Habakuku 3 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 3:1-19

Pemphero la Habakuku

1Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

2Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;

Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.

Muzichitenso masiku athu ano,

masiku athu ano zidziwike;

mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

3Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,

Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.

Sela

Ulemerero wake unaphimba mlengalenga

ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.

4Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;

kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,

mʼmene anabisamo mphamvu zake.

5Patsogolo pake pankagwa mliri;

nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.

6Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;

anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.

Mapiri okhazikika anagumuka

ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.

Njira zake ndi zachikhalire.

7Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,

mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

8Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?

Kodi munakalipira timitsinje?

Kodi munapsera mtima nyanja

pamene munakwera pa akavalo anu

ndiponso magaleta anu achipulumutso?

9Munasolola uta wanu mʼchimake,

munayitanitsa mivi yambiri.

Sela

Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;

10mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.

Madzi amphamvu anasefukira;

nyanja yozama inakokoma

ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,

pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,

pa kunyezimira kwa mkondo wanu.

12Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,

ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.

13Munapita kukalanditsa anthu anu,

kukapulumutsa wodzozedwa wanu.

Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,

munawononga anthu ake onse.

Sela

14Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake

pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,

ankasangalala ngati kuti akudzawononga

osauka amene akubisala.

15Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,

kuvundula madzi amphamvu.

16Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,

milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;

mafupa anga anaguluka,

ndipo mawondo anga anawombana.

Komabe ndikuyembekezera mofatsa,

tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.

17Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,

ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.

Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,

ndipo mʼminda musatuluke kanthu.

Ngakhale nkhosa

ndi ngʼombe zithe mʼkhola,

18komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;

amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,

amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

Japanese Contemporary Bible

ハバクク書 3:1-19

3

ハバククの祈り

1これは、ハバククが主の前で歌った勝利の祈りです。

2主よ。

今、私は、あなたのうわさを聞きました。

あなたがしようとしておられるみわざを知り、

恐れをもって礼拝しています。

この非常時に直面している私たちを、

再び、昔のあなたのようにお助けください。

あなたの力を示してください。

御怒りの中にも、あわれみを忘れないでください。

3神がシナイ山から砂漠を越えて来られるのが

見えます。

その輝きが天地に満ちています。

その栄光は天に満ち、地は神への賛美でいっぱいです。

神は、なんとすばらしい方でしょう。

4両手からは、まばゆいばかりの光が放たれます。

神は恐るべき力を秘め、

5疫病を従えて進みます。

6神はしばらくの間じっと立ち止まり、

地上を見渡します。

それから国々を揺り動かし、

今までびくともしなかった山々を打ち砕き、

丘を平らにするのです。

あなたの力は変わることがありません。

7クシャンとミデヤンの人々が

恐れおののいているのが見えます。

8-9主よ、川を打ち、海の水を左右に分けたのは、

怒ってそうしたのですか。

川や海に不満を抱いたからですか。

いいえ、

あなたの救いの戦車を遣わそうとされたのです。

すべての人がその力を見ました。

それから、あなたが命じると、

泉が地の上にわき出ました。

10山々はそれを見て、震えました。

激流が走り、

深い淵が叫んで、主への降伏を告げました。

11見上げる太陽と月は光を失い始め、

あなたの矢から発する輝きと槍のひらめきとで、

ぼやけています。

12あなたは憤りに燃えて地を行き巡り、

御怒りで国々を踏みつけました。

13ご自分が選んだ民を救うために出て行き、

悪者たちの頭を砕き、

頭のてっぺんから足のつま先まで、

その骨をさらしものにしました。

14イスラエルなど物の数ではないと、

つむじ風のようにやって来た者たちを、

彼らの武器で滅ぼしました。

15あなたの騎手たちは海を渡って前進し、

大水は高くもり上がりました。

16このすべてを聞いて、私は震え、

歯ががくがくしています。

足もとがふらつき、ぶるぶる震えています。

私は、侵略した民に苦しみが襲いかかる日を、

静かに待ち望みましょう。

17いちじくの木が全滅して花も実もつけず、

オリーブの木も実りがなく、

畑が荒れたままであっても、

羊の群れが野で死に、牛小屋がからっぽでも、

18私は主を喜びます。

私を救ってくださる神のおかげで幸せです。

19神、主は私の力です。

私を鹿のように速く走れるようにし、

山の向こうに安全に連れて行ってくださるのです。

(聖歌隊の指揮者のために。

この頌歌を歌うときは弦楽器の伴奏で歌うこと。)