Masalimo 30 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 30:1-12

Salimo 30

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.

1Ndidzakukwezani Yehova,

chifukwa mwanditulutsa kwakuya,

ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.

2Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo

ndipo Inu munandichiritsa.

3Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,

munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

4Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;

tamandani dzina lake loyera.

5Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi

koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;

utha kuchezera kulira usiku wonse,

koma chimwemwe chimabwera mmawa.

6Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,

“Sindidzagwedezekanso.”

7Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,

munachititsa phiri langa kuyima chilili;

koma pamene munabisa nkhope yanu,

ndinataya mtima.

8Kwa Inu Yehova ndinayitana;

kwa Ambuye ndinapempha chifundo;

9“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga

ngati nditsikira ku dzenje?

Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?

Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

10Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;

Yehova mukhale thandizo langa.”

11Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;

munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,

12kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 30:1-12

第 30 篇

感恩的禱告

大衛的詩,作獻殿之歌。

1耶和華啊,我要讚美你,

因為你救我脫離危難,

不讓我的仇敵幸災樂禍。

2我的上帝耶和華啊,

我呼求你,你就醫治了我。

3耶和華啊,你從陰間把我救出,

沒有讓我落入墳墓。

4耶和華忠心的子民啊,

你們要歌頌祂,

讚美祂的聖名。

5因為祂的怒氣瞬間消逝,

祂的恩惠卻持續一生。

我們雖然整夜哭泣,

早晨必定歡呼。

6我在順境中曾說:

「我永不動搖。」

7耶和華啊,

你向我施恩,我便穩固如山;

你掩面不理我,我就驚慌失措。

8耶和華啊,我向你呼求,

懇求你憐憫,說:

9「耶和華啊,

我被毀滅、落入墳墓有何益處?

我歸於塵土,還能讚美你、

宣揚你的信實嗎?

10耶和華啊,求你垂聽我的呼求,憐憫我!

耶和華啊,求你幫助我!」

11你把我的哀哭變成了舞步,

為我脫下悲傷的麻衣,

披上喜樂的外袍,

12好叫我從心底歌頌你,

不致默然無聲。

我的上帝耶和華啊,

我要永遠向你感恩!