Yeremiya 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 1:1-19

1Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. 2Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. 3Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

4Yehova anayankhula nane kuti,

5“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,

iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;

ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

6Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

7Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. 8Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

9Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu

polowera pa zipata za Yerusalemu;

iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake

ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.

16Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo

chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.

Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,

ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

Persian Contemporary Bible

ارميا 1:1-19

1اين كتاب شامل پيامهايی است كه خدا به اِرميا پسر حلقيا داد. ارميا يكی از كاهنان شهر عناتوت (واقع در سرزمين بنيامين) بود. 2نخستين پيام، در سال سيزدهم سلطنت يوشيا (پسر آمون)، پادشاه يهودا، بر ارميا نازل شد. 3پيامهای ديگری نيز در دورهٔ سلطنت يهوياقيم (پسر يوشيا) تا يازدهمين سال پادشاهی صدقيا (پسر يوشيا)، بر او نازل شد. در ماه پنجم همين سال بود كه اورشليم به تصرف درآمد و اهالی شهر اسير و تبعيد شدند.

دعوت ارميا

4‏-5خداوند به من فرمود: «پيش از آنكه در رحم مادرت شكل بگيری تو را انتخاب كردم. پيش از اينكه چشم به جهان بگشايی، تو را برگزيدم و تعيين كردم تا در ميان مردم جهان پيام‌آور من باشی.»

6اما من گفتم: «خداوندا، اين كار از من ساخته نيست! من جوانی كم سن و بی‌تجربه هستم!»

7خداوند فرمود: «چنين مگو! چون به هر جايی كه تو را بفرستم، خواهی رفت و هر چه به تو بگويم، خواهی گفت. 8از مردم نترس، زيرا من با تو هستم و از تو محافظت می‌كنم.»

9آنگاه دست بر لبهايم گذارد و گفت: «اينک كلام خود را در دهانت گذاشتم! 10از امروز رسالت تو آغاز می‌شود! تو بايد به قومها و حكومتها هشدار دهی و بگويی كه من برخی از ايشان را ريشه‌كن كرده، از بين خواهم برد و برخی ديگر را پا برجا نگاه داشته، تقويت خواهم كرد.»

دو رؤيا

11سپس فرمود: «ارميا، نگاه كن! چه می‌بينی؟»

گفتم: «شاخه‌ای از درخت بادام!»

12فرمود: «چنين است! و اين بدان معناست كه مراقب خواهم بود تا هر آنچه گفته‌ام، انجام شود1‏:12 در عبری واژه‌های «مراقب بودن» و «بادام» شبيه يکديگرند.‏

13بار ديگر خداوند از من پرسيد: «حالا چه می‌بينی؟»

جواب دادم: «يک ديگ آب جوش كه از سوی شمال بر اين سرزمين فرو می‌ريزد.»

14فرمود: «آری، بلايی از سوی شمال بر تمام اهالی اين سرزمين نازل خواهد شد. 15من سپاهيان مملكتهای شمالی را فرا خواهم خواند تا به اورشليم آمده تخت فرمانروايی خود را كنار دروازه‌های شهر بر پا دارند و همهٔ حصارهای آن و ساير شهرهای يهودا را تسخير كنند. 16اينست مجازات قوم من به سبب شرارتهايشان! آنها مرا ترک گفته، خدايان ديگر را می‌پرستند و در برابر بتهايی كه خود ساخته‌اند، سجده می‌كنند.

17«حال، برخيز و آماده شو و آنچه كه من می‌گويم به ايشان بگو. از آنها مترس و گرنه كاری می‌كنم كه در برابر آنها آشفته و هراسان شوی! 18امروز تو را در برابر آنها همچون شهری حصاردار و ستونی آهنين و ديواری برنجين، مقاوم می‌سازم تا در برابر تمام افراد اين سرزمين بايستی، در برابر پادشاهان يهودا، بزرگان، كاهنان و همهٔ مردم. 19آنها با تو به ستيز برخواهند خاست، اما كاری از پيش نخواهند برد، چون من، خداوند، با تو هستم و تو را رهايی خواهم داد.»