Marko 14 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 14:1-72

Yesu Adzozedwa ku Betaniya

1Tsopano panali patatsala masiku awiri okha kuti tsiku la Paska ndi Phwando la Buledi wopanda yisiti lifike, ndipo akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ankafunafuna mpata woti amugwire Yesu ndi kumupha. 2Iwo anati, “Koma osati nthawi yaphwando, chifukwa anthu angachite chiwawa.”

3Pamene Iye anali mʼBetaniya, atakhala pa tebulo akudya mʼnyumba ya munthu wodziwika kuti Simoni wakhate, anabwera mayi ndi botolo la mafuta onunkhira amtengo wapamwamba opangidwa ndi nadi. Anaphwanya botololo nakhuthula mafutawo pa mutu wa Yesu.

4Ena mwa iwo amene analipo, anakwiya nati kwa wina ndi mnzake, “Chifukwa chiyani akuwononga mafuta onunkhirawa? 5Akanatheka kugulitsidwa ndi ndalama zambiri zoposa malipiro a pa chaka ndipo ndalamazo ndi kupatsa osauka.” Ndipo anamudzudzula iye mwaukali.

6Yesu anati, “Musiyeni, chifukwa chiyani mukumuvutitsa? Wandichitira Ine chinthu chabwino. 7Anthu osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, ndipo mukhoza kuwathandiza nthawi iliyonse mungafune. Koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse. 8Wachita zimene akanatha. Wathira mafuta onunkhira pa thupi langa nthawi isanakwane kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda. 9Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse, zimene wachitazi zidzanenedwa pomukumbukira iye.”

10Kenaka Yudasi Isikarioti, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anapita kwa akulu a ansembe kuti akamupereke Yesu. 11Iwo anakondwa pakumva zimenezi ndipo analonjeza kumupatsa iye ndalama. Ndipo ankadikira mpata wabwino woti amupereke.

Mgonero wa Ambuye

12Pa tsiku loyamba la Phwando la Buledi wopanda yisiti, nthawi imene mwa mwambo inali ya kupha mwana wankhosa wa Paska, ophunzira a Yesu anafunsa Iye kuti, “Mufuna tipite kuti kumene tikakonzekere kuti mukadyere Paska?”

13Pamenepo anatumiza awiri mwa ophunzira ake, nawawuza kuti, “Pitani mu mzinda, ndipo mukakumana ndi mwamuna wonyamula mtsuko wa madzi. Kamutsatireni iye. 14Kawuzeni mwini nyumba imene iye akalowemo kuti, ‘Aphunzitsi akufunsa: kodi chili kuti chipinda changa cha alendo, kumene ndidyere Paska ndi ophunzira anga?’ 15Iye adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala kale ndi zonse ndi chokonzedwa kale. Katikonzereni ife Paska kumeneko.”

16Ophunzirawo anachoka, napita mu mzindawo ndipo anakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Choncho anakakonza Paska.

17Ndipo kutada Yesu anafika ndi khumi ndi awiriwo. 18Pamene ankadya pa tebulo Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka, mmodzi amene akudya ndi Ine.”

19Iwo anamva chisoni, ndipo mmodzi ndi mmodzi anati kwa Iye, “Kodi ndine?”

20Iye anayankha kuti, “Ndi mmodzi mwa khumi ndi awirinu, amene akusunsa buledi mʼmbale pamodzi ndi Ine. 21Mwana wa Munthu adzapita monga momwe zinalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene adzapereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”

22Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, ili ndi thupi langa.”

23Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo.

24Iye anawawuza kuti, “Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri. 25Zoonadi, ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mphesa mpaka tsikulo pamene ndidzamwa chatsopano mu ufumu wa Mulungu.”

26Atayimba nyimbo, anapita ku phiri la Olivi.

Yesu Aneneratu zakuti Petro Adzamukana

27Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa:

“ ‘Kantha Mʼbusa,

ndipo nkhosa zidzabalalika.’

28Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”

29Petro anati, “Ngakhale onse adzakuthaweni, ine sindidzatero.”

30Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”

31Koma Petro ananenetsa kuti, “Ngakhale kutakhala kufa nanu, ine sindidzakukanani.” Ndipo ena onse ananena chimodzimodzi.

Mu Getsemani

32Ndipo anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Khalani pano pamene Ine ndi kupemphera.” 33Iye anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane, ndipo anayamba kumva chisoni kwambiri ndi kuvutika mu mtima. 34Iye anawawuza kuti, “Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo musagone.”

35Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi ndi kupemphera kuti ngati ndi kotheka oralo limupitirire. 36Iye anati, “Abba, Atate, zinthu zonse ndi zotheka ndi Inu. Chotsereni chikhochi. Komabe chitani zimene Inu mukufuna, osati zimene Ine ndikufuna.”

37Kenaka anabwerera kwa ophunzira ake ndipo anawapeza akugona, Iye anati kwa Petro, “Simoni, kodi uli mtulo? Kodi simukanatha kukhala maso kwa ora limodzi? 38Khalani tcheru ndi kupemphera kuti musalowe mʼmayesero. Mzimu ukufuna, koma thupi ndi lofowoka.”

39Kenakanso anachoka ndi kukapemphera chimodzimodzi. 40Iye atabwerera, anawapezanso akugona, chifukwa mʼmaso mwawo munadzaza tulo. Iwo sanadziwe choti anene kwa Iye.

41Atabweranso kachitatu, anawafunsa kuti, “Kodi mukugonabe ndi kupumula? Pakwana! Nthawi yafika. Taonani, Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa. 42Nyamukani! Tiyeni tizipita! Uyu wondipereka Ine wafika!”

Amugwira Yesu

43Iye akuyankhulabe, Yudasi, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anatulukira. Anali ndi gulu la anthu litanyamula malupanga ndi zibonga, otumidwa ndi akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo, ndi akuluakulu.

44Tsopano womupereka anapangana chizindikiro ndi iwo kuti: “Amene ndikapsompsone ndi iyeyo; mukamugwire ndi kumutenga ali womangidwa.” 45Atapita kwa Yesu nthawi yomweyo, Yudasi anati, “Aphunzitsi,” ndipo anapsompsona. 46Anthu anamugwira Yesu ndi kumumanga. 47Kenaka mmodzi wa iwo amene anayima pafupipo anatulutsa lupanga lake nakhapa wantchito wa wamkulu wa ansembe, nʼkudula khutu lake.

48Yesu anati, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira, kuti mubwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? 49Tsiku ndi tsiku ndinali ndi inu, kuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, koma inu simunandigwire. Koma malemba ayenera kukwaniritsidwa.” 50Pamenepo ophunzira ake onse anathawa namusiya yekha.

51Mnyamata wamngʼono amene anangofundira nsalu yokha, wopanda chovala ankamutsatira Yesu. Atamugwira, 52anathawa wamaliseche kusiya nsalu yake mʼmbuyo.

Yesu ku Bwalo la Milandu

53Anamutengera Yesu kwa mkulu wa ansembe, ndipo akulu a ansembe, akuluakulu ndi aphunzitsi amalamulo anasonkhana pamodzi. 54Petro anamutsatira ali patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Kumeneko anakhala pansi ndi alonda namawotha moto.

55Akulu a ansembe ndi onse olamulira a Ayuda ankafunafuna umboni womutsutsa Yesu kuti amuphe, koma sanapeze wina uliwonse. 56Ambiri anamunenera Iye maumboni abodza, koma maumboni awo sanagwirizane.

57Kenaka ena anayimirira namunenera umboni wonama womutsutsa Iye kunena kuti, 58“Tamumva akunena kuti, ‘Ndidzawononga Nyumba ya Mulungu iyi yopangidwa ndi anthu ndipo mʼmasiku atatu ndidzamanga ina, osati yopangidwa ndi munthu.’ ” 59Ngakhale iwonso umboni wawo sunagwirizane.

60Kenaka mkulu wa ansembe anayimirira pakati pawo namufunsa Yesu kuti, “Kodi suyankha? Kodi umboni uwu ndi wotani umene anthu akukuchitira?” 61Koma Yesu anakhala chete ndipo sanayankhe.

Mkulu wa ansembe anabwereza kumufunsa Iye kuti, “Kodi ndiwe Khristu Mwana wa Wodalitsikayo?”

62Yesu anati, “Ndine, ndipo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera mʼmitambo ya kumwamba.”

63Mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zaunsembe zake. Iye anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani tikufuna mboni zinanso? 64Mwamva mwanowo. Muganiza chiyani?”

Onse anavomereza kuti ndi woyenera imfa. 65Kenaka ena anayamba kumulavulira malovu; anamumanga mʼmaso, namumenya ndi zibakera ndipo anati, “Nenera!” Ndipo asilikali anamutenga namumenya.

