Masalimo 15 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 15:1-5

Salimo 15

Salimo la Davide.

1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?

Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

2Munthu wa makhalidwe abwino,

amene amachita zolungama,

woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,

3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,

amene sachitira choyipa mnansi wake

kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,

4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.

Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,

amene amakwaniritsa zomwe walonjeza

ngakhale pamene zikumupweteka,

5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja

ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi

sadzagwedezeka konse.

O Livro

Salmos 15:1-5

Salmo 15

Salmo de David.

1Senhor, quem pode achar refúgio no teu tabernáculo

e ficar contigo no teu santo monte?

2Certamente aquele que anda em retidão,

que pratica a justiça e que fala verdade.

3Aquele que não calunia os outros,

que respeita o próximo

e não dá ouvidos à maledicência.

4Aquele que sabe censurar quem pratica o pecado,

mas que honra os que temem o Senhor;

também aquele que cumpre as promessa que faz;

ainda que fique prejudicado, nada o fará mudar de ideias.

5Aquele que ajuda os pobres,

sem esperar pesados serviços em recompensa;

que recusa receber subornos contra o inocente.

Quem assim procede permanecerá firme para sempre.