1Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
popondapo mapazi ake.
2Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
maufumu ndi akalonga ake.
3Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5Ambuye ali ngati mdani;
wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
mfumu ndi wansembe.
7Ambuye wakana guwa lake la nsembe
ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8Yehova anatsimikiza kugwetsa
makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
onse anawonongeka pamodzi.
9Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
aweramitsa mitu yawo pansi.
11Maso anga atopa ndi kulira,
ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
mʼmisewu ya mu mzinda.
12Anawo akufunsa amayi awo kuti,
“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
mʼmanja mwa amayi awo.
13Ndinganene chiyani za iwe?
Ndingakufanizire ndi chiyani,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
kuti ndikutonthoze,
iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
kodi ndani angakuchiritse?
14Masomphenya a aneneri ako
anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
anali achabechabe ndi osocheretsa.
15Onse oyenda mʼnjira yako
akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
wokongola kotheratu,
chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
tili ndi moyo kuti tilione.”
17Yehova wachita chimene anakonzeratu;
wakwaniritsa mawu ake,
amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
wakweza mphamvu za adani ako.
18Mitima ya anthu
ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
misozi yako itsike ngati mtsinje
usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19Dzuka, fuwula usiku,
pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
mʼmalo opatulika a Ambuye?
21Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
mwawapha mopanda chifundo.
22Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
1چگونه خداوند اورشليم را با ابر خشم و غضب خويش پوشانيد و جلال آسمانی اسرائيل را تباه كرد. او در روز خشم خود، حتی خانهٔ خويش را به ياد نياورد.
2خداوند به خانههای اسرائيل رحم نكرد و تمام آنها را ويران نمود. او قلعههای اورشليم را در هم شكست و اسرائيل را با تمام بزرگانش بیحرمت نمود.
3او به هنگام خشم خود حاكمان اسرائيل را نابود كرد و هنگام حملهٔ دشمن از قوم خود حمايت ننمود. آتش خشم او سراسر خاک اسرائيل را به نابودی كشاند.
4او مانند يک دشمن، تير و كمانش را به سوی ما نشانه گرفت و جوانان برومند ما را كشت. او خشم خود را همچون شعلهٔ آتش بر خيمههای اورشليم فرود آورد.
5بلی، خداوند همچون يک دشمن، اسرائيل را هلاک كرد و قصرها و قلعههايش را ويران نمود و بر غم و غصهٔ ساكنان يهودا افزود.
6او خانهٔ خود را كه محل عبادت بود ويران نموده است و ديگر كسی روزهای «سَبَت» و عيدهای مقدس را گرامی نمیدارد. او در شدت خشم خويش پادشاهان و كاهنان را خوار نموده است.
7خداوند قربانگاه خود را واگذارد و خانهٔ خويش را ترک گفت. ديوارهای قصرهای اورشليم را به دست دشمن داد تا خراب كنند. اينک دشمن در خانهٔ خدا كه زمانی در آن عبادت میكرديم، فرياد شادی و پيروزی سر میدهد.
8خداوند قصد نمود حصارهای اورشليم را در هم بكوبد. او شهر را اندازهگيری كرد تا هيچ قسمتش از خرابی در امان نماند؛ و اينک برجها و حصارهای اورشليم فرو ريختهاند.
9دروازههای اورشليم به زمين افتادهاند و پشتبندهايشان شكستهاند. پادشاهان و بزرگان اسرائيل به سرزمینهای دور دست تبعيد شدهاند. ديگر شريعت خدا تعليم داده نمیشود و انبیا نيز از جانب خداوند رؤيا نمیبينند.
10ريشسفيدان اورشليم پلاس بر تن كرده، خاموش بر زمين نشستهاند و از شدت غم بر سر خود خاک میريزند. دختران جوان اورشليم از شرم سر خود را به زير میافكنند.
11چشمانم از گريه تار شده است. از ديدن مصيبتی كه بر سر قومم آمده، غمی جانكاه وجودم را فرا گرفته است. كودكان و شيرخوارگان در كوچههای شهر از حال رفتهاند.
12آنها مانند مجروحان جنگی در كوچهها افتادهاند؛ گرسنه و تشنه، مادران خود را میخوانند و در آغوش ايشان جان میدهند.
13ای اورشليم، غم تو را با غم چه كسی میتوانم مقايسه كنم؟ چه بگويم و چگونه تو را دلداری دهم؟ زخم تو همچون دريا عميق است. چه كسی میتواند شفايت دهد؟
14انبيايت به دروغ برای تو نبوت كردند و گناهانت را به تو نشان ندادند. آنها با دادن پيامهای دروغ تو را فريب دادند و باعث اسارتت شدند.
15اينک هر رهگذری كه از كنارت میگذرد با استهزا سر خود را تكان داده میگويد: «آيا اين است آن شهری كه به زيباترين و محبوبترين شهر دنيا معروف بود!»
16تمام دشمنانت تو را مسخره میكنند و با نفرت میگويند: «بالاخره نابودش كرديم! انتظار چنين روزی را میكشيديم و آن را با چشمان خود ديديم.»
17اما اين كار، كار خداوند بود. او آنچه را سالها پيش فرموده بود انجام داد. همانگونه كه بارها اخطار كرده بود، به اورشليم رحم نكرد و آن را از بين برد و باعث شد دشمنانش از خرابی شهر شاد شوند و به قدرتشان ببالند.
18ای مردم اورشليم در حضور خداوند گريه كنيد؛ ای ديوارهای اورشليم، شب و روز همچون سيل، اشک بريزيد و چشمان خود را از گريستن بازمداريد.
19شب هنگام برخيزيد و نالههای دل خود را همچون آب در حضور خداوند بريزيد! دستهای خود را به سوی او بلند كنيد و برای فرزندانتان كه در كوچهها از گرسنگی میميرند، التماس نماييد!
20خداوندا، اين قوم تو هستند كه آنها را به چنين بلايی دچار كردهای. ببين چگونه مادران كودكانشان را كه در آغوش خود پروردهاند، میخورند؛ و كاهنان و انبیا در خانه خداوند كشته میشوند.
21ببين چگونه پير و جوان، دختر و پسر، به شمشير دشمن كشته شده و در كوچهها افتادهاند. تو در روز غضبت بر ايشان رحم نكردی و ايشان را كشتی.
22ای خداوند، تو دشمنانم را بر من فراخواندی و آنها از هر سو مرا به وحشت انداختند. در آن روز غضبت، كسی جان به در نبرد، تمام فرزندانم كه آنها را در آغوش خود پرورده بودم به دست دشمنانم كشته شدند.