Luka 19 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 19:1-48

Zakeyu Apulumutsidwa

1Yesu analowa mu Yeriko napitirira. 2Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera. 3Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu. 4Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.

5Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.” 6Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.

7Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”

8Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”

9Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu. 10Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”

Antchito Opindula Mosiyana

11Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo. 12Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo. 13Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’

14“Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’

15“Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.

16“Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’

17“Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’

18“Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’

19“Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’

20“Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu. 21Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’

22“Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale? 23Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’

24“Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’ ”

25Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”

26Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho. 27Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”

Yesu Alowa mu Yerusalemu Mwaulemerero

28Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu. 29Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo, 30“Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno. 31Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’ ”

32Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira. 33Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”

34Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”

35Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu. 36Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.

37Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.

38“Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!”

“Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”

39Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”

40Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”

41Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira 42nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako. 43Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse. 44Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”

Yesu mʼNyumba ya Mulungu

45Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda. 46Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”

47Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe. 48Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.

Persian Contemporary Bible

لوقا 19:1-48

باجگيری به عيسی ايمان می‌آورد

1عيسی وارد اريحا شد تا از آنجا راه خود را به سوی اورشليم ادامه دهد. 2در اريحا شخص ثروتمندی زندگی می‌كرد، به نام «زَكّی» كه رئيس مأمورين باج و خراج بود؛ 3او می‌خواست عيسی را ببيند، اما به سبب ازدحام مردم نمی‌توانست، چون قدش كوتاه بود. 4پس جلو دويد و از درخت چناری كه در كنار راه بود، بالا رفت تا از آنجا عيسی را ببيند.

5وقتی عيسی نزديک درخت رسيد، به بالا نگاه كرد و او را به نام صدا زد و فرمود: «زَكّی، بشتاب و پايين بيا! چون می‌خواهم امروز به خانه تو بيايم و مهمانت باشم!»

6زَكّی با عجله پايين آمد و با هيجان و شادی، عيسی را به خانه خود برد.

7تمام كسانی كه اين واقعه را ديدند، گله و شكايت سر داده، با ناراحتی می‌گفتند: «او میهمان يک گناهكار بدنام شده است!»

8اما زَكّی در حضور عيسای خداوند ايستاد و گفت: «سَروَر من، اينک نصف دارايی خود را به فقرا خواهم بخشيد، و اگر از كسی ماليات اضافی گرفته باشم، چهار برابر آن را پس خواهم داد!»

9‏-10عيسی به او فرمود: «اين نشان می‌دهد كه امروز نجات به اهل اين خانه روی آورده است. اين مرد، يكی از فرزندان ابراهيم است كه گمراه شده بود. من آمده‌ام تا چنين اشخاص را بيابم و نجات بخشم!»

در كار خداوند، كوشا و وفادار باشيد

11چون عيسی به اورشليم نزديک می‌شد، داستانی تعريف كرد تا نظر بعضی اشخاص را درباره ملكوت خدا اصلاح كند، چون تصور می‌كردند كه ملكوت خدا همان موقع آغاز خواهد شد. 12پس چنين فرمود: «در يكی از ايالات امپراتوری روم، نجيب‌زاده‌ای زندگی می‌كرد. روزی او سفر دور و درازی به پايتخت كرد، تا از جانب امپراتور به مقام پادشاهی آن ايالت منصوب شود. 13اما پيش از عزيمت، ده نفر از دستياران خود را احضار كرد و به هر يک، مبلغی پول داد تا در غياب او به تجارت بپردازند. 14اما برخی از اهالی آن ايالت كه با او مخالف بودند، نمايندگانی به حضور امپراتور فرستادند تا اطلاع دهند كه مايل نيستند آن نجيب‌زاده بر آنان حكمرانی كند.

15«اما آن شخص به مقام پادشاهی منصوب شد و به ايالت خود بازگشت و دستياران خود را فرا خواند تا ببيند با پولش چه كرده‌اند و چه مقدار سود به دست آورده‌اند.

16«پس اولی آمد و گفت كه ده برابر سرمايه اصلی سود كرده است.

17«پادشاه گفت: آفرين بر تو، ای خدمتگزار خوب! چون در كار و مسئوليت كوچكی كه به تو سپردم، امين بودی، حكمرانی ده شهر را به تو واگذار می‌كنم!

18«نفر دوم نيز گزارش رضايت بخشی داد. او گفت كه پنج برابر سرمايه اصلی، سود كرده است.

19«به او نيز گفت: بسيار خوب! تو نيز حاكم پنج شهر باش!

