Masalimo 43 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 43:1-5

Salimo 43

1Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 43:1-5

第 43 篇

流亡异乡者的祷告

1上帝啊,

求你为我伸张正义,

在不虔敬的人面前为我辩护,

救我脱离诡诈邪恶的人。

2你是保护我的上帝,

你为何丢弃我?

为何让我受仇敌的攻击,

使我哀伤不已呢?

3求你以光明和真理引导我,

领我到你的圣山,到你的居所。

4我要到上帝的祭坛前,

到赐我喜乐的上帝面前。

上帝啊,我的上帝,

我要弹琴赞美你。

5我的心啊!

你为何沮丧?为何烦躁?

要仰望上帝,

因为我还要赞美祂——我的救主,我的上帝。