Marko 7 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 7:1-37

Miyambo ya Makolo ya Ayuda

1Afarisi ndi ena mwa aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anasonkhana momuzungulira Yesu ndipo 2iwo anaona ophunzira ake akudya chakudya ndi mʼmanja mwakuda kapena kuti mʼmanja mosasamba. 3(Afarisi ndi Ayuda onse sadya pokhapokha atasamba mʼmanja, kusunga mwambo wa makolo awo. 4Akabwera kuchokera ku msika samadya pokhapokha atasamba. Ndipo amasunga miyambo ina yambiri monga, kutsuka zikho, mitsuko ndi maketulo).

5Choncho Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anafunsa Yesu kuti, “Nʼchifukwa chiyani ophunzira anu satsatira mwambo wa makolo, mʼmalo mwake amangodya chakudya ndi mʼmanja mwakuda?”

6Iye anayankha kuti, “Yesaya ananena zoona pamene ananenera za inu achiphamaso; monga kunalembedwa kuti:

“Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

7Amandilambira Ine kwachabe;

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.

8Mwasiya malamulo a Mulungu ndipo mwagwiritsitsa miyambo ya anthu.”

9Ndipo anawawuzanso kuti, “Inu muli ndi njira yabwino yokankhira kumbali malamulo a Mulungu kuti mukatsatire miyambo yanuyo! 10Pakuti Mose anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako,’ ndipo, ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 11Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukanayenera kulandira kuchokera kwa ine ndi Korobani’ (kutanthauza kuti, mphatso yoperekedwa kwa Mulungu), 12pamenepo inu simumalola kuti achitire kanthu kalikonse abambo kapena amayi ake. 13Potero mumachepetsa mawu a Mulungu kukhala wopanda mphamvu ndi miyambo yanu imene mumapatsirana. Ndipo mumachita zinthu zina zambiri monga zimenezi.”

14Yesu anayitananso gulu la anthu ndipo anati, “Tandimverani nonsenu, ndipo zindikirani izi. 15Palibe kanthu kunja kwa munthu kamene kakalowa mwa iye kangamusandutse wodetsedwa. Koma zimene zituluka mwa munthu ndizo zimupanga kukhala wodetsedwa.” 16(Ngati wina ali ndi makutu akumva amve).

17Atalisiya gulu la anthu ndi kulowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa za fanizoli 18Iye anawafunsa kuti, “Kodi nanunso simumvetsetsa? Kodi simukuona kuti palibe kanthu kamene kakalowa mwa munthu kochokera kunja kakhoza kumudetsa? 19Pakuti sikalowa mu mtima wake koma mʼmimba mwake, ndipo kenaka kamatuluka kunja.” (Ndi mawu amenewa, Yesu anayeretsa zakudya zonse).

20Anapitiriza kuti, “Chimene chichokera mwa munthu ndi chomwe chimamudetsa. 21Pakuti kuchokera mʼkati mwa mitima ya anthu, mumatuluka maganizo oyipa, chiwerewere, kuba, kupha, chigololo, 22dyera, nkhwidzi, chinyengo, machitidwe onyansa, kaduka, chipongwe, kudzikuza ndi kupusa. 23Zoyipa zonsezi zimatuluka mʼkati ndipo zimadetsa munthu.”

Chikhulupiriro cha Mayi wa ku Siriya Fonisia

24Yesu anachoka kumalo amenewo napita ku madera a Turo. Iye analowa mʼnyumba ndipo sanafune wina kuti adziwe zimenezi; komabe sanathe kudzibisa. 25Kunena zoona, amayi amene kamwana kawo kakakazi kanali kogwidwa ndi mzimu woyipa, atangomva za Iye, anabwera nagwada pa mapazi ake. 26Mayiyu anali Mhelene, wobadwira ku Fonisia wa ku Siriya. Anamupempha Yesu kuti atulutse chiwanda mwa mwana wake.

27Iye anamuwuza kuti, “Choyamba asiye ana adye zimene akuzifuna, pakuti si kwabwino kutenga buledi wa ana ndi kuponyera agalu awo.”

28Mayiyo anayankha kuti, “Inde Ambuye, koma ngakhale agalu amadya zomwe zimagwa pansi kuchokera pa tebulo la ana.”

29Ndipo Iye anamuwuza kuti, “Chifukwa cha yankholi, ukhoza kupita; chiwanda chachoka mwa mwana wako wamkazi.”

30Atapita kwawo anakapeza mwana wake aligone pa bedi, chiwanda chitatuluka.

Kuchiritsidwa kwa Munthu Wosamva ndi Wosayankhula

31Ndipo Yesu anachoka ku dera la Turo nadutsa pakati pa Sidoni, kutsikira ku nyanja ya Galileya kupita ku dera la Dekapoli. 32Kumeneko anthu ena anabweretsa kwa Iye munthu amene anali wosamva ndi wosayankhula, ndipo anamupempha kuti asanjike dzanja pa iye.

