Masalimo 25 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 25:1-22

Salimo 25

Salimo la Davide.

1Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.

2Ndimadalira Inu Mulungu wanga.

Musalole kuti ndichite manyazi

kapena kuti adani anga andipambane.

3Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye

sadzachititsidwa manyazi

koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi

ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.

4Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova,

phunzitseni mayendedwe anu;

5tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa,

pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga,

ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.

6Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu,

pakuti ndi zakalekale.

7Musakumbukire machimo a ubwana wanga

ndi makhalidwe anga owukira;

molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine,

pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.

8Yehova ndi wabwino ndi wolungama;

choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.

9Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama

ndipo amawaphunzitsa njira zake.

10Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika

kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.

11Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova,

khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.

12Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova?

Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.

13Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse,

ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.

14Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa;

amawulula pangano lake kwa iwowo.

15Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse,

pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.

16Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima,

pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.

17Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira;

masuleni ku zowawa zanga.

18Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga

ndipo mufafanize machimo anga onse.

19Onani mmene adani anga achulukira

ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.

20Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa;

musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndimathawira kwa Inu.

21Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze,

chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.

22Wombolani Israeli Inu Mulungu,

ku mavuto ake onse!

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 25:1-22

Zaburi 2525 Zaburi hii imetungwa kila mstari ukianzia na herufi ya alfabeti ya Kiebrania zikifuatana tangu Aleph (A) hadi Taw (T); zote ni 22.

Kumwomba Mungu Uongozi Na Ulinzi

Zaburi ya Daudi.

125:1 Za 86:4; 143:8Kwako wewe, Ee Bwana,

nainua nafsi yangu,

225:2 Za 31:6; 143:8ni wewe ninayekutumainia,

Ee Mungu wangu.

Usiniache niaibike,

wala usiache adui zangu wakanishinda.

325:3 Za 22:5; 2Tim 3:4; Isa 29:22; 24:16; Hab 1:13; Sef 3:4Kamwe hakuna hata mmoja anayekutegemea

atakayeaibishwa,

bali wataaibishwa

wafanyao hila bila sababu.

425:4 Ay 34:32Nionyeshe njia zako, Ee Bwana,

nifundishe mapito yako,

525:5 Za 31:3; 43:3; Yn 16:13niongoze katika kweli yako na kunifundisha,

kwa maana wewe ni Mungu Mwokozi wangu,

nalo tumaini langu liko kwako wakati wote.

625:6 Za 5:7; 98:3; Isa 63:7, 15; Yer 31:20; Hos 11:8Kumbuka, Ee Bwana, rehema zako kuu na upendo,

kwa maana zimekuwepo tangu zamani.

725:7 Ay 13:26; Isa 54:4; Yer 3:25; 31:19; 32:30; 2Tim 2:22; Eze 16:22, 60; 23:3; Za 34:8; 83:1; 107:17; 6:4; 51:1; 69:16; 109:26; 119:124; Kut 3:21; 1Nya 16:34Usizikumbuke dhambi za ujana wangu

wala njia zangu za uasi,

sawasawa na upendo wako unikumbuke,

kwa maana wewe ni mwema, Ee Bwana.

825:8 Za 32:8; 92:15; Isa 26:7; 28:26Bwana ni mwema na mwenye adili,

kwa hiyo huwafundisha wenye dhambi njia zake.

925:9 Za 23:3, 4; 18:25; 103:18; 132:12Huwaongoza wanyenyekevu katika haki,

naye huwafundisha njia yake.

1025:10 Za 18:25; 103:18; 132:12Njia zote za Bwana ni za upendo na uaminifu

kwa wale wanaoshika shuhuda za agano lake.

1125:11 Kut 9:16; Za 31:3; 79:9; 34:9; Kut 32:30; Za 78:38; Yer 14:7Ee Bwana, kwa ajili ya jina lako,

unisamehe uovu wangu, ijapokuwa ni mwingi.

1225:12 Ay 1:8Ni nani basi, mtu yule anayemcha Bwana?

Atamfundisha katika njia

atakayoichagua kwa ajili yake.

1325:13 Kum 30:15; Mt 5:5; Ay 8:7; 1Fal 3:14; Hes 14:24Mtu huyo atafanikiwa maishani mwake,

nao wazao wake watairithi nchi.

1425:14 Mit 3:32; Yn 7:17; Mwa 17:2Siri ya Bwana iko kwa wale wamchao,

yeye huwajulisha agano lake.

1525:15 2Nya 20:12; Za 119:110; 123:2; Ebr 12:2; Ay 34:30Macho yangu humwelekea Bwana daima,

kwa kuwa yeye peke yake ndiye ataitoa

miguu yangu kutoka mtego.

1625:16 Hes 6:25; Za 6:4; 68:6Nigeukie na unihurumie,

kwa maana mimi ni mpweke na mwenye kuteseka.

1725:17 1Fal 1:29; Za 6:3; 39:2; 34:6, 17; 40:12; 54:7; 116:3Shida za moyo wangu zimeongezeka,

niokoe katika dhiki yangu.

1825:18 Za 13:3; Rum 12:12; 2Sam 16:12Uangalie mateso na shida zangu

na uniondolee dhambi zangu zote.

1925:19 Za 3:1; 9:13; 69:4; 35:19Tazama adui zangu walivyo wengi,

pia uone jinsi wanavyonichukia vikali!

2025:20 Za 2:12; 86:2; 17:13; 22:21; 43:1; 71:2; 116:4; 140:1; 142:6; 144:11Uyalinde maisha yangu na uniokoe,

usiniache niaibike,

kwa maana nimekukimbilia wewe.

2125:21 Mwa 20:5; Mal 2:6; Mit 10:9; 1Fal 9:4; Za 88:10; 111:8; Isa 60:17Uadilifu na uaminifu vinilinde,

kwa sababu tumaini langu ni kwako.

2225:22 Za 103:8; Lk 24:21Ee Mungu, wakomboe Israeli,

katika shida zao zote!