Masalimo 16 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 16:1-11

Salimo 16

Mikitamu ya Davide.

1Ndisungeni Inu Mulungu,

pakuti ine ndimathawira kwa Inu.

2Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;

popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”

3Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,

amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.

4Anthu amene amathamangira kwa milungu ina

mavuto awo adzachulukadi.

Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi

kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.

5Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;

mwateteza kolimba gawo langa.

6Malire a malo anga akhala pabwino;

ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.

7Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;

ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.

8Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.

Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,

sindidzagwedezeka.

9Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;

thupi langanso lidzakhala pabwino,

10chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,

simudzalola kuti woyera wanu avunde.

11Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;

mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,

ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

O Livro

Salmos 16:1-11

Salmo 16

Salmo de David. Poema de instrução.

1Guarda-me, ó Deus,

porque em ti me refugio.

2Eu disse ao Senhor:

“Tu és o meu Senhor,

não tenho outra riqueza além de ti.”

3Quero a companhia do povo santo nesta terra;

eles são a verdadeira nobreza.

4Terão muito a sofrer,

todos esses que prestam culto a outros deuses.

Quanto a mim, nunca hei de oferecer desses sacrifícios,

nem sequer pronunciarei o nome dos seus deuses.

5O Senhor é a minha herança e a minha recompensa;

tu guardas tudo o que me pertence.

6Faz com que a parte que me toca, nesta vida, seja deliciosa.

Sim, ele é como uma herança maravilhosa!

7Louvarei o Senhor que sempre me tem aconselhado;

até durante a noite ele me ensina o que devo fazer.

8Tenho posto o Senhor continuamente diante de mim;

visto que ele está ao meu lado, não serei movido.

9Portanto, o meu coração está alegre

e a minha alma está satisfeita;

o meu corpo repousará em segurança.

10Pois não deixarás a minha alma no mundo dos mortos,

nem permitirás que o teu santo conheça a corrupção.

11Dás-me a conhecer o caminho da vida

e as abundantes alegrias que há na tua presença.

A vida ao teu lado é um gozo permanente!