chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda.
Sela
5Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe,
Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando;
imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi;
imbirani Iye salimo la matamando.
8Mulungu akulamulira mitundu ya anthu;
Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana
monga anthu a Mulungu wa Abrahamu,
pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu;
Iye wakwezedwa kwakukulu.
Psalm 47In Hebrew texts 47:1-9 is numbered 47:2-10.
For the director of music. Of the Sons of Korah. A psalm.
1Clap your hands, all you nations;
shout to God with cries of joy.
2For the Lord Most High is awesome,
the great King over all the earth.
3He subdued nations under us,
peoples under our feet.
4He chose our inheritance for us,
the pride of Jacob, whom he loved.47:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
5God has ascended amid shouts of joy,
the Lord amid the sounding of trumpets.
6Sing praises to God, sing praises;
sing praises to our King, sing praises.
7For God is the King of all the earth;
sing to him a psalm of praise.
8God reigns over the nations;
God is seated on his holy throne.
9The nobles of the nations assemble
as the people of the God of Abraham,
for the kings47:9 Or shields of the earth belong to God;
he is greatly exalted.