Zefaniya 1 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 1:1-18

1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse

pa dziko lapansi,”

akutero Yehova.

3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;

ndidzawononga mbalame zamlengalenga

ndi nsomba za mʼnyanja.

Ndidzawononga anthu oyipa,

ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda

ndi onse okhala mu Yerusalemu.

Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,

mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:

5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo

kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,

amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,

komanso mʼdzina la Moleki,

6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,

osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.

7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,

chifukwa tsiku la Yehova layandikira.

Yehova wakonzekera kupereka nsembe;

wapatula iwo amene wawayitana.

8Pa tsiku la nsembe ya Yehova

ndidzalanga akalonga

ndi ana aamuna a mfumu

ndi onse amene amavala

zovala zachilendo.

9Pa tsiku limenelo ndidzalanga

onse amene safuna kuponda pa chiwundo,

amene amadzaza nyumba ya ambuye awo

ndi chiwawa ndi chinyengo.

10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,

“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,

kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,

ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.

11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;

a malonda anu onse adzapululidwa,

ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.

12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale

ndi kulanga onse amene sakulabadira,

amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,

amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,

chabwino kaya choyipa.’

13Chuma chawo chidzafunkhidwa,

nyumba zawo zidzagwetsedwa.

Adzamanga nyumba,

koma osakhalamo;

adzadzala minda ya mpesa

koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,

layandikira ndipo lifika msanga.

Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,

ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.

15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,

tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,

tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,

tsiku la mdima ndi lachisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,

tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa

ndi nsanja za pa ngodya.

17Ndidzabweretsa msautso pa anthu

ndipo adzayenda ngati anthu osaona,

chifukwa achimwira Yehova,

magazi awo adzamwazika ngati fumbi

ndi mnofu wawo ngati ndowe.

18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo

sadzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Dziko lonse lapansi lidzanyeka

mʼmoto wa nsanje yake

chifukwa adzakantha modzidzimutsa

onse okhala pa dziko lapansi.

Japanese Contemporary Bible

ゼパニヤ書 1:1-18

1

1表題――主からのことば。あて先――ゼパニヤ。彼はクシの子、ゲダルヤの孫、アマルヤの曾孫、ヒゼキヤの曾々孫。時代――ユダの王、アモンの子ヨシヤの治世。

主の日に下される全世界へのさばき

2主はこう言う。

「わたしは、おまえの国にあるものを一掃し、

徹底的に滅ぼす。

3人も動物もだ。

人間と人間が拝む偶像、すべては消え去る。

空の鳥も海の魚も死に絶える。

4わたしはこぶしでユダとエルサレムを打ち砕き、

残っているバアルの礼拝者を断ち滅ぼす。

偶像に仕える祭司を抹殺し、

そのため、彼らの記憶さえ消え去る。

5彼らは屋上に上って、太陽や月や星を拝んでいる。

『主に従っている』と言いながら、

モレクをも礼拝している。

わたしは、そんな彼らを滅ぼす。

6そして、以前は主を礼拝していたのに

今は礼拝していない者や、主を愛したことも

愛そうと思ったこともない者を滅ぼす。」

7静まって、主の前に立て。

主のさばきの恐ろしい日がくるからだ。

神はご自分の民を虐殺する手はずを整え、

死刑執行人を選んでいる。

8「さばきの日に、わたしはユダの指導者と君主たち、

それに異教の服を着ている者すべてを罰する。

9そうだ、異教の習慣に従う者や、

盗みや人殺しをほしいままにして、

主人の家を暴力と詐欺による邪悪な利得で満たす者を

罰する。

10警告を発する叫び声が、

エルサレムの中心から遠く離れた門から上がり、

だんだん近づいてきて、ついに前進する軍勢の音が、

町が立っている丘の頂に達する。

11エルサレムの民よ、泣き悲しめ。

町の貪欲な商売人、高利貸しは一人残らず死ぬのだ。

12わたしは、ともしびをかざして、

エルサレムの暗い隅々まで捜し回る。

罪にどっぷりつかり、神に関心を示さず、

神はそっとしておいてくれると考えている者たちを

見つけ出して罰するのだ。

13彼らの財産は敵に奪われ、家は荒らされる。

自分たちが建てた新しい家に住む機会は決してない。

自分たちが植えたぶどう畑のぶどう酒を

飲むことも決してない。

14その恐るべき日は近い。

急ぎ足でやってくる。

その日には、勇士たちも泣きくずれる。

15それは神の怒りが注ぎ出される日、

恐ろしい苦悩と苦痛の日、崩壊と荒廃の日、

暗闇と陰鬱、

暗雲と暗黒の日。

16角笛が吹き鳴らされ、ときの声が上がる。

城壁で囲まれた町と、最も強固な胸壁が崩れ落ちる。

17わたしは彼らを、

目が見えずに手探りで道を捜し回る人のように

無力にする。主に罪を犯したからだ。

それで、彼らの血はちりの中に注ぎ出され、

死体は地面に置かれたまま朽ちはてる。」

18あなたがたの金銀も、主の怒りの日には役に立たない。

そんなもので自分の身代金を払うことはできない。

神のねたみの炎が、全地をなめ尽くすからだ。

神はユダの民すべてをたちまちのうちに取り除く。