Marko 15 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 15:1-47

Yesu ku Bwalo la Pilato

1Mmamawa, akulu a ansembe pamodzi ndi akuluakulu, aphunzitsi amalamulo ndi olamulira onse anamanga fundo. Anamumanga Yesu, namutenga ndi kukamupereka kwa Pilato.

2Pilato anafunsa kuti, “Kodi Iwe ndi Mfumu ya Ayuda?”

Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”

3Akulu a ansembe anamunenera zinthu zambiri. 4Ndipo Pilato anamufunsanso Iye kuti, “Kodi Iwe suyankhapo kanthu? Tamva zinthu zambiri akukunenerazi.”

5Koma Yesu sanayankhebe, ndipo Pilato anadabwa.

6Pa nthawi ya Phwando, panali chizolowezi chomasula munthu wamʼndende amene anthu amupempha. 7Munthu wotchedwa Baraba anali mʼndende pamodzi ndi anthu owukira amene anapha anthu pa nthawi ya chipolowe. 8Gulu la anthu linabwera kwa Pilato ndi kumufunsa kuti awachitire zimene amachita nthawi zonse.

9“Kodi mukufuna kuti ndikumasulireni mfumu ya Ayuda?” Pilato anafunsa, 10podziwa kuti akulu a ansembe anamupereka Yesu kwa iye chifukwa cha nsanje. 11Koma akulu a ansembe anasonkhezera anthu kuti Pilato amasule Baraba mʼmalo mwa Yesu.

12Pilato anawafunsa kuti, “Kodi nanga ndichite chiyani ndi uyu amene mukumutcha mfumu ya Ayuda?”

13Anafuwula kuti, “Mpachikeni!”

14Pilato anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani? Wapalamula mlandu wotani?”

Koma anafuwula kwambiri, “Mpachikeni!”

15Pilato pofuna kuwakondweretsa anthuwo, anawamasulira Baraba. Analamula kuti Yesu akwapulidwe mwankhanza, ndipo anamupereka kuti akapachikidwe.

Chipongwe cha Asilikali

16Asilikali anamutenga Yesu ndi kupita naye mʼkati mwa nyumba yaufumu (dera lokhalako asilikali a mfumu) ndipo anasonkhanitsa gulu lonse la asilikali. 17Anamuveka Iye mwinjiro wofiira, kenaka analuka chipewa cha minga ndi kuyika pa mutu pake. 18Ndipo anayamba kunena kwa lye kuti, “Ulemu kwa inu Mfumu ya Ayuda!” 19Ndipo anamugogoda pa mutu mobwerezabwereza ndi ndodo ndi kumulavulira. Anamugwadira ndi kumulambira Iye. 20Ndipo anamuchita chipongwe, anamuvula mwinjiro wofiira uja ndi kumuveka zovala zake. Kenaka anamutenga kuti akamupachike.

Yesu Apachikidwa pa Mtanda

21Munthu wina ochokera ku Kurene, Simoni, abambo a Alekisanda ndi Rufasi amadutsa kuchokera ku dziko la kwawo, ndipo anamuwumiriza kuti anyamule mtanda. 22Anafika naye Yesu pa malo otchedwa Gologota (kutanthauza kuti, malo a bade) 23Kenaka anamupatsa Iye vinyo wosakaniza ndi mure, koma Iye sanamwe. 24Ndipo anamupachika Iye. Anachita maere ogawana zovala zake kuti aone chimene aliyense angatenge.

25Linali ora lachitatu mmawa pamene anamupachika Yesu. 26Chikwangwani cholembedwapo mlandu wake chinali choti: mfumu ya ayuda. 27Achifwamba awiri anapachikidwanso pamodzi ndi Iye, wina kumanja kwake ndi wina kumanzere kwake. 28(Ndipo malemba anakwaniritsidwa amene amati, “Iye anayikidwa mʼgulu la anthu oyipa).” 29Amene amadutsa pafupi anamunenera mawu amwano, akupukusa mitu yawo ndi kuti, “Haa! Iwe amene udzawononga Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso masiku atatu, 30tsika kuchoka pa mtandapo ndipo udzipulumutse wekha!”