33Atamutengera iye pambali, patali ndi gulu la anthu, Yesu analowetsa zala zake mʼmakutu a munthuyo. Kenaka anapaka malovu pachala ndi kukhudza lilime la munthuyo. 34Iye anayangʼana kumwamba ndipo ndi mawu otsitsa moyo, anati kwa iye, “Efataa!” (Kutanthauza kuti, “Tsekuka!”) 35Atachita izi, makutu a munthuyo anatsekuka komanso lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula momveka bwino.

36Yesu anawalamula kuti asawuze wina aliyense. Koma pamene anapitiriza kuwaletsa, iwo anapitiriza kuyankhula za izi. 37Anthu anadabwa kwambiri. Iwo anati, “Wachita zonse bwino, ngakhale Iyenso atsekula makutu a osamva ndi osayankhula kuti ayankhule.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬可福音 7:1-37

傳統與誡命

1有法利賽人和一些律法教師從耶路撒冷來見耶穌。 2他們看到祂的門徒有些吃飯前沒有照禮儀洗手。 3因為法利賽人和所有的猶太人都拘守古人的傳統,總是先照禮儀洗手之後才吃飯; 4從市場回來也要先潔淨自己,然後才吃飯。他們還拘守許多其他規矩,如洗杯、罐、銅器等。

5他們質問耶穌:「為什麼你的門徒違背祖先的傳統,竟用不潔淨的手吃飯呢?」

6耶穌回答說:「以賽亞先知針對你們這些偽君子所說的預言一點不錯,正如聖經上說,

『這些人嘴上尊崇我,

心卻遠離我。

7他們的教導無非是人的規條,

他們敬拜我也是枉然。』

8你們只知拘守人的傳統,卻無視上帝的誡命。」 9耶穌又對他們說:「你們為了拘守自己的傳統,竟巧妙地廢除了上帝的誡命。 10摩西說,『要孝敬父母』,又說,『咒罵父母的,必被處死。』 11你們卻認為人若對父母說,『我把供養你們的錢財已經全部奉獻給上帝了』, 12他就可以不奉養父母。 13你們就是這樣為了拘守傳統而廢除上帝的道,類似的情形還有很多。」

內心的污穢

14耶穌又召集眾人,教導他們說:「我的話,你們要聽明白, 15從外面進去的不會使人污穢,只有從人裡面發出來的才會使人污穢。 16有耳可聽的,都應當聽!」

17耶穌離開眾人,進了屋子,門徒問祂這比喻的意思。 18耶穌說:「你們也不明白嗎?你們不知道嗎?從外面進去的,不會使人污穢, 19因為不能進入他的心,只能進他的腸胃,最後會排出來,也就是說所有的食物都是潔淨的。 20從人裡面發出來的才使人污穢, 21因為從裡面,就是從人的心裡能夠生出惡念、苟合、偷盜、謀殺、 22通姦、貪婪、邪惡、詭詐、放蕩、嫉妒、毀謗、驕傲、狂妄。 23這一切惡事都是從裡面生出來的,能使人污穢。」

外族婦人的信心

24耶穌從那裡啟程去泰爾西頓地區。祂進了一戶人家,原本不想讓人知道,卻無法避開人們的注意。 25-26當時有一個婦人的小女兒被污鬼附身,她聽見耶穌的事,就來俯伏在祂腳前,懇求祂趕出她女兒身上的鬼。這婦人是希臘人,來自敘利亞腓尼基

27耶穌對她說:「要先讓兒女們吃飽,因為把兒女的食物丟給狗吃不合適。」

28婦人說:「主啊,你說的對,但桌子下的狗也吃孩子們掉下來的碎渣呀!」

29耶穌說:「因為你這句話,你回去吧,鬼已經離開你的女兒了。」

30她回到家裡,見女兒躺在床上,鬼已經離開了。

醫治聾啞的人

31耶穌離開泰爾地區,經過西頓,來到低加坡里地區的加利利湖。 32有人帶著一個又聾又啞的人來見耶穌,懇求祂把手按在這個人身上。 33耶穌就帶他離開眾人走到一邊,用指頭伸進他的耳朵,又吐唾沫抹他的舌頭, 34望天長歎,對他說:「以法大!」意思是「開了吧!」 35他的耳朵立刻開了,舌頭靈活了,說話也清楚了。 36耶穌吩咐他們不要將這事告訴人。可是耶穌越是這樣吩咐,他們越是極力宣揚, 37聽見的人都十分驚奇,說:「祂做的事好極了,甚至叫聾子聽見,啞巴說話!」