Masalimo 125 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 125:1-5

Salimo 125

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,

limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2Monga mapiri azungulira Yerusalemu,

momwemonso Yehova azungulira anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala

pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,

kuti anthu olungamawo

angachite nawonso zoyipa.

4Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,

amene ndi olungama mtima

5Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 125:1-5

Tryghed hos Herren

1En valfartssang.

De, der stoler på Herren,

står fast som Zions bjerg.

I evighed rokkes de ikke.

2Som bjergene omslutter Jerusalem,

vil Herren altid omslutte sit folk.

3Onde konger skal ikke herske for evigt

over det land, Gud gav de gudfrygtige,

for ellers ville de glemme deres gudsfrygt.

4Herre, vis godhed mod de gode,

de, som har et oprigtigt hjerte.

5Men de, som slår ind på ondskabens vej,

vil Herren jage bort sammen med de onde.

Fred være med Israel!