Masalimo 108 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 108:1-13

Salimo 108

Nyimbo. Salimo la Davide.

1Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;

ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.

2Dzukani, zeze ndi pangwe!

Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.

3Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.

4Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;

kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.

5Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,

ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

6Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

7Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.

9Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo

ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;

ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

11Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana

ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?

12Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,

pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.

13Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,

ndipo adzapondereza pansi adani athu.

Korean Living Bible

시편 108:1-13

승리에 대한 확신

(다윗의 찬송시)

1하나님이시여,

내가 마음에

확신을 가지게 되었으므로

영혼으로 노래하며

주를 찬양하겠습니다.

2비파야, 수금아, 깨어라!

내가 새벽을 깨우리라.

3여호와여, 내가 많은 나라 가운데서

주께 감사하며

많은 민족 가운데서

주를 찬양하겠습니다.

4주의 사랑은 너무나 커서

하늘보다 높고

주의 성실하심은 창공에 이릅니다.

5하나님이시여, 주의 위대하심을

하늘에 보이시고

주의 영광을 온 세상에 나타내소서.

6주의 능력으로 우리를 구원하시고

우리 기도에 응답하셔서

주께서 사랑하시는 자들이

구출되게 하소서.

7하나님이 108:7 또는 ‘그 거룩하심으로’그의 성소에서

말씀하셨다.

“내가 의기 양양하게 세겜을 나누고

숙곳 골짜기를 측량하리라.

8길르앗이 내 것이요

므낫세도 내 것이며

에브라임은 내 머리의 투구요

유다는 나의 다스리는 지팡이이며

9모압은 나의 목욕통이다.

내가 에돔에게 내 신발을 던지고

블레셋에게

의기 양양하게 외치리라.”

10누가 나를

요새화된 성으로 데리고 가며

누가 나를 에돔으로 인도할까?

11하나님이시여, 주께서 정말

우리를 버리셨습니까?

이제는 주께서 우리 군대와

함께 나아가지 않을 작정이십니까?

12우리를 도와 대적을 치게 하소서.

사람의 도움은 쓸모가 없습니다.

13하나님이 우리와 함께하시면

우리가 승리할 것이니

그가 우리 대적을 짓밟을 것임이라.