31Chimodzimodzinso akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamunyoza Iye pakati pawo. Iwo anati, “Anapulumutsa ena, koma sangathe kudzipulumutsa yekha! 32Musiyeni Khristu, Mfumu ya Aisraeli, atsike tsopano kuchoka pa mtanda, kuti ife tione ndi kukhulupirira.” Iwonso amene anapachikidwa naye pamodzi anamulalatira.

Imfa ya Yesu

33Pa ora lachisanu ndi chimodzi masana mdima unabwera pa dziko lonse mpaka pa ora lachisanu ndi chinayi masana. 34Pa ora lachisanu ndi chinayi Yesu analira mofuwula kuti, “Eloi, Eloi, lama sabakitani?” Kutanthauza kuti, “Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?”

35Ena amene anali pafupi atamva izi anati, “Tamverani, akuyitana Eliya.”

36Munthu wina anathamanga, natenga chinkhupule atachiviyika mu vinyo wosasa, anachizika ku mtengo, ndi kumupatsa Yesu kuti amwe. Munthuyo anati, “Musiyeni yekha tsopano. Tiyeni tione ngati Eliya angabwere kudzamutsitsa.”

37Ndi mawu ofuwula, Yesu anapuma komaliza.

38Chinsalu chotchinga cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati kuyambira pamwamba mpaka pansi. 39Ndipo Kenturiyo, amene anayima patsogolo pa Yesu, atamva kulira kwake ndi kuona mmene anafera anati, “Zoonadi, uyu anali Mwana wa Mulungu.”

40Amayi ena anali patali kuonerera. Pakati pawo panali Mariya Magadalena, Mariya amayi a Yakobo wamngʼono ndi Yose ndi Salome. 41Amayi awa ankamutsatira Iye mu Galileya ndi kumutumikira Iye pa zosowa zake. Amayi enanso ambiri amene anabwera naye ku Yerusalemu analinso pomwepo.

Yesu Ayikidwa Mʼmanda

42Linali Tsiku Lokonzekera (kunena kuti, tsiku lomwe limatsatizana ndi Sabata). Choncho madzulo atayandikira, 43Yosefe wa ku Arimateyu, mkulu wolamulira odziwika bwino, amene amadikirira ufumu wa Mulungu, anapita kwa Pilato molimba mtima ndi kukapempha mtembo wa Yesu. 44Pilato anadabwa pakumva kuti anali atamwalira kale. Anayitana Kenturiyo, namufunsa ngati Yesu anali atamwalira kale. 45Atawuzidwa ndi Kenturiyo kuti zinali motero, anapereka mtembowo kwa Yosefe. 46Choncho Yosefe anagula nsalu yabafuta, natsitsa thupi, ndipo analikulunga mʼnsalu, naliyika mʼmanda amene anawagoba pa mwala. Kenaka anagubuduza mwala umene anatseka nawo mandawo. 47Mariya Magadalena ndi Mariya amayi a Yose anaona kumene anamuyika Yesu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

马可福音 15:1-47

耶稣在彼拉多面前受审

1清早,祭司长、长老、律法教师和全公会的人商定后,便把耶稣绑起来押送到彼拉多那里。

2彼拉多问耶稣:“你是犹太人的王吗?”

耶稣回答说:“如你所言。”

3祭司长控告耶稣许多罪。

4彼拉多又问道:“你看,他们控告你这么多,你都不回答吗?”