Petro Akana Yesu

66Petro ali chakumunsi kwa bwalo la milandu, mmodzi wa atsikana a ntchito a mkulu wa ansembe anabwera. 67Ataona Petro akuwotha moto, anamuyangʼanitsitsa.

Iye anati, “Iwenso unali pamodzi ndi Mnazareti, Yesu.”

68Koma iye anakana nati, “Sindikudziwa kapena kumvetsetsa zimene ukuyankhula.” Ndipo anachoka napita ku chipata.

69Pamene mtsikana wantchitoyo anamuona iye, anatinso kwa iwo amene anayimirira pomwepo, “Munthu uyu ndi mmodzi mwa iwo.” 70Anakananso kachiwiri.

Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pafupi anati kwa Petro, “Zoonadi ndiwe mmodzi wa iwo, pakuti ndiwe mu Galileya.”

71Iye anayamba kudzitemberera, nalumbira kuti, “Sindimudziwa munthu ameneyu.”

72Nthawi yomweyo tambala analira kachiwiri. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Yesu ananena anamuwuza kuti, “Tambala asanalire kawiri, iwe udzandikana katatu.” Ndipo iye anasweka mtima nayamba kulira.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

马可福音 14:1-72

谋害耶稣

1再过两天就是逾越节和除酵节,祭司长和律法教师正暗暗地找机会拘捕、杀害耶稣。

2他们说:“我们不能在节期那天下手,以免在百姓中引起骚乱。”

耶稣受膏

3耶稣在伯大尼村患过麻风病的西门家里吃饭,有个女人带了一瓶极贵重的纯哪哒香膏进来,把玉瓶打破,将香膏倒在耶稣头上。 4有些人生气地彼此议论说:“为什么这样浪费? 5这瓶香膏可以卖三百多个银币14:5 三百多个银币”相当于当时人们一年的工钱。来周济穷人。”他们就责备那女人。

6耶稣说:“随她吧!何必为难她呢?她在我身上做的是一件美事。 7因为你们身边总会有穷人,你们随时都可以帮助他们,可是你们身边不会总有我。 8她做了自己能做的。她是为我的安葬做准备,提前用香膏抹了我的身体。 9我实在告诉你们,无论福音传到世界哪个角落,人们都会传扬这女人的事迹,纪念她。”

犹大出卖耶稣

10十二门徒当中的加略犹大去见祭司长,要把耶稣出卖给他们。 11他们听了喜出望外,答应给他酬金。于是犹大伺机出卖耶稣。

最后的晚餐

12除酵节的第一天,就是宰杀逾越节羔羊的那天,门徒问耶稣:“我们该到什么地方为你准备逾越节的晚餐呢?”

13耶稣就派了两个门徒,并嘱咐他们:“你们进城会看到一个人带着一瓶水迎面而来,你们就跟着他。 14他进哪一家,你们也跟着进去,对那家的主人说,‘我们的老师问你,祂的客房在哪里,祂要和门徒在里面吃逾越节的晚餐。’ 15主人会带你们到楼上一间布置整齐的大房间,你们就在那里准备吧。”

16两个门徒出去,进了城,所遇见的果然和耶稣所说的一样。他们预备了逾越节的晚餐。

17傍晚时分,耶稣带着十二门徒来了。 18用餐的时候,耶稣说:“我实在告诉你们,你们中间有一个人要出卖我,他现在正和我同桌吃饭。”

19他们听了都感到不安,一个一个地问耶稣:“不是我吧?” 20耶稣说:“是你们十二个人中的一个,他现在正和我一起在盘子里蘸饼吃。 21人子一定会受害,正如圣经的记载,但出卖人子的人有祸了,他还不如不生在这世上!”

22他们吃的时候,耶稣拿起饼来,祝谢后,便掰开,分给门徒,说:“拿去吃吧!这是我的身体。” 23接着又拿起杯来,祝谢后,递给他们,他们都喝了。 24耶稣说:“这是我为万人所流的立约之血。 25我实在告诉你们,从今天起,一直到我在上帝的国喝新酒的那天之前,我不会再喝这葡萄酒。”

26他们唱完诗歌,就出门去了橄榄山。

预言彼得不认主

27耶稣对他们说:“你们都要背弃我,因为圣经上说,

“‘我要击打牧人,

羊群将四散。’

28但我复活后,要先你们一步去加利利。”

29彼得说:“即使所有人都背弃你,我也决不会背弃你!”

