Hagai 2 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 2:1-23

Ulemerero wa Nyumba Yatsopano ya Yehova

1Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti: 2“Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti, 3‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu? 4Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 5‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’

6“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda. 7Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 8‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 9‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

Madalitso kwa Anthu Oyipitsidwa

10Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti: 11“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena: 12Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’ ”

Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”

13Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?”

Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”

14Pamenepo Hagai anati, “ ‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.

15“ ‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova. 16Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha. 17Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova 18‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino. 19Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso.

“ ‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’ ”

Zerubabeli Mphete Yolamulira ya Yehova

20Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti: 21“Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi. 22Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.

23“ ‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

New Russian Translation

Аггей 2:1-23

Будущее величие нового храма

1В двадцать первый день седьмого месяца2:1 17 октября 520 г. до н. э. было слово Господа через пророка Аггея:

2– Говори с наместником Иудеи Зоровавелем, сыном Шеалтиила, первосвященником Иисусом, сыном Иоседека, и остальным народом. Спроси их: 3«Кто из вас еще помнит этот дом в его прежней славе? Каким вы видите его сейчас? Разве он не кажется вам ничтожным?» 4Но сейчас ободрись, Зоровавель, – возвещает Господь. – Ободрись, Иисус, сын Иоседека, первосвященник. Ободритесь, и весь народ страны, – возвещает Господь, – и трудитесь, потому что Я с вами, – возвещает Господь Сил, – 5по завету, который Я заключил с вами, когда вы вышли из Египта. Мой Дух пребывает с вами; не бойтесь!

6Так говорит Господь Сил:

– Вскоре Я еще раз сотрясу небеса и землю, море и сушу. 7Я сотрясу все народы, и их сокровища придут сюда, и Я наполню этот дом славой2:7 Я наполню этот дом славой – Это обещание исполнилось в Иисусе Христе. Например, в Новом Завете (Лк. 2:27-32) рассказывается о том, как младенца Иисуса впервые принесли в храм. Позже, перед самой смертью, Иисус заявил в храме, что Он – Живая Вода, которая может дать истинную жизнь всем тем, кто поверит в Него (Ин. 7:37-39). Это заявление о пути спасения, которое Бог предлагает всем, является еще одним исполнением данного Им обещания., – говорит Господь Сил. – 8Серебро и золото Мои, – возвещает Господь Сил. – 9Слава этого дома превзойдет славу прежнего, – говорит Господь Сил, – и здесь Я дарую благоденствие, – возвещает Господь Сил.

Обличение народа

10В двадцать четвертый день девятого месяца, во второй год правления царя Дария2:10 18 декабря 520 г. до н. э., было слово Господа к пророку Аггею:

11– Так говорит Господь Сил: Спроси священников, что говорит Закон: 12если кто-то несет посвященное мясо в поле одежды и прикоснется ею к хлебу, похлебке, вину, маслу или другой еде, освятится ли эта еда?

Священники ответили:

– Нет.

13Тогда Аггей сказал:

– А если тот, кто осквернился, прикоснувшись к покойнику, коснется одной из этих вещей, тогда эта вещь осквернится?

– Да, – ответили священники, – тогда осквернится.

14И Аггей сказал:

– Так и с этим народом, с этим родом, что предо Мной, – возвещает Господь. – Все, что они делают, и все, что они приносят там, нечисто.

Обещание благословения

15– Вспомните недавнее прошлое, до того, как камень был положен на камень в храме Господа. 16Когда вы приходили к копне, в которой было двадцать мер, в ней оказывалось лишь десять. Когда вы приходили к давильне, чтобы начерпать пятьдесят мер, в ней оказывалось всего двадцать. 17Я поражал все труды ваших рук знойным ветром, плесенью и градом, но вы не обращались ко Мне, – возвещает Господь. – 18Вспомните недавнее прошлое, начиная с сегодняшнего дня, двадцать четвертого дня девятого месяца, когда были заложены основания храма. 19Остались ли еще семена в закромах? Ни виноградная лоза, ни инжир, ни гранат, ни олива до сих пор не принесли плода. Но с этого дня Я благословлю вас.

Зоровавель – избранник Бога

20В двадцать четвертый день месяца во второй раз к пророку Аггею было слово Господа:

21– Скажи Зоровавелю, наместнику Иудеи, что Я сотрясу небо и землю. 22Я низвергну царские престолы и сломлю силу чужеземных царств. Я опрокину колесницы и колесничих; падут кони и их наездники погибнут от мечей друг друга. 23В тот день, – возвещает Господь Сил, – Я возьму тебя, Мой слуга Зоровавель, сын Шеалтиила, – возвещает Господь, – и уподоблю перстню с печатью2:23 Печать была знаком власти, а также удостоверяла личность ее владельца и его право на собственность. Здесь Бог в лице Зоровавеля обращает в благословение то проклятие, которое Он произнес над его дедом, царем Иехонией (см. Иер. 22:24). Зоровавель таким образом становится прообразом Христа и залогом Его пришествия., потому что Я избрал тебя, – возвещает Господь Сил.