Masalimo 112 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 112:1-10

Salimo 112

1Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,

amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;

mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;

wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,

amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

6Ndithu sadzagwedezeka;

munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;

mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.

8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;

potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;

nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;

adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.

Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

Persian Contemporary Bible

مزامير 112:1-10

خوشبختی درستكاران

1خداوند را سپاس باد!

خوشا به حال كسی كه از خداوند می‌ترسد و احكام او را با رغبت انجام می‌دهد. 2فرزندان شخص درستكار در دنيا نيرومند خواهند شد و نسل او بركت خواهند يافت. 3خانواده‌اش صاحب مال و ثروت خواهد شد و خوبی‌های او هرگز از ياد نخواهد رفت.

4برای كسی كه درستكار و بخشنده، مهربان و نيكوكار است، حتی در تاريكی شب نيز نور طلوع می‌كند. 5خوشبخت است كسی كه دلسوز و قرض دهنده باشد و در كسب و كارش با انصاف باشد. 6او در زندگی پيوسته ثابت قدم و پايدار خواهد بود و نام نيكش هميشه در يادها باقی خواهد ماند.

7او از شنيدن خبر بد نمی‌ترسد، زيرا ايمان او قوی است و بر خداوند توكل دارد. 8او نگران نمی‌شود و نمی‌ترسد زيرا مطمئن است كه شكست دشمنانش را خواهد ديد. 9با سخاوتمندی به فقيران می‌بخشد؛ اثرات نيكوكاری او تا ابد باقی می‌ماند و هميشه نزد مردم سربلند و محترم می‌باشد. 10بدكاران اين را می‌بينند و خشمگين می‌شوند؛ دندانهای خود را به هم می‌فشارند و همراه آرزوهايشان از بين می‌روند.