5耶稣仍旧一言不发,彼拉多感到惊奇。

6每年逾越节的时候,彼拉多都会照惯例按犹太人的要求释放一个囚犯。 7那时,有一个囚犯名叫巴拉巴,与其他作乱时杀过人的囚犯关在一起。 8百姓聚来,要求彼拉多照惯例释放囚犯。

9彼拉多问:“你们要我为你们释放犹太人的王吗?” 10因为他知道祭司长把耶稣押来是出于妒忌。 11但祭司长却煽动百姓,叫他们要求彼拉多释放巴拉巴

12彼拉多只好问:“那么,这位你们称之为犹太人之王的,我如何处置呢?”

13他们喊着说:“把祂钉在十字架上!”

14彼拉多问:“为什么?祂犯了什么罪?”

他们却更大声地喊:“把祂钉在十字架上!”

15为了取悦众人,彼拉多释放了巴拉巴,命人将耶稣鞭打后带出去钉十字架。

耶稣受辱

16于是,卫兵把耶稣带进总督府的院子,集合了全营的兵。 17他们给祂穿上紫袍,用荆棘编成王冠戴在祂头上, 18向祂行礼,并喊着说:“犹太人的王万岁!” 19他们用苇秆打祂的头,向祂吐唾沫,跪拜祂。 20戏弄完了,就脱去祂的紫袍,给祂穿上原来的衣服,押祂出去钉十字架。

钉十字架

21亚历山大鲁孚的父亲古利奈西门从乡下来,途经那地方,卫兵就强迫他背耶稣的十字架。 22他们把耶稣带到各各他——意思是“髑髅地”, 23拿没药调和的酒给祂喝,但祂不肯喝。 24他们把耶稣钉在十字架上,还抽签分祂的衣服。 25他们钉祂十字架的时间是在上午九点钟。 26祂的罪状牌上写着“犹太人的王”。

27他们还把两个强盗钉在十字架上,一个在祂右边,一个在祂左边, 28这应验了圣经的话:“祂被列在罪犯中。” 29过路的人都嘲笑祂,摇着头说:“哈,你这要把圣殿拆毁又在三天内重建的人啊, 30救救你自己,从十字架上下来吧!”

31祭司长和律法教师也嘲讽说:“祂救了别人,却救不了自己! 32以色列的王基督,现在从十字架上下来吧!让我们看看,我们就信了!”与祂同钉十字架的强盗也对祂出言不逊。

耶稣之死

33正午时分,黑暗笼罩着整个大地,一直到下午三点。 34大约在三点,耶稣大声呼喊:“以罗伊,以罗伊,拉马撒巴各大尼?”意思是:“我的上帝,我的上帝,你为什么离弃我?”

35有些站在旁边的人听见了,就说:“听,祂在呼叫以利亚。”

36有人跑去把一块海绵蘸满酸酒,绑在苇秆上送给祂喝,说:“等等,让我们看看以利亚会不会救祂下来。”

37耶稣大叫一声,就断了气。 38圣殿的幔子从上到下裂成两半。 39站在对面的百夫长看见耶稣喊叫15:39 有些古卷无“喊叫”二字。断气的情形,便说:“这人真是上帝的儿子!”

40有些妇女在远处观看,其中有抹大拉玛丽亚、小雅各约西的母亲玛丽亚撒罗米41耶稣在加利利时,她们已经跟随祂、服侍祂了。此外还有好些跟着祂上耶路撒冷的妇女。

安葬耶稣

42那天是犹太人的预备日,也就是安息日的前一天。傍晚, 43亚利马太约瑟鼓起勇气去见彼拉多,要求领取耶稣的遗体。他是一位德高望重的公会议员,一位等候上帝国降临的人。 44彼拉多听见耶稣已经死了,十分惊讶,便把百夫长召来问个明白, 45得知耶稣确实已死,便将耶稣的遗体交给约瑟

46约瑟把耶稣的遗体取下来,用买来的细麻布裹好,安放在一个在岩壁上凿出的墓穴里,又滚来一块大石头堵住洞口。 47抹大拉玛丽亚约西的母亲玛丽亚都亲眼看到了安葬耶稣的地方。