Masalimo 29 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 29:1-11

Salimo 29

Salimo la Davide.

1Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,

pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

3Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;

Mulungu waulemerero abangula,

Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.

4Liwu la Yehova ndi lamphamvu;

liwu la Yehova ndi laulemerero.

5Liwu la Yehova limathyola mikungudza;

Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.

6Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,

Siriyoni ngati mwana wa njati:

7Liwu la Yehova limakantha

ngati kungʼanima kwa mphenzi.

8Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;

Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.

9Liwu la Yehova limapindapinda mibawa

ndi kuyeretsa nkhalango.

Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

10Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,

Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.

11Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;

Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 29:1-11

第 29 篇

上帝威嚴的聲音

大衛的詩。

1上帝的眾子啊,

要讚美耶和華,

讚美祂的榮耀和能力,

2要讚美祂榮耀的名,

穿上聖潔的衣服敬拜祂。

3耶和華的聲音迴盪在海上,

榮耀的上帝打雷,

在洪濤之上打雷。

4耶和華的聲音充滿能力;

耶和華的聲音充滿威嚴。

5耶和華的聲音震斷香柏樹,

耶和華劈碎黎巴嫩的香柏樹,

6使黎巴嫩山跳躍如小牛,

西連山跳躍如野牛。

7耶和華的聲音攜閃電而來,

8震動曠野,

震動加低斯的曠野。

9耶和華的聲音擊倒橡樹29·9 擊倒橡樹」或譯「使母鹿生產」。

使樹木凋零。

眾人在祂殿中高呼:

「榮耀歸於耶和華!」

10耶和華坐在洪濤之上,

耶和華永遠坐著為王。

11耶和華賜力量給自己的子民,

賜給他們平安的福樂。