Masalimo 111 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

Persian Contemporary Bible

مزامير 111:1-10

خداوند را سپاس باد!

1خداوند را با تمام دل خود در ميان قوم او ستايش خواهم كرد.

2كارهای خداوند چه شگفت‌انگيزند! همهٔ كسانی كه به آنها علاقمند هستند در باره‌شان می‌انديشند. 3كارهای خداوند شكوهمند است و عدالتش جاودانی! 4كارهای شگفت‌انگيز خداوند، فراموش نشدنی است! او رحيم و بخشنده است! 5خداوند، روزی ترسندگان خود را می‌رساند، او هرگز عهد خود را از ياد نمی‌برد. 6خداوند سرزمينهای قومهای بيگانه را به بنی‌اسرائيل بخشيد و به اين وسيله قدرتش را به قوم خود نشان داد.

7هر كاری كه خداوند انجام می‌دهد، درست و منصفانه است. همهٔ احكام او قابل اعتماد می‌باشند. 8كارها و احكام خداوند تا ابد باقی می‌مانند، زيرا بر عدل و راستی بنا شده‌اند. 9او با دادن فديه، قوم خود را آزاد كرده است و با آنها عهد ابدی بسته است. او مقدس و قدرتمند است.

10انسان چگونه خردمند می‌شود؟ خداترسی نخستين گام در اين راه است. خداوند به همهٔ كسانی كه دستوراتش را اجرا می‌كنند، خرد می‌بخشد.

خداوند را تا ابد سپاس باد.