Masalimo 110 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 110:1-7

Salimo 110

Salimo la Davide.

1Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,

“Khala ku dzanja langa lamanja

mpaka nditasandutsa adani ako

kukhala chopondapo mapazi ako.”

2Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;

udzalamulira pakati pa adani ako.

3Ankhondo ako adzakhala odzipereka

pa tsiku lako la nkhondo.

Atavala chiyero chaulemerero,

kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,

udzalandira mame a unyamata wako.

4Yehova walumbira

ndipo sadzasintha maganizo ake:

“Ndiwe wansembe mpaka muyaya

monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

5Ambuye ali kudzanja lako lamanja;

Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.

6Adzaweruza anthu a mitundu ina,

adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.

7Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;

choncho adzaweramutsa mutu wake.

Korean Living Bible

시편 110:1-7

메시아의 통치에 대한 선언

(다윗의 시)

1여호와께서 나의 주님에게 말씀하셨다.

“내가 네 원수들을

110:1 또는 ‘네 발등상이 되게 하기까지’네 발 앞에 굴복시킬 때까지

너는 내 오른편에 앉아 있거라.”

2여호와께서 시온에서부터

주의 110:2 또는 ‘권능의 홀을’능력의 지팡이를

뻗치실 것입니다.

주는 주의 원수들을 다스리소서.

3주의 능력의 날에

주의 백성이 거룩한 옷을 입고

자진해서 주께 나아갈 것입니다. 그들은 새벽 이슬 같은

주의 청년들입니다.

4여호와께서 약속하셨으니

그 마음을 바꾸지 않으시리라.

“너는 110:4 또는 ‘멜기세덱의 반차를 좇아’멜기세덱의 계열에 속한

영원한 제사장이다.”

5여호와께서는 주님의

오른편에 계십니다.

그가 분노하시는 날에

세상의 왕들을

쳐서 죽이실 것입니다.

6그가 모든 나라를 심판하여

시체를 산더미처럼 쌓고

온 세상의 통치자들을

쳐서 죽이실 것이다.

7그가 길가의 시냇물을 마시고

힘을 얻어 110:7 또는 ‘그 머리를 드시리로다’의기 양양하리라.