Habakuku 2 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 2:1-20

1Ndidzakhala pa malo anga aulonda,

ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo;

ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze,

ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.

Yankho la Yehova

2Tsono Yehova anandiyankha, nati:

“Lemba masomphenyawa

ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale

kuti wowerenga awawerenge mosavuta.

3Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake;

masomphenyawa akunena zamʼtsogolo

ndipo sizidzalephera kuchitika.

Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere;

zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.

4“Taona, mdani wadzitukumula;

zokhumba zake sizowongoka,

koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.

5Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo;

ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika.

Pakuti ngodzikonda ngati manda,

ngosakhutitsidwa ngati imfa,

wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu

ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse.

6“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti,

“Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake

ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda!

Kodi izi zidzachitika mpaka liti?

7Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi?

Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha?

Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.

8Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu,

mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo.

Pakuti wakhetsa magazi a anthu;

wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

9“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo,

kukweza malo ake okhalapo,

kuthawa mavuto!

10Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu,

kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.

11Mwala pa khoma udzafuwula,

ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.

12“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi

ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!

13Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize

kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto,

ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?

14Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova,

monga momwe madzi amadzazira nyanja.

15“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa,

kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera,

kuti aone umaliseche wawo.

16Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero.

Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere!

Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe,

ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.

17Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni,

ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga.

Pakuti wakhetsa magazi a anthu;

wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

18“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu,

kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza?

Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake;

amapanga mafano amene samatha kuyankhula.

19Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’

Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’

Kodi zimenezi zingathe kulangiza?

Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva;

mʼkati mwake mulibe mpweya.

20Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika;

dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

Japanese Contemporary Bible

ハバクク書 2:1-20

2

1今、私は見張り台に立ち、

神が私の訴えにどう答えるか待っていましょう。

主の答え

2すると主はこう言いました。

「板に、わたしの答えを書き記せ。

だれでもひと目で読んで

ほかの者にすぐ伝えることができるように、

大きな字で、はっきり書きなさい。

3だが、わたしが計画しているこのことは、

今すぐには起こらない。

ゆっくりと、着実に、確かに、

幻が実現する時が近づいている。

遅いように思えても、失望してはならない。

これらのことは必ず起こる。

忍耐していなさい。

ただの一日も遅れることはない。

4今から言うことをよく聞いておけ。

このカルデヤ人たちがそうするように、

悪者は自分だけを信頼して失敗する。

だが正しい人は、わたしを信頼して生きる。

5そのうえ、このおごり高ぶったカルデヤ人は、

自分たちのぶどう酒によって裏切られる。

ぶどう酒は人を欺くものだからだ。

彼らは貪欲で、多くの国をかき集めてきたが、

まるで死や地獄のように、決して満足しない。

6捕らえられた者たちが彼らをあざける時が

こようとしている。

『強盗ども。とうとう年貢の納め時だ。

人を虐げ、ゆすり取った当然の報いを受けろ』と。」

7「突然、おまえに借りのある者たちが怒って刃向かい、

おまえの持ち物を奪い取る。

その時、おまえはなすすべもなく立ち尽くし、

震える。

8おまえは多くの国を破滅させた。

今度はおまえが破滅する番だ。

人殺しめ。

おまえは田舎とすべての町を無法状態にした。

9邪悪な手段で富を得ながら、

危険を逃れて生きようとしているおまえは災いだ。

10殺人を犯すことで自分の名を辱め、

いのちさえ失っている。

11まさに、自分の家の壁の石がおまえを訴え、

天井の梁がそれに同調している。

12殺人と強奪で得た金で町を築くおまえは災いだ。

13主に逆らう国々の利益は

彼らの手の中で灰になると、主は定めていなかったか。

彼らがどんなに精を出しても、すべてが水の泡だ。

14(海が水で満たされているように、

全地が主の栄光を知ることで満たされる時がくる。)

15酔っぱらいをこづくように、

近隣の国々をよろめかせ、

その裸と恥を眺めて楽しんでいるおまえは災いだ。

16やがておまえの全盛期は終わり、辱められる。

神のさばきの杯を飲