Zefaniya 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 1:1-18

1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse

pa dziko lapansi,”

akutero Yehova.

3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;

ndidzawononga mbalame zamlengalenga

ndi nsomba za mʼnyanja.

Ndidzawononga anthu oyipa,

ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda

ndi onse okhala mu Yerusalemu.

Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,

mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:

5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo

kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,

amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,

komanso mʼdzina la Moleki,

6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,

osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.

7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,

chifukwa tsiku la Yehova layandikira.

Yehova wakonzekera kupereka nsembe;

wapatula iwo amene wawayitana.

8Pa tsiku la nsembe ya Yehova

ndidzalanga akalonga

ndi ana aamuna a mfumu

ndi onse amene amavala

zovala zachilendo.

9Pa tsiku limenelo ndidzalanga

onse amene safuna kuponda pa chiwundo,

amene amadzaza nyumba ya ambuye awo

ndi chiwawa ndi chinyengo.

10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,

“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,

kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,

ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.

11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;

a malonda anu onse adzapululidwa,

ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.

12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale

ndi kulanga onse amene sakulabadira,

amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,

amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,

chabwino kaya choyipa.’

13Chuma chawo chidzafunkhidwa,

nyumba zawo zidzagwetsedwa.

Adzamanga nyumba,

koma osakhalamo;

adzadzala minda ya mpesa

koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,

layandikira ndipo lifika msanga.

Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,

ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.

15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,

tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,

tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,

tsiku la mdima ndi lachisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,

tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa

ndi nsanja za pa ngodya.

17Ndidzabweretsa msautso pa anthu

ndipo adzayenda ngati anthu osaona,

chifukwa achimwira Yehova,

magazi awo adzamwazika ngati fumbi

ndi mnofu wawo ngati ndowe.

18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo

sadzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Dziko lonse lapansi lidzanyeka

mʼmoto wa nsanje yake

chifukwa adzakantha modzidzimutsa

onse okhala pa dziko lapansi.

New Russian Translation

Софония 1:1-18

1Слово Господа, которое было к Софонии, сыну Кушия, сына Гедалии, сына Амарии, сына Езекии, во время правления иудейского царя Иосии, сына Амона1:1 Царь Иосия правил в 640–610 гг. до н. э..

Суд над землей

2– Я все смету с лица земли, –

возвещает Господь. –

3Погублю и людей, и скот;

погублю и птиц в небесах,

и рыбу в морях.

Я повергну нечестивцев в прах1:3 Смысл этого места в еврейском тексте неясен.

и сотру человека с лица земли, –

говорит Господь.

Суд над Иудеей

4– Я воздену руку над Иудеей

и над жителями Иерусалима

и сотру здесь последний след Баала1:4 Баал – ханаанский бог плодородия и бог-громовержец.,

имена его жрецов и священников:

5и тех, кто поклоняется на крышах

небесному воинству,

и тех, кто поклоняется и клянется в верности

как Господу, так и Молоху1:5 Или: «своему царю». Молох – аммонитский бог, в жертвы которому приносились дети. По Закону за поклонение Молоху израильтянам грозила смертная казнь (см. Лев. 18:21; 20:2-5).,

6и тех, кто отвернулся от Господа

и не ищет Господа и не вопрошает Его.

7Умолкни перед Владыкой Господом,

так как близок день Господа.

Он приготовил жертву

и уже созвал1:7 Букв.: «освятил». гостей.

8– В день жертвы Господней

Я накажу вождей, и сыновей царя,

и всех, кто наряжается в чужеземное платье1:8 Или: «следуют обычаям других народов». Это был обычай, когда люди при поклонении Баалу наряжались в специальную одежду (см. 4 Цар. 10:22)..

9Я накажу в тот день всех,

кто прыгает через порог1:9 Или: «порог святилища». Вероятно, иудеи подражали некоторым религиозным обычаям филистимлян (см. 1 Цар. 5:5).,

кто наполняет дом своих владык1:9 Или: «Владыки своего»; или: «своих богов».

насилием и обманом.

10– В тот день,

– говорит Господь, –

поднимется крик от Рыбных ворот,

плач из новой части города1:10 Рыбные ворота и новый район города находились в северной части Иерусалима. И именно с севера должен был прийти враг.

и страшный грохот с холмов.

11Плачьте, жители торгового района,

потому что погибнут купцы

и будут истреблены торгующие за серебро.

12Тогда Я обойду Иерусалим со светильниками

в поисках самодовольных и накажу их –

тех, кто подобен вину на дрожжах1:12 Образное сравнение с долго стоявшим вином, в котором образовался осадок, говорит о том, что люди, наслаждающиеся жизнью, полной изобилия, становятся равнодушными и самодовольными и полагают, что и Господь должен с безразличием относиться к добру и злу в мире (см. Иер. 48:11).,

кто думает: «Господь не сделает нам ничего:

ни плохого, ни хорошего».

13Их богатства будут расхищены,

и дома придут в запустение.

Они построят дома,

а жить в них не будут;

посадят они виноградники,

но вина пить не будут.

День Господень

14– Близок великий день Господень,

близок и очень спешит.

Страшный шум поднимется в день Господа,

даже храбрые воины будут кричать.

15Тот день будет днем гнева,

днем скорби и муки,

днем гибели и разрушения,

днем мглы и мрака,

днем туч и тьмы,

16днем звука рога и клича к битве

против укрепленных городов

и высоких башен.

17– Я пошлю на людей такую беду,

что они станут бродить, как слепые,

за то, что согрешили перед Господом.

Их кровь прольется, как вода,

и плоть их будет выброшена, как навоз.

18Ни серебро, ни золото

не смогут спасти их в день гнева Господа.

В пламени Его ревности

сгорит вся земля;

внезапный конец положит Он всем,

кто живет на земле.