Masalimo 29 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 29:1-11

Salimo 29

Salimo la Davide.

1Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,

pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

3Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;

Mulungu waulemerero abangula,

Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.

4Liwu la Yehova ndi lamphamvu;

liwu la Yehova ndi laulemerero.

5Liwu la Yehova limathyola mikungudza;

Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.

6Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,

Siriyoni ngati mwana wa njati:

7Liwu la Yehova limakantha

ngati kungʼanima kwa mphenzi.

8Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;

Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.

9Liwu la Yehova limapindapinda mibawa

ndi kuyeretsa nkhalango.

Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

10Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,

Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.

11Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;

Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 29:1-11

Lovprisning til skabningens Herre

1En sang af David.

Pris Herren, hele himlens hær,

for han har al magt og herlighed.

2Giv Herren den ære, der tilkommer ham,

kom til hans trone i tilbedelse.

3Hans røst runger over de sorte skyer,

den Almægtige tordner fra sin himmel.

4Der er styrke i hans stemme,

han taler med umådelig kraft.

5Hans stemme splintrer de største træer,

knækker Libanons stolte cedre.

6Den får Libanon og Hermon til at hoppe,

som var de kalve eller unge tyre.

7Når Herren taler,

springer lynene frem.

8Hans røst får landet til at skælve,

selv Kadeshørkenen begynder at ryste.

9Hans råb får træerne til at bøje sig,

og bladene falder til jorden.

Alle i hans helligdom råber: „Giv ære til Gud!”

10Han herskede over syndfloden,

han er Konge over alt til evig tid.

11Han styrker sit folk,

velsigner det med fred.