Masalimo 109 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 109:1-31

Salimo 109

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mulungu amene ndimakutamandani,

musakhale chete,

2pakuti anthu oyipa ndi achinyengo

atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane;

iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.

3Andizungulira ndi mawu audani,

amandinena popanda chifukwa.

4Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,

koma ine ndine munthu wapemphero.

5Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,

ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.

6Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;

lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.

7Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,

ndipo mapemphero ake amutsutse.

8Masiku ake akhale owerengeka;

munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.

9Ana ake akhale amasiye

ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.

10Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;

apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.

11Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;

alendo afunkhe ntchito za manja ake.

12Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima

kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.

13Zidzukulu zake zithe nʼkufa,

mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.

14Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;

tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.

15Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,

kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.

16Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,

koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka

ndi osweka mtima.

17Anakonda kutemberera,

matembererowo abwerere kwa iye;

sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena,

choncho madalitso akhale kutali naye.

18Anavala kutemberera ngati chovala;

kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi,

kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.

19Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,

ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.

20Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,

kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.

21Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

muchite nane molingana ndi dzina lanu,

chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.

22Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,

ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.

23Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,

ndapirikitsidwa ngati dzombe.

24Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,

thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.

25Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;

akandiona, amapukusa mitu yawo.

26Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;

pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.

27Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,

kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.

28Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;

pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi,

koma mtumiki wanu adzasangalala.

29Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,

ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.

30Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;

ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.

31Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,

kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

Korean Living Bible

시편 109:1-31

원수를 벌해 달라는 기도

(다윗의 시. 성가대 지휘자를 따라 부른 노래)

1내 찬송의 하나님이시여,

잠잠하지 마소서.

2악한 자들이 나를 헐뜯고

나에 대하여 거짓말을 하며

3이유 없이 나를

미워하고 공격합니다.

4나는 그들을 사랑하고

그들을 위해 기도하는데도

그들은 나를 대적합니다.

5그들이 선을 악으로,

사랑을 증오로 갚고 있습니다.

6109:6 또는 ‘악인으로’악한 재판관을 택하여

내 원수를 재판하게 하시고

109:6 히 ‘사탄’고소자를

그의 오른편에 서게 하소서.

7그가 재판을 받을 때에

유죄 선고를 받게 하시고

그의 기도도 죄가 되게 하소서.

8그의 사는 날을 짧게 하시며

그의 직분을

다른 사람이 갖게 하소서.

9그의 자녀들은 고아가 되고

그의 아내는 과부가 되게 하시며

10그 자녀들이 집 없이 떠돌아다니고

구걸하는 신세가 되게 하소서.

11빚쟁이가 그의 재산을 몰수하고

낯선 사람이

그가 수고하여 얻은 것을

약탈하게 하시며

12그에게 친절을 베푸는 자도

없게 하소서.

고아가 된 그의 자녀들에게

동정을 베푸는 자가 없게 하시고

13그의 후손이 끊어지게 하시며

다음 세대에 그의 이름이

사라지게 하소서.

14여호와여,

109:14 또는 ‘열조의’아버지의 죄를 기억하시며

그 어머니의 죄를 용서하지 마시고

15그들의 죄악을 항상 생각하시며

지상에서 그들에 대한 기억이

사라지게 하소서.

16그는 다른 사람에게

친절을 베풀지 않았고

가난하고 힘없는 자와

마음이 상한 자를

핍박하고 죽였습니다.

17그가 남을 저주하기 좋아하였으니

이제 그 저주가 자기에게

돌아가게 하소서.

그는 다른 사람에게 축복하기를

기뻐하지 않았습니다.

복이 그를 떠나게 하소서.

18그는 저주하기를

옷 입듯이 하였습니다.

이제 그 저주가 물처럼

그의 몸 속에

들어가게 하시고

기름처럼 그의 뼛속에

들어가게 하소서.

19그 저주가

입고 다니는 옷과 같게 하시고

항상 두르고 다니는

띠와 같게 하소서.

20여호와여, 이것이

나를 대적하며 악담하는

내 원수들이 받는 벌이 되게 하소서.

21그러나 주 여호와여,

주의 이름을 위하여 나를 도우시고

주의 인자한 사랑으로

나를 건지소서.

22나는 가난하고 궁색하며

마음에 상처를 입었습니다.

23내가 저녁 그림자처럼 사라져가고

메뚜기처럼 날려갑니다.

24내가 금식하다가 무릎이

쇠약해졌고

내 몸은 뼈와 가죽만

남았습니다.

25사람들이 나를 보면

비웃고 조롱하며 머리를 흔듭니다.

26여호와 나의 하나님이시여,

나를 도우시고

주의 한결같은 사랑으로

나를 구원하소서.

27주께서 나를 구하시는 분이심을

내 원수들이 알게 하소서.

28그들이 나를 저주하지마는

주는 나를 축복하실 것입니다.

그들이 나를 칠 때

수치를 당할 것이나

주의 종은 기뻐할 것입니다.

29내 원수들은 옷 입듯이

항상 모욕과 수치를

당하게 하소서.

30내가 큰 소리로

여호와께 감사하며

많은 군중 가운데서

그를 찬양하리라.

31여호와는 가난한 사람의

오른편에 서서

그를 죄인으로 몰아

죽이려는 자들에게서

그의 생명을 구하신다.