Masalimo 17 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 17:1-15

Salimo 17

Pemphero la Davide.

1Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;

mverani kulira kwanga.

Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa

popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.

2Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;

maso anu aone chimene ndi cholungama.

3Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,

ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;

Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.

4Kunena za ntchito za anthu,

monga mwa mawu a pakamwa panu,

Ine ndadzisunga ndekha

posatsata njira zachiwawa.

5Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;

mapazi anga sanaterereke.

6Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;

tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.

7Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,

Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja

iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.

8Mundisunge ine ngati mwanadiso;

mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,

9kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine,

kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

10Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo,

ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.

11Andisaka, tsopano andizungulira

ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.

12Iwo ali ngati mkango wofuna nyama;

ngati mkango waukulu wokhala mobisala.

13Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi;

landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.

14Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere,

kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno.

Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu;

ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri,

ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.

15Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;

pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

O Livro

Salmos 17:1-15

Salmo 17

Oração de David.

1Senhor, aplica a tua justiça na minha vida;

atende à súplica que te dirijo.

Dá ouvidos à minha oração,

pois é feita com toda a sinceridade.

2Publica a tua sentença a meu favor;

dá-me razão, Senhor.

3Tu me puseste à prova,

até durante a noite me tens examinado,

e não tens encontrado nada de falso;

estou decidido a não pecar nas minhas palavras.

4Tenho seguido as tuas palavras;

tenho-me guardado de homens cruéis e violentos.

5Dirige os meus passos nos teus caminhos,

para que nunca vacile.

6Se te chamei, ó Deus,

é porque sei que me queres ouvir;

escuta-me e dá ouvidos às palavras da minha oração.

7Mostra-me as maravilhas do teu amor.

Tu livras os que em ti se refugiam,

daqueles que são teus inimigos

e que se revoltam contra ti.

8Guarda-me como se fosse a menina do teu olho;

esconde-me, à sombra das tuas asas,

dos homens maus que me oprimem,

9Defende-me dos perversos que me oprimem,

dos que andam à minha volta para me matar.

10Andam inchados de orgulho;

só sabem falar com altivez.

11Espiam os meus passos,

observam-me cuidadosamente,

para me lançar ao chão, assim que puderem.

12São como leões desejosos de se lançar sobre a presa;

como leõezinhos que se escondem,

esperando a oportunidade.

13Senhor, levanta-te e fá-los parar;

livra a minha alma dessa gente perversa,

livra-me pela tua espada.

14Salva-me desta gente mundana,

cujos interesses estão só nos lucros desta vida.

Tu enches de bens materiais aqueles que amas,

fartas os seus filhos e os filhos dos seus filhos.

15Pela tua justiça, verei a tua face;

quando acordar,

ficarei satisfeito com a visão da tua presença!