Salimo 28
Salimo la Davide.
1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;
musakhale osamva kwa ine.
Pakuti mukapitirira kukhala chete,
ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2Imvani kupempha chifundo kwanga
pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,
pomwe ndikukweza manja anga
kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,
pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,
amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo
koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo
ndi ntchito zawo zoyipa;
abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita
ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,
ndi zimene manja ake anazichita,
Iye adzawakhadzula
ndipo sadzawathandizanso.
6Matamando apite kwa Yehova,
popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;
mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.
Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe
ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,
linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;
mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
A Psalm of David.
1Unto thee will I cry, O LORD my rock; be not silent to me: lest, if thou be silent to me, I become like them that go down into the pit.28.1 to me: Heb. from me
2Hear the voice of my supplications, when I cry unto thee, when I lift up my hands toward thy holy oracle.28.2 thy…: or, the oracle of thy sanctuary
3Draw me not away with the wicked, and with the workers of iniquity, which speak peace to their neighbours, but mischief is in their hearts.
4Give them according to their deeds, and according to the wickedness of their endeavours: give them after the work of their hands; render to them their desert.
5Because they regard not the works of the LORD, nor the operation of his hands, he shall destroy them, and not build them up.
6Blessed be the LORD, because he hath heard the voice of my supplications.
7The LORD is my strength and my shield; my heart trusted in him, and I am helped: therefore my heart greatly rejoiceth; and with my song will I praise him.
8The LORD is their strength, and he is the saving strength of his anointed.28.8 their: or, his28.8 saving…: Heb. strength of salvations
9Save thy people, and bless thine inheritance: feed them also, and lift them up for ever.28.9 feed: or, rule