Masalimo 31 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 31:1-25

Tillid i kriser

1Til korlederen: En sang af David.

2Herre, jeg søger ly hos dig,

for du svigter mig aldrig.

Kom og red mig,

for du er altid trofast.

3Bøj dig og lyt til min bøn,

grib ind og red mig hurtigt.

Vær du min fæstning og mit tilflugtssted,

hvor mine fjender ikke kan nå mig.

4Ja, du er min klippeborg og min fæstning.

Hjælp mig igen, og jeg vil ære dig.

5Gør mig fri af den fælde, mine fjender har sat,

for du er mit håb og min tilflugt.

6Mit liv er i dine hænder.31,6 Mere ordret: „I dine hænder betror jeg min ånd.”

Frels mig, Herre, min trofaste Gud.

7Jeg hader dem, der dyrker jammerlige afguder.

Jeg stoler altid selv på dig og din magt.

8Jeg jubler over din trofaste nåde,

for du kender mine problemer,

og du har set mine lidelser.

9Du udleverede mig ikke til fjenden,

men førte mig til et sikkert sted.

10Herre, vær mig nådig,

for jeg er i nød.

Mine øjne er røde af gråd,

mit indre fortæres af smerte.

11Jeg er døden nær af sorg,

mine dage går med at sukke.

Mit livsmod er brudt,

min krop sygner hen.

12Mine fjender håner mig,

mine naboer spotter mig.

Mine venner frygter mig,

de flygter, når de ser mig på gaden.

13De har afskrevet mig, som var jeg allerede død,

jeg er kasseret som en krukke, der blev knust.

14Jeg hører, hvad der hviskes i krogene,

jeg ved, jeg er omringet af fjender.

De rotter sig sammen imod mig,

de planlægger at slå mig ihjel.

15Men Herre, jeg stoler på dig.

Jeg siger: „Du er min Gud!

16Mit liv er i dine hænder.

Red mig fra alle mine fjender.

17Se i nåde til din stakkels tjener,

frels mig, min trofaste Gud.”

18Herre, lad mig ikke i stikken,

når jeg råber til dig om hjælp.

Gør det af med de onde mennesker,

lad dem synke stumme i graven.

19Sæt en stopper for deres falske anklager,

luk munden på de hovmodige løgnere,

som anklager de gudfrygtige uden grund.

20Hvor er din godhed dog stor,

du velsigner alle, der ærer dig.

Enhver kan se din nåde

over dem, der søger din hjælp.

21Du beskytter dem, der adlyder dig,

de er skærmet mod vold og overgreb.

Du holder din hånd over dem

og renser dem fra de falske anklager.

22Jeg priser dig, Herre, for din trofaste nåde.

Du reddede mig, da jeg var omringet af fjender.

23Jeg sagde i min angst,

„Herren har forladt mig.”

Men du hørte min bøn,

da jeg råbte om hjælp.

24Følg Herren, alt hans folk,

for han beskytter de lydige,

men straffer de oprørske.

25Hold ud og tab ikke modet,

I, der stoler på Herren.