1Ine ndine munthu amene ndaona masautso
ndi ndodo ya ukali wake.
2Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa
mu mdima osati mʼkuwala;
3zoonadi anandikantha ndi dzanja lake
mobwerezabwereza tsiku lonse.
4Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,
ndipo waphwanya mafupa anga.
5Wandizinga ndi kundizungulira
ndi zowawa ndi zolemetsa.
6Wandikhazika mu mdima
ngati amene anafa kale.
7Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,
wandimanga ndi maunyolo.
8Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,
amakana pemphero langa.
9Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;
ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10Wandidikirira ngati chimbalangondo,
wandibisalira ngati mkango.
11Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,
ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12Wakoka uta wake
ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13Walasa mtima wanga
ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;
amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15Wandidyetsa zowawa
ndipo wandimwetsa ndulu.
16Wathyola mano anga ndi miyala;
wandiviviniza mʼfumbi;
17Wandichotsera mtendere;
ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka
ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,
zili ngati zowawa ndi ndulu.
20Ine ndikuzikumbukira bwino izi,
ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21Komabe ndimakumbukira zimenezi,
nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,
ndi chifundo chake ndi chosatha.
23Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;
kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;
motero ndimamuyembekezera.”
25Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,
kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha
Yehova modekha.
27Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli
pamene ali wamngʼono.
28Akhale chete pa yekha,
chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29Abise nkhope yake mʼfumbi
mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,
ndipo amuchititse manyazi.
31Chifukwa Ambuye satayiratu
anthu nthawi zonse.
32Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,
chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33Pakuti sabweretsa masautso mwadala,
kapena zowawa kwa ana a anthu.
34Kuphwanya ndi phazi
a mʼndende onse a mʼdziko,
35kukaniza munthu ufulu wake
pamaso pa Wammwambamwamba,
36kumana munthu chiweruzo cholungama—
kodi Ambuye saona zonsezi?
37Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika
ngati Ambuye sanavomereze?
38Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka
mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula
akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,
ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu
kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42“Ife tachimwa ndi kuwukira
ndipo inu simunakhululuke.
43“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo
mwatitha mopanda chifundo.
44Mwadzikuta mu mtambo
kotero mapemphero athu sakukufikani.
45Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala
pakati pa mitundu ya anthu.
46“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,
tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe
chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49Misozi idzatsika kosalekeza,
ndipo sidzasiya,
50mpaka Yehova ayangʼane pansi
kuchokera kumwamba ndi kuona.
51Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi
chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52Akundisaka ngati mbalame,
amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje
ndi kundiponya miyala;
54madzi anamiza mutu wanga
ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,
kuchokera mʼdzenje lozama.
56Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere
kulira kwanga kopempha thandizo.”
57Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,
ndipo munati, “Usaope.”
58Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;
munapulumutsa moyo wanga.
59Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.
Mundiweruzire ndinu!
60Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,
chiwembu chawo chonse pa ine.
61Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,
chiwembu chawo chonse pa ine,
62manongʼonongʼo a adani anga
ondiwukira ine tsiku lonse.
63Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,
akundinyoza mu nyimbo zawo.
64Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,
chifukwa cha zimene manja awo achita.
65Phimbani mitima yawo,
ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66Muwalondole mwaukali ndipo
muwawonongeretu pa dziko lapansi.
1من كسی هستم كه از خشم و غضب خدا مصیبتها ديدهام. 2خدا مرا به اعماق تاريكی كشانده است. 3او بر ضد من برخاسته و دستش تمام روز بر من بلند است.
4او پوست بدنم را فرسوده و استخوانهايم را شكسته است. 5جان مرا با تلخی و مشقت پوشانده است. 6مرا مانند كسی كه سالهاست مرده، در تاريكی نشانده است.
7با زنجيرهای سنگين مرا بسته و دورم را حصار كشيده است تا نتوانم فرار كنم. 8فرياد برمیآورم و كمک میطلبم، ولی او به دادم نمیرسد. 9با ديوارهای سنگی راه مرا بسته است و طريق مرا پر پيچ و خم نموده است.
10او در كمين من نشست و مانند شير بر من هجوم آورد؛ 11مرا به ميان بيشه كشانيد و پارهپارهام كرد و تنها و بیكس رهايم ساخت. 12او كمانش را كشيد و مرا هدف قرار داد، 13و تيرهايش به اعماق قلبم فرو رفت.
14مردم تمام روز به من میخندند و مرا مسخره میكنند.
15او زندگی را به كامم تلخ كرده است. 16صورتم را به خاک ماليده است و دهانم را از سنگريزه پر كرده و دندانهايم را شكسته است. 17سلامتی و خوشبختی از من رخت بربسته است. 18رمق و اميدی برايم نمانده، زيرا خداوند مرا ترک گفته است. 19وقتی مصيبت و سرگردانی خود را به ياد میآورم، جانم تلخ میگردد. 20بلی، آنها را دائم به ياد میآورم و وجودم پريشان میشود.
