Maliro 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 1:1-22

1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,

umene kale unali wodzaza ndi anthu!

Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!

Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.

Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,

tsopano wasanduka kapolo.

2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,

misozi ili pa masaya pake.

Mwa abwenzi ake onse,

palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.

Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;

onse akhala adani ake.

3Yuda watengedwa ku ukapolo,

kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.

Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;

ndipo alibe malo opumulira.

Onse omuthamangitsa iye amupitirira,

ndipo alibe kwina kothawira.

4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,

chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.

Zipata zake zonse zili pululu,

ansembe akubuwula.

Anamwali ake akulira,

ndipo ali mʼmasautso woopsa.

5Adani ake asanduka mabwana ake;

odana naye akupeza bwino.

Yehova wamubweretsera mavuto

chifukwa cha machimo ake ambiri.

Ana ake atengedwa ukapolo

pamaso pa mdani.

6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni

wachokeratu.

Akalonga ake ali ngati mbawala

zosowa msipu;

alibe mphamvu zothawira

owathamangitsa.

7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,

Yerusalemu amakumbukira chuma chonse

chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.

Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,

panalibe aliyense womuthandiza.

Adani ake ankamuyangʼana

ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

8Yerusalemu wachimwa kwambiri

ndipo potero wakhala wodetsedwa.

Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,

chifukwa aona umaliseche wake.

Iye mwini akubuwula

ndipo akubisa nkhope yake.

9Uve wake umaonekera pa zovala zake;

iye sanaganizire za tsogolo lake.

Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;

ndipo analibe womutonthoza.

“Inu Yehova, taonani masautso anga,

pakuti mdani wapambana.”

10Adani amulanda

chuma chake chonse;

iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,

amene Inu Mulungu munawaletsa

kulowa mu msonkhano wanu.

11Anthu ake onse akubuwula

pamene akufunafuna chakudya;

asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya

kuti akhale ndi moyo.

“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,

chifukwa ine ndanyozeka.”

12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?

Yangʼanani ndipo muone.

Kodi pali mavuto ofanana ndi

amene andigwerawa,

amene Ambuye anandibweretsera

pa tsiku la ukali wake?

13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,

unalowa mpaka mʼmafupa anga.

Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga

ndipo anandibweza.

Anandisiya wopanda chilichonse,

wolefuka tsiku lonse.

14“Wazindikira machimo anga onse

ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.

Machimowa afika pakhosi panga,

ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.

Iye wandipereka

kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15“Ambuye wakana

anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:

wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,

kuti litekedze anyamata anga;

mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza

anamwali a Yuda.

16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira

ndipo maso anga adzaza ndi misozi.

Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,

palibe aliyense wondilimbitsa mtima.

Ana anga ali okhaokha

chifukwa mdani watigonjetsa.

17“Ziyoni wakweza manja ake,

koma palibe aliyense womutonthoza.

Yehova walamula kuti abale ake

a Yakobo akhale adani ake;

Yerusalemu wasanduka

chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18“Yehova ndi wolungama,

koma ndine ndinawukira malamulo ake.

Imvani inu anthu a mitundu yonse;

onani masautso anga.

Anyamata ndi anamwali anga

agwidwa ukapolo.

19“Ndinayitana abwenzi anga

koma anandinyenga.

Ansembe ndi akuluakulu anga

anafa mu mzinda

pamene ankafunafuna chakudya

kuti akhale ndi moyo.

20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!

Ndikuzunzika mʼkati mwanga,

ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa

chifukwa ndakhala osamvera.

Mʼmisewu anthu akuphedwa,

ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21“Anthu amva kubuwula kwanga,

koma palibe wonditonthoza.

Adani anga onse amva masautso anga;

iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.

Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija

kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;

muwalange

ngati mmene mwandilangira ine

chifukwa cha machimo anga onse.

Ndikubuwula kwambiri

ndipo mtima wanga walefuka.”

Persian Contemporary Bible

مراثی 1:1-22

1اورشليم كه زمانی پرجمعيت بود اينک متروک شده است! شهری كه در بين قومها محبوب بود اينک بيوه گشته است! او كه ملكهٔ شهرها بود اينک برده شده است!

2اورشليم تمام شب می‌گريد و قطره‌های اشک روی گونه‌هايش می‌غلتد. از ميان يارانش يكی هم باقی نمانده كه او را تسلی دهد. دوستانش به او خيانت كرده و همگی با او دشمن شده‌اند.

3مردم مصيبت‌زده و رنجديدهٔ يهودا به اسارت رفته‌اند؛ به ديار غربت تبعيد شده‌اند و اينک هيچ آسايش ندارند. دشمنان، آنها را احاطه نموده عرصه را بر آنها تنگ كرده‌اند.

4ديگر كسی به خانهٔ خدا نمی‌آيد تا در روزهای عيد عبادت كند. دخترانی كه سرود می‌خواندند اينک عزادارند، و كاهنان تنها آه می‌كشند. دروازه‌های شهر، متروک شده و اورشليم در ماتم فرو رفته است.