30耶稣说:“我实在告诉你,就在今天晚上鸡叫两次以前,你会三次不认我。”

31彼得郑重地说:“就算要我跟你一起死,我也不会不认你。”其他门徒也都这样说。

客西马尼园的祷告

32他们到了客西马尼园,耶稣对门徒说:“你们坐在这里,我要去祷告。”

33于是耶稣带着彼得雅各约翰向前走。祂觉得极其难过,非常伤痛, 34说:“我心里非常忧伤,几乎要死,你们留在这里警醒。” 35耶稣往前走了不远,俯伏在地祷告,如果可以,不要让那时刻临到祂。

36祂说:“阿爸,父啊,你无所不能,求你撤去此杯。然而,愿你的旨意成就,而非我的意愿。”

37祂回来,见他们都睡着了,就对彼得说:“西门,你在睡觉吗?你不能警醒一时吗? 38你们要警醒祷告,免得陷入诱惑。你们的心灵虽然愿意,肉体却很软弱。”

39耶稣又去祷告,所祈求的跟上次一样。 40祂回来时见他们又睡着了,因为他们困得眼皮发沉,也不知道对祂说什么。 41祂第三次祷告回来后,对他们说:“你们还在睡觉休息吗?够了,时候到了,看啊,人子要被出卖、交在罪人的手里了。 42起来,我们走吧。看啊,出卖我的人已经来了!”

耶稣被捕

43耶稣还在说话的时候,十二门徒之一的犹大已带了一群人拿着刀棍迎面而来。他们奉了祭司长、律法教师和长老之命来捉拿耶稣。 44出卖耶稣的犹大预先和他们定了暗号,说:“我亲吻谁,谁就是耶稣,你们把祂抓起来,小心押走。”

45犹大随即走到耶稣跟前说:“老师。”然后就亲吻耶稣。 46其他人就下手捉拿耶稣。 47站在旁边的一个门徒拔出刀朝大祭司的奴仆砍去,削掉了他一只耳朵。

48耶稣问那群人:“你们像对付强盗一样拿着刀棍来抓我吗? 49我天天和你们在一起,在圣殿里教导人,你们没有来抓我。你们现在这样做是要应验圣经的话。”

50那时,门徒都撇下耶稣,各自逃命去了。 51只有一个身上披着一块麻布的青年跟着耶稣。他们上去捉他, 52他丢了那块麻布,赤身逃走了。

大祭司审问耶稣

53他们把耶稣押到大祭司那里,众祭司长、长老和律法教师都来了。 54那时彼得远远地跟着耶稣,一直来到大祭司的院子,与卫兵们坐在一起烤火。 55祭司长和全公会的人正在寻找证据控告耶稣,要定祂死罪,只是找不到。 56不少人作伪证控告祂,他们的证词却不一致。 57后来,有几个人站起来作伪证说: 58“我们听见祂说,‘我要拆毁这座人手建造的圣殿,三天内不靠人力另造一座。’” 59即使这样,他们的证词也不一致。

60最后,大祭司在众人面前站起来质问耶稣:“你不回答吗?这些人作证控告你的是什么呢?”

61耶稣还是沉默不语,什么也不答。大祭司又问祂:“你是那当受称颂者的儿子基督吗?” 62耶稣说:“我是!将来你们要看见人子坐在全能上帝的右边,驾着天上的云降临。”

63大祭司便撕裂衣服,说:“我们还需要什么证人呢? 64你们听见祂说亵渎的话了,你们看怎么办?”他们都判祂死罪。

65有几个人向祂吐唾沫,蒙上祂的眼睛,挥拳打祂,嘲笑祂说:“你说预言吧!”卫兵押祂下去时,也打祂。

彼得三次不认耶稣

66那时,彼得仍在院子里,大祭司的一个婢女走过来, 67彼得在烤火,打量了他一番,说:“你也是那个拿撒勒人耶稣的同伙。”

68“我不知道也不明白你在说什么!”彼得一边否认,一边躲到外院去。那时,鸡叫了。

69一会儿,那婢女又看见彼得,就对旁边的人说:“他是跟他们一伙的!” 70彼得又加以否认。

再过了一会儿,旁观的人也指着彼得说:“你一定是跟他们一伙的,因为你也是加利利人!”

71彼得又赌咒又发誓,说:“我根本不认识你们说的这个人。” 72就在这时候,鸡又叫了。彼得突然想起耶稣曾对他说:“在鸡叫两次以前,你会三次不认我”,忍不住痛哭起来。