Masalimo 42 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 42:1-11

BUKU LACHIWIRI

Masalimo 42–72

Salimo 42

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi,

kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.

2Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo.

Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?

3Misozi yanga yakhala chakudya changa

usana ndi usiku,

pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti,

“Mulungu wako ali kuti?”

4Zinthu izi ndimazikumbukira

pamene ndikukhuthula moyo wanga:

momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu,

kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu

ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko

pakati pa anthu a pa chikondwerero.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Yembekezera Mulungu,

pakuti ndidzamulambirabe,

Mpulumutsi wanga ndi 6Mulungu wanga.

Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga

kotero ndidzakumbukira Inu

kuchokera ku dziko la Yorodani,

ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.

7Madzi akuya akuyitana madzi akuya

mu mkokomo wa mathithi anu;

mafunde anu onse obwera mwamphamvu

andimiza.

8Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake,

nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane;

pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.

9Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa,

“Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?”

10Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo

pamene adani anga akundinyoza,

tsiku lonse akunena kuti,

“Mulungu wako ali kuti?”

11Bwanji ukumva chisoni,

iwe mtima wanga?

Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso,

Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 42:1-11

卷二:诗篇42—72

第 42 篇

流落异乡者的祷告

可拉后裔作的训诲诗,交给乐长。

1上帝啊,我的心切慕你,

像鹿切慕溪水。

2我心里渴慕上帝,

渴慕永活的上帝,

我何时才能去朝拜祂呢?

3我不吃不喝,昼夜以泪洗面,

人们整天讥笑我:

“你的上帝在哪里?”

4从前我带领众人浩浩荡荡去上帝的殿,

在欢呼、感恩声中一起过节。

我回想这些事,

心中无限忧伤。

5我的心啊!

你为何沮丧?为何烦躁?

要仰望上帝,

因为我还要赞美祂——我的救主,我的上帝。

6我的上帝啊,我心中沮丧,

便在约旦河、黑门山和米萨山想起你。

7你的瀑布发出巨响,

回荡在深渊之间,

你的洪涛巨浪淹没我。

8白天耶和华将祂的慈爱浇灌我;

夜间我歌颂祂,

向赐我生命的上帝祷告。

9我对上帝——我的磐石说:

“你为何忘记我?

为何要我受仇敌的攻击,使我哀伤不已呢?”

10仇敌的辱骂刺骨钻心。

他们整天对我说:

“你的上帝在哪里?”

11我的心啊!

你为何沮丧?为何烦躁?

要仰望上帝,

因为我还要赞美祂——我的救主,我的上帝。