Luka 20 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 20:1-47

Amufunsa Yesu za Ulamuliro Wake

1Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye. 2Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”

3Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe, 4‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’ ”

5Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’ 6Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”

7Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”

8Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”

Fanizo la Olima Mʼmunda Wamphesa

9Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali. 10Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu. 11Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu. 12Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.

13“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’

14“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’ 15Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha.

“Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa? 16Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.”

Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”

17Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti,

“ ‘Mwala umene omanga nyumba anawukana

wasanduka mwala wa pa ngodya.

18Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’ ”

19Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.

Za Kupereka Msonkho kwa Kaisara

20Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza. 21Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi. 22Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”

23Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti, 24“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”

25Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.”

Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”

26Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.

Za Kuuka kwa Akufa ndi Ukwati

27Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso. 28Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo. 29Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana. 30Wachiwiri 31ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana. 32Pa mapeto pake mkaziyo anafanso. 33Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”

34Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. 35Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. 36Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa. 37Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’ 38Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”

39Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!” 40Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.

Khristu ndi Mwana wa Ndani?

41Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide? 42Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Ambuye anati kwa Ambuye anga:

‘Khalani ku dzanja langa lamanja,

43mpaka Ine nditasandutsa adani anu

chopondapo mapazi anu?’

44Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”

Achenjeza za Aphunzitsi Amalamulo

45Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake, 46“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando. 47Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

Persian Contemporary Bible

لوقا 20:1-47

اقتدار و اختيارات عيسی

1در يكی از همان روزها كه عيسی در خانهٔ خدا تعليم می‌داد و پيغام نجاتبخش خدا را به مردم اعلام می‌كرد، كاهنان اعظم و ساير علمای دين با اعضای مجلس شورای يهود نزد او آمدند، 2تا بپرسند با چه اجازه و اختياری، فروشندگان را از خانه خدا بيرون كرده است.

3عيسی پاسخ داد: «پيش از آنكه جواب شما را بدهم، می‌خواهم از شما سؤالی بكنم: 4آيا يحيی را خدا فرستاده بود تا مردم را تعميد دهد، يا با اختيار خودش تعميد می‌داد؟»

5ايشان درباره اين موضوع با يكديگر مشورت كرده، گفتند: «اگر بگوييم از سوی خدا فرستاده شده بود، خود را به دام انداخته‌ايم، زيرا خواهد پرسيد: پس چرا به او ايمان نياورديد؟ 6و اگر بگوييم كه خدا او را نفرستاده بود، مردم ما را سنگسار خواهند كرد، چون يحيی را فرستاده خدا می‌دانند.» 7بنابراين جواب دادند: «ما نمی‌دانيم!»

8عيسی فرمود: «پس من نيز جواب سؤال شما را نخواهم داد!»

حكايت باغبانهای ظالم

9آنگاه رو به جماعت كرده، اين حكايت را برای ايشان تعريف كرد: «شخصی تاكستانی درست كرد و آن را به چند باغبان اجاره داد و خودش به سرزمين دوردستی سفر كرد تا در آنجا زندگی كند. 10در فصل انگورچينی، يكی از خدمتگزاران خود را فرستاد تا سهم خود را از محصول تاكستان بگيرد. اما باغبانها او را زدند و دست خالی بازگرداندند. 11پس صاحب باغ يک نفر ديگر را فرستاد. اما باز هم بی‌فايده بود؛ او نيز كتک خورد، ناسزا شنيد و دست خالی بازگشت. 12سومی را فرستاد. او را نيز زدند و زخمی كردند و از باغ بيرون انداختند.

13«صاحب باغ با خود گفت: حال چه بايد كرد؟ فهميدم چه كنم! پسر عزيزم را خواهم فرستاد. يقيناً به او احترام خواهند گذاشت.

14«وقتی باغبانها پسر او را ديدند، با خود فكر كرده، گفتند: اين بهترين فرصت است! پس از مرگ صاحب باغ، تمام ملک به اين پسر خواهد رسيد. پس بياييد او را بكشيم تا باغ به خودمان برسد.

15«بنابراين، او را گرفتند و كشان‌كشان از باغ بيرون بردند و كشتند. حال به نظر شما، صاحب باغ چه خواهد كرد؟ 16بگذاريد بگويم چه خواهد كرد: او خواهد آمد و همه باغبانها را خواهد كشت و باغ را به ديگران اجاره خواهد داد.»

شنوندگان اعتراض‌كنان گفتند: «باغبانها هرگز چنين كاری نخواهند كرد!»

17عيسی نگاهی به ايشان كرد و گفت: «پس منظور كلام خدا چيست كه می‌گويد: سنگی كه معماران دور انداختند، سنگ اصلی ساختمان شد؟ 18هر کس بر آن سنگ بيفتد، خرد خواهد شد و اگر آن سنگ بر كسی بيفتد، او را له خواهد كرد!»

19وقتی كاهنان اعظم و علمای دين اين داستان را شنيدند، خواستند همانجا او را دستگير كنند، چون متوجه شدند كه اين داستان را درباره ايشان گفته، و منظورش از باغبانهای ظالم، آنان بوده است. اما می‌ترسيدند كه اگر خودشان دست به چنين كاری بزنند، آشوب به پا شود.

