Masalimo 28 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 28:1-9

第 28 篇

祈求上帝幫助

大衛的詩。

1耶和華啊,我呼求你;

我的磐石啊,別不理我。

你若默然不語,

我必絕望而死。

2我向你呼求,

向你的至聖所舉手禱告時,

求你垂聽。

3求你不要把我與奸惡人一同責罰,

他們對鄰居口蜜腹劍。

4求你使他們罪有應得,

按他們的惡行,

按他們手上的罪惡報應他們。

5他們既然毫不在意耶和華的作為和祂的創造,

祂必永遠毀滅他們。

6耶和華當受稱頌!

因為祂聽了我的懇求。

7祂是我的力量,我的盾牌。

我信靠祂,就得幫助,

我的心歡喜雀躍,

我要歌唱讚美祂。

8耶和華是祂子民的力量,

是祂膏立者得救的堡壘。

9耶和華啊,

求你拯救你的子民,

賜福給你揀選的人,

如牧人般照顧他們,

永遠扶持他們。