21اما نور اميدی بر قلبم میتابد، وقتی به ياد میآورم كه 22رحمت خداوند بیزوال است. آری، به سبب محبت اوست كه ما تلف نشدهايم. 23وفاداری خدا عظيم است و رحمت او هر صبح بر ما میتابد. 24به خود میگويم: «من فقط خداوند را دارم، پس به او اميد خواهم بست.» 25خداوند برای كسانی كه به او توكل دارند و او را میطلبند نيكوست. 26پس خوبست كه چشم اميدمان به او باشد و با صبر منتظر باشيم تا خداوند ما را نجات دهد. 27خوبست انسان در جوانی بياموزد كه سختيها را تحمل كند. 28هنگامی كه او دچار مصيبت میگردد بهتر آنست كه در سكوت و تنهايی بنشيند 29و در برابر خداوند سر تعظيم فرود آورد، زيرا ممكن است اميدی باشد. 30وقتی او را میزنند و اهانت میكنند خوبست آنها را تحمل كند، 31زيرا خداوند تا ابد او را ترک نخواهد كرد. 32هر چند خدا كسی را اندوهگين كند، اما رحمتش شامل حال او خواهد شد، زيرا محبت او عظيم است. 33او از آزردن و غمگين ساختن انسان خشنود نمیگردد.
34هنگامی كه ستمديدگان جهان زير پا له میشوند، 35و زمانی كه حق انسانی كه خدای متعال آن را به وی داده است، پايمال میگردد، 36و هنگامی كه مظلومی در دادگاه محكوم میشود، آيا خداوند اينها را نمیبيند؟ 37آيا بدون اجازهٔ خداوند هيچ امری واقع میشود؟ 38آيا هم مصيبت و هم بركت از جانب خدای متعال نازل نمیشود؟
39پس چرا وقتی ما انسانهای فانی به سبب گناهانمان تنبيه میشويم، گله و شكايت میكنيم؟ 40به جای گله و شكايت بياييد كردار خود را بسنجيم و به سوی خداوند بازگرديم. 41بياييد قلبهای خود را برای خدايی كه در آسمان است بگشاييم و دستهای خود را به سوی او برافرازيم. 42زيرا ما گناه كردهايم و نسبت به او ياغی شدهايم و او اين شرارت ما را فراموش نكرده است.
43ای خدا، تو به هنگام غضب خود ما را تعقيب نموده و هلاک كردهای و رحم ننمودهای. 44خود را با ابر پوشانيدهای تا دعاهای ما به حضور تو نرسد. 45ما را مثل خاكروبه و زباله به ميان قومها انداختهای. 46تمام دشمنانمان به ما توهين میكنند. 47خرابی و نابودی دامنگير ما شده و در ترس و خطر زندگی میكنيم.
48-49به سبب نابودی قومم، روز و شب سيل اشک از چشمانم جاريست. آنقدر خواهم گريست 50تا خداوند از آسمان نظر كند و پاسخ دهد! 51هنگامی كه میبينم چه بر سر دختران جوان اورشليم آمده است، دلم از اندوه پر میشود.
52كسانی كه هرگز آزارشان نداده بودم، دشمن من شدند و مرا همچون پرندهای به دام انداختند. 53آنها مرا در چاه افكندند و سر چاه را با سنگ پوشاندند. 54آب از سرم گذشت و فكر كردم مرگم حتمی است. 55اما ای خداوند، وقتی از عمق چاه نام تو را خواندم 56صدايم را شنيدی و به نالههايم توجه كردی. 57آری، هنگامی كه تو را خواندم به كمكم آمدی و گفتی: «نترس!»
58ای خداوند، تو به دادم رسيدی و جانم را از مرگ رهايی بخشيدی. 59ای خداوند، تو ظلمی را كه به من كردهاند ديدهای، پس داوری كن و داد مرا بستان. 60ديدهای كه چگونه ايشان دشمن من شده و توطئهها بر ضد من چيدهاند. 61ای خداوند، تو شنيدهای كه چگونه به من اهانت كرده و عليه من نقشه كشيدهاند. 62تو از تمام آنچه كه مخالفانم هر روز درباره من میگويند و نقشههايی كه میكشند باخبری. 63ببين چگونه میخندند و شب و روز مرا مسخره میكنند.
64ای خداوند، ايشان را به سزای اعمالشان برسان. 65ايشان را لعنت كن تا غم و تاريكی وجودشان را فرا گيرد. 66با خشم و غضب آنها را تعقيب كن و از روی زمين محو و نابود گردان.