جواب دندان‌شكن

20از این رو می‌كوشيدند او را وادار كنند سخنی بگويد تا از آن، عليه او استفاده كنند و او را به مقامات رومی تحويل دهند. به همين منظور چند مأمور مخفی نزد او فرستادند كه خود را حقجو نشان می‌دادند. 21ايشان به عيسی گفتند: «استاد، ما می‌دانيم كه آنچه تو می‌گويی و تعليم می‌دهی، راست و درست است. ما می‌دانيم كه تو بدون توجه به مقام و موقعيت افراد، هميشه حقيقت را می‌گويی و راه خدا را تعليم می‌دهی. 22حال بفرما آيا طبق شريعت موسی، درست است كه ما به دولت روم باج و خراج بدهيم؟»

23عيسی كه متوجه مكر و حيلهٔ ايشان شده بود، گفت: 24«سكه‌ای به من نشان دهيد. نقش و نام چه كسی بر روی آن است؟»

جواب دادند: «امپراتور روم.»

25فرمود: «هر چه مال امپراتور است، به امپراتور بدهيد، و هر چه مال خداست، به خدا!»

26به اين ترتيب، تلاش آنان برای به دام انداختن عيسی بی‌اثر ماند و از جواب او مات و مبهوت ماندند و ديگر حرفی نزدند.

آيا قيامتی در كار هست؟

27سپس عده‌ای از صدوقی‌ها نزد او آمدند. صدوقی‌ها معتقد به روز قيامت نبودند و می‌گفتند كه مرگ پايان زندگی است. ايشان مسئله‌ای را مطرح كردند 28و چنين گفتند: «در تورات موسی آمده كه اگر مردی بی‌اولاد بميرد، برادرش بايد بيوهٔ او را به همسری اختيار كند و فرزندان ايشان، فرزندان آن برادر مرده به حساب خواهند آمد تا نسل او برقرار بماند. 29باری، در خانواده‌ای هفت برادر بودند. برادر بزرگتر همسری گرفت و بی‌اولاد مرد. 30برادر كوچكترش با آن بيوه ازدواج كرد و او هم بی‌اولاد مرد. 31به اين ترتيب، تا برادر هفتم، همه يكی پس از ديگری، با آن زن ازدواج كردند و همه نيز بی‌اولاد مردند. 32در آخر، آن زن نيز مرد. 33حال، سؤال ما اينست كه در روز قيامت، او زن كدام يک از آن هفت برادر خواهد بود؟ چون هر هفت برادر با او ازدواج كرده بودند؟»

34عيسی جواب داد: «ازدواج، برای مردم فانی اين دنياست؛ 35‏-36اما كسانی كه شايسته شمرده شوند كه پس از مرگ زنده گردند، وقتی به آن عالم بروند، نه ازدواج می‌كنند و نه می‌ميرند؛ و از اين لحاظ مانند فرشتگان و فرزندان خدا می‌شوند؛ زيرا از مرگ به يک زندگی تازه منتقل شده‌اند.

37«اما درباره سؤال اصلی شما، يعنی اينكه آيا قيامت مردگان وجود دارد يا نه، موسی به روشنی نشان داد كه قيامت وجود خواهد داشت. زيرا وقتی موسی بازگو می‌كند كه چگونه خدا در بوته سوزان بر او ظاهر شد، از خدا به عنوان خدای ابراهيم، خدای اسحاق و خدای يعقوب نام می‌برد. 38و هنگامی كه خدا، خدای كسی ناميده می‌شود، منظور آنست كه آن شخص زنده است و نه مرده! زيرا در نظر خدا، همه زنده هستند!»

39چند نفر از علمای دين كه آنجا ايستاده بودند، گفتند: «استاد، بسيار خوب جواب دادی!» 40و از آن پس ديگر كسی جرأت نكرد سؤالی از او بكند!

مسيح پسر کيست؟

41اما اين بار عيسی خود سؤالی از ايشان كرد. او فرمود: «چرا می‌گويند كه مسيح موعود بايد از نسل داوود پادشاه باشد؟ 42‏-43در حالی که خود داوود، در كتاب زبور نوشته است كه خدا به خداوند من، مسيح، گفت: به دست راست من بنشين تا دشمنانت را زير پايهايت بيفكنم. 44چگونه ممكن است كه مسيح، هم پسر داوود باشد و هم خداوند او؟»

تظاهر به دينداری

45سپس در حالی که جمعيت به او گوش می‌دادند، رو به شاگردان خود كرد و گفت: 46«از اين علمای متظاهر دوری كنيد كه دوست دارند با قباهای بلند، خودنمايی كنند و به هنگام عبور از كوچه و بازار، مردم به ايشان تعظيم كنند؛ و چقدر دوست دارند كه در عبادتگاه‌ها و جشنهای مذهبی، بالای مجلس بنشينند. 47اما حتی وقتی دعاهای طولانی می‌كنند و تظاهر به دينداری می‌نمايند، تمام هوش و حواسشان به اينست كه چگونه اموال بيوه‌زنان را تصاحب كنند. از این رو مجازات آنان بسيار شديد خواهد بود.»