5دشمنانش بر او غلبه يافته كامياب شده‌اند. خداوند اورشليم را برای گناهان بسيارش تنبيه كرده است. دشمنان، فرزندان او را اسير كرده، به ديار غربت به بردگی برده‌اند.

6تمام شكوه و زيبايی اورشليم از دست رفته است. بزرگانش مانند غزالهای گرسنه دنبال چراگاه می‌گردند و ناتوانتر از آنند كه بتوانند از چنگ دشمن فرار كنند.

7اينک اورشليم در ميان مصیبتها، روزهای پرشكوه گذشته را به ياد می‌آورد. زمانی كه او به محاصرهٔ دشمن درآمد، هيچ مدد كننده‌ای نداشت؛ دشمن او را مغلوب كرد و به شكست او خنديد.

8اورشليم گناهان بسياری مرتكب شده و ناپاک گرديده است. تمام كسانی كه او را تكريم می‌كردند، اينک تحقيرش می‌كنند، زيرا برهنگی و خواری او را ديده‌اند. او می‌نالد و از شرم، چهرهٔ خود را می‌پوشاند.

9لكهٔ ننگی بر دامن اورشليم بود، اما او اعتنايی نكرد؛ او به عاقبت خود نيانديشيد و ناگهان سقوط كرد. اينک كسی نيست كه او را تسلی دهد. او از خداوند رحمت می‌طلبد، زيرا دشمن بر او غالب آمده است.

10دشمن، گنجينه‌های او را غارت كرد و قومهای بيگانه در برابر چشمانش به عبادتگاه مقدسش داخل شدند، قومهایی كه خدا ورود آنها را به عبادتگاهش قدغن كرده بود.

11اهالی اورشليم برای يک لقمه نان آه می‌كشند. هر چه داشتند برای خوراک دادند تا زنده بمانند. اورشليم می‌گويد: «خداوندا، ببين چگونه خوار شده‌ام!

12«ای كسانی كه از كنارم می‌گذريد، چرا به من نگاه نمی‌كنيد؟ نگاهی به من بيندازيد و ببينيد آيا غمی همچون غم من وجود دارد؟ ببينيد خداوند به هنگام خشم خود به من چه كرده است!

13«او از آسمان آتش نازل كرد و تا مغز استخوان مرا سوزاند. سر راهم دام گسترد و مرا به زمين كوبيد. او مرا ترک گفت و در غمی بی‌پايان رهايم كرد.

14«گناهانم را به هم بافت و همچون طنابی بر گردنم انداخت و مرا زير يوغ بردگی كشاند. تمام توانم را گرفت و مرا در چنگ دشمنانم كه قويتر از من بودند رها كرد.

15«خداوند تمام سربازان شجاع مرا از من گرفت. او لشكری بر ضد من فرا خواند تا جوانان مرا از بين ببرند. خداوند شهر محبوب خود را همچون انگور در چرخشت پايمال كرد.

16«برای اين مصيبتهاست كه می‌گريم و قطره‌های اشک بر گونه‌هايم می‌غلتد. آن كه به من دلداری می‌داد و جانم را تازه می‌ساخت از من دور شده است. دشمن بر من غالب آمده و فرزندانم بی‌كس شده‌اند.

17«دستهای خود را دراز می‌كنم و كمک می‌طلبم، اما كسی نيست كه به دادم برسد. خداوند قومهای همسايه را بر ضد من فرا خوانده و من مورد نفرت آنان قرار گرفته‌ام.

18«اما خداوند عادلانه حكم فرموده است، زيرا من از فرمان او سرپيچی كرده بودم. ای مردم جهان، اندوه مرا بنگريد و ببينيد چگونه پسران و دخترانم را به اسيری برده‌اند.

19«از ياران كمک خواستم، اما ايشان به من خيانت كردند. كاهنان و ريش‌سفيدان در حالی كه به دنبال لقمه نانی بودند تا خود را زنده نگه دارند، در كوچه‌های شهر از گرسنگی جان دادند.

20«ای خداوند، ببين چقدر پريشان و نگرانم! به خاطر گناهانی كه انجام داده‌ام جانم در عذاب است. در خانه، بلای كشنده در انتظارم است و در بيرون، شمشير مرگبار.

21«مردم ناله‌هايم را می‌شنوند، اما كسی به دادم نمی‌رسد. دشمنانم چون شنيدند چه بلايی بر سرم آوردی، شاد شدند. ای خداوند، به وعده‌ات وفا كن و بگذار دشمنانم نيز به بلای من دچار گردند.

22«به گناهان آنها نيز نظر كن و همانگونه كه مرا برای گناهانم تنبيه كرده‌ای، آنان را نيز به سزای كردارشان برسان. ناله‌های من بسيار و دلم بی‌تاب است.»