Miyambo 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 1:1-33

Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu

1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:

2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;

kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;

3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,

akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.

4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,

achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.

5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,

ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,

6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,

mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.

7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.

Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Malangizo kuti Asunge Nzeru

Malangizo kwa Achinyamata

8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako

ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.

9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako

ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.

10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa

usamawamvere.

11Akadzati, “Tiye kuno;

tikabisale kuti tiphe anthu,

tikabisalire anthu osalakwa;

12tiwameze amoyo ngati manda,

ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.

13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali

ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;

14Bwera, chita nafe maere,

ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”

15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,

usatsagane nawo mʼnjira zawozo.

16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,

amathamangira kukhetsa magazi.

17Nʼkopanda phindu kutchera msampha

mbalame zikuona!

18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;

amangodzitchera okha msampha!

19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;

chumacho chimapha mwiniwake.

Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru

20Nzeru ikufuwula mu msewu,

ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;

21ikufuwula pa mphambano ya misewu,

ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,

22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?

Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?

Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?

23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.

Ine ndikukuwuzani maganizo anga

ndi kukudziwitsani mawu anga.

24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.

Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.

25Uphungu wanga munawunyoza.

Kudzudzula kwanga simunakusamale.

26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;

ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.

27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,

tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,

mavuto ndi masautso akadzakugwerani.

28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;

mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.

29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso

ndipo sanasankhe kuopa Yehova,

30popeza iwo sanasamale malangizo anga

ndipo ananyoza chidzudzulo changa.

31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo

ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.

32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,

ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.

33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;

adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mithali 1:1-33

Utangulizi: Kusudi Na Kiini

11:1 1Fal 4:29-34Mithali za Solomoni mwana wa Daudi, mfalme wa Israeli:

2Kwa kupata hekima na nidhamu;

kwa kufahamu maneno ya busara;

31:3 Mit 2:1; 2:1, 9kwa kujipatia nidhamu na busara,

kufanya lililo sawa, haki na bila kupendelea;

41:4 Mit 8:5, 12; 2:10-11huwapa busara wajinga,

maarifa na akili kwa vijana;

51:5 Mit 9:9wenye hekima na wasikilize nao waongeze elimu yao,

wenye kupambanua na wapate mwongozo;

61:6 Za 78:2; Mt 13:10-17; Hes 12:8; Amu 14:12kwa kufahamu mithali na mifano,

misemo na vitendawili vya wenye hekima.

71:7 Kut 20:20; Ay 28:28Kumcha Bwana ndicho chanzo cha maarifa,

lakini wapumbavu hudharau hekima na adabu.

Onyo Dhidi Ya Ushawishi Wa Marafiki Waovu

81:8 Mit 6:20; 22:17; Kum 21:18Mwanangu, sikiliza mwongozo wa baba yako,

wala usiyaache mafundisho ya mama yako.

91:9 Mit 3:21-22; 4:1-9Hayo yatakuwa taji la maua la neema kichwani pako,

na mkufu wa kuipamba shingo yako.

101:10 Mwa 39:7; Ay 24:15; Kum 13:8; Rum 16:18Mwanangu, kama wenye dhambi wakikushawishi,

usikubaliane nao.

111:11 Mit 12:6; Yer 5:26; Mik 7:2Kama wakisema, “Twende tufuatane;

tukamvizie mtu na kumwaga damu,

njoo tukavizie nafsi isiyo na hatia;

121:12 Ay 33:18; Mwa 38:25; Za 40:3tuwameze wakiwa hai kama kaburi,1:12 Kaburi hapa maana yake ni Kuzimu, kwa Kiebrania ni Sheol.

wakiwa wazima kama wale wanaotumbukia shimoni.

13Tutapata aina zote za vitu vya thamani

na kujaza nyumba zetu kwa nyara.

141:14 Mit 1:19Njoo ushirikiane nasi,

vitu vyote tutakavyopata tutagawana.”

151:15 Za 119:101; Mwa 49:6; Mit 4:14Mwanangu, usiandamane nao.

Usiweke mguu wako katika njia zao,

161:16 Mit 6:18; Isa 59:7kwa kuwa miguu yao hukimbilia kwenye dhambi,

ni wepesi kumwaga damu.

17Tazama ni jinsi gani ilivyo kazi bure kutandaza wavu

wakati ndege wote wanakuona!

181:18 Za 71:10Watu hawa huvizia kumwaga damu yao wenyewe;

hujivizia tu wenyewe!

191:19 Mit 11:19; 15:27; 2Fal 5:20-27Huu ndio mwisho wa wote ambao wanajipatia mali kwa hila;

huuondoa uhai wa wale wenye mali.

Onyo Dhidi Ya Kukataa Hekima

201:20 Ay 28:12; Mt 7:10-13; 9:1-3, 13-15Hekima huita kwa sauti kuu barabarani,

hupaza sauti yake kwenye viwanja vikubwa;

21kwenye makutano ya barabara za mji

zenye makelele mengi hupaza sauti,

kwenye malango ya mji hutoa hotuba yake:

221:22 Mit 6:32; 7:7; 8:5; 9:4, 16; Za 50:17“Enyi wajinga, mtangʼangʼania ujinga wenu hadi lini?

Mpaka lini wenye mizaha watafurahia mizaha,

na wapumbavu kuchukia maarifa?

231:23 Yoe 2:28; Yn 7:37Kama mngekuwa mmeitikia karipio langu,

ningekuwa nimemimina roho yangu kwenu

na kuwafahamisha maneno yangu.

241:24 Isa 65:12; Zek 7:11Lakini kwa kuwa mlinikataa nilipowaita

na hakuna yeyote aliyekubali

niliponyoosha mkono wangu,

251:25 Lk 7:30kwa kuwa mliyapuuza mashauri yangu yote

na hamkukubali karipio langu,

261:26 Za 2:4; Kum 28:63; Mit 10:24mimi nami nitawacheka katika maafa yenu,

nitawadhihaki wakati janga litawapata:

271:27 Za 18:18; Mit 5:12-14wakati janga litawapata kama tufani,

wakati maafa yatawazoa kama upepo wa kisulisuli,

wakati dhiki na taabu zitawalemea.

281:28 Isa 1:15; Mik 3:4; Eze 8:18; Hos 5:6“Ndipo watakaponiita lakini sitawajibu;

watanitafuta lakini hawatanipata.

291:29 Ay 21:14; Isa 27:11; Mdo 7:51Kwa kuwa walichukia maarifa,

wala hawakuchagua kumcha Bwana,

301:30 Ay 21:14; Za 81:11kwa kuwa hawakukubali mashauri yangu,

na kukataa maonyo yangu,

311:31 2Nya 36:16; Yer 14:16watakula matunda ya njia zao,

na watashibishwa matunda ya hila zao.

321:32 Isa 66:4; Yer 2:19Kwa kuwa ukaidi wa wajinga utawaua,

nako kuridhika kwa wajinga kutawaangamiza.

331:33 Hes 24:21; Za 25:12; 112:8Lakini yeyote anisikilizaye ataishi kwa usalama,

atatulia, bila kuwa na hofu ya madhara.”