Masalimo 30 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 30:1-12

Salimo 30

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.

1Ndidzakukwezani Yehova,

chifukwa mwanditulutsa kwakuya,

ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.

2Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo

ndipo Inu munandichiritsa.

3Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,

munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

4Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;

tamandani dzina lake loyera.

5Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi

koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;

utha kuchezera kulira usiku wonse,

koma chimwemwe chimabwera mmawa.

6Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,

“Sindidzagwedezekanso.”

7Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,

munachititsa phiri langa kuyima chilili;

koma pamene munabisa nkhope yanu,

ndinataya mtima.

8Kwa Inu Yehova ndinayitana;

kwa Ambuye ndinapempha chifundo;

9“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga

ngati nditsikira ku dzenje?

Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?

Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

10Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;

Yehova mukhale thandizo langa.”

11Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;

munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,

12kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 30:1-13

Lovsang efter helbredelse

1En sang af David, som blev sunget ved templets indvielse.

2Herre, jeg priser dig, for du reddede mig.

Mine fjender fik ikke lov at triumfere over mig.

3Herre, min Gud, jeg råbte om hjælp,

og du helbredte mig.

4Du reddede mig fra den sikre død,

kaldte mig tilbage fra gravens rand.

5Syng for Herren, I, som adlyder ham!

Pris hans hellige navn!

6Hans vrede varer et øjeblik,

men hans nåde bringer livet tilbage.

Den gråd, der lyder om natten,

afløses af glæde om morgenen.

Selvsikkerhedens fristelse

7Jeg blev selvsikker og mente,

jeg kunne klare det hele.

8Men det var jo din nåde,

der gjorde mig til det, jeg var.

Så da du vendte dig fra mig,

blev jeg grebet af panik.

9Jeg råbte til dig, Herre,

tryglede dig om nåde.

10„Hvad opnår du ved, at jeg dør?

Hvad gavner det, at jeg lægges i graven?

Kan en død synge lovsange

eller fortælle om din trofasthed?

11Hør på mig, Herre, og vær mig nådig.

Herre, kom og hjælp mig.”

12Da vendte du min sorg til glæde,

tog min sørgedragt og klædte mig i festtøj.

13Nu kan jeg synge af glæde,

fra nu af vil jeg altid takke dig.