20‏-21«اما سومی همان مبلغی را كه در ابتدا گرفته بود، بدون كم و زياد پس آورد و گفت: من از ترس شما، سرمايه‌تان را در جای امنی نگهداری كردم، چون می‌دانستم كه مردی هستيد سختگير و از آنچه زحمت نكشيده‌ايد، سود می‌طلبيد و از سرمايه‌ای كه نگذاشته‌ايد، انتظار بهره داريد؟

22«پادشاه او را سرزنش كرده، گفت: ای خدمتكار پست و شرور، تو با اين سخنان خودت را محكوم كردی! تو كه می‌دانستی من اينقدر سختگير هستم، 23چرا پولم را به منفعت ندادی تا به هنگام مراجعت، لااقل سودش را بگيرم؟

24«آنگاه به حاضران فرمود كه پول را از او بگيرند و به آن خدمتكاری بدهند كه از همه بيشتر سود آورده بود.

25«گفتند: قربان، او خودش به اندازه كافی دارد!

26«پادشاه جواب داد: بلی، اين حقيقت هميشه صادق است كه آنانی كه زياد دارند، بيشتر به دست می‌آورند و آنانی كه كم دارند، همان را نيز از دست می‌دهند. 27و اما مخالفينی كه نمی‌خواستند بر آنان حكومت كنم، ايشان را اكنون به اينجا بياوريد و در حضور من، گردن بزنيد.»

ورود عيسی به اورشليم

28پس از تعريف اين داستان، عيسی پيشاپيش ديگران، به سوی اورشليم به راه افتاد. 29وقتی به «بيت‌فاجی» و «بيت‌عنيا» واقع بر كوه زيتون رسيدند، دو نفر از شاگردان خود را زودتر فرستاد، 30و به ايشان گفت: «به روستايی كه در پيش است، برويد. وقتی وارد شديد، كرّه الاغی را بسته خواهيد ديد كه تا به حال كسی بر آن سوار نشده است. آن را باز كنيد و به اينجا بياوريد. 31اگر كسی پرسيد كه چه می‌كنيد، فقط بگوييد: خداوند آن را لازم دارد!»

32آن دو شاگرد رفتند و كرّه الاغ را همانگونه كه عيسی فرموده بود، يافتند. 33وقتی آن را باز می‌كردند، صاحبانش جويای ماجرا شده، پرسيدند: «چه می‌كنيد؟ چرا كرّه الاغ را باز می‌كنيد؟»

34جواب دادند: «خداوند آن را لازم دارد!»

35پس كرّه الاغ را نزد عيسی آوردند، و جامه‌های خود را بر آن انداختند تا او سوار شود.

36هنگامی كه عيسی به راه افتاد، مردم به احترام او، لباسهای خود را در راه، در مقابل او پهن می‌كردند. 37وقتی به سرازيری كوه زيتون رسيدند، گروه انبوه پيروانش فرياد شادی برآورده، برای همه معجزات و كارهای عجيبی كه انجام داده بود، خدا را شكر می‌كردند، 38و می‌گفتند: «مبارک باد پادشاهی كه به نام خداوند می‌آيد! آرامش در آسمان و جلال بر خدا باد!»

39آنگاه برخی از فريسيان كه در ميان جمعيت بودند، به عيسی گفتند:

«استاد، پيروانت را امر كن كه ساكت باشند! اين چه چيزهاست كه می‌گويند؟»

40عيسی جواب داد: «اگر آنان ساكت شوند، سنگهای كنار راه بانگ شادی برخواهند آورد!»

گريه برای اورشليم

41اما همين كه به اورشليم نزديک شدند و عيسی شهر را از دور ديد، به گريه افتاد، 42و در حالی که اشک می‌ريخت، گفت: «ای اورشليم، صلح و آرامش جاويد در اختيار تو قرار داده شد، اما تو آن را رد كردی! و اينک ديگر بسيار دير است! 43بزودی دشمنانت، در پشت همين ديوارها، سنگرها ساخته، از هر سو تو را محاصره و احاطه خواهند كرد. 44آنگاه تو را با خاک يكسان كرده، ساكنانت را به خاک و خون خواهند كشيد. حتی نخواهند گذاشت سنگی بر سنگی ديگر باقی بماند، بلكه همه چيز را زير و رو خواهند كرد. زيرا فرصتی را كه خدا به تو داده بود، رد كردی!»

پاکسازی معبد

45سپس وارد خانهٔ خدا شد و كسانی را كه در آنجا مشغول خريد و فروش بودند، بيرون كرد و بساط آنان را در هم ريخت، 46و به ايشان گفت: «در كلام خدا نوشته شده است كه خانه من محل عبادت خواهد بود، اما شما آن را تبديل به پناهگاه دزدان كرده‌ايد!»

47از آن پس عيسی هر روز در خانه خدا تعليم می‌داد. كاهنان اعظم، علمای دين و بزرگان قوم در پی فرصتی می‌گشتند تا او را از بين ببرند، 48اما راهی پيدا نمی‌كردند، چون مردم همواره گرد او جمع می‌شدند تا سخنانش را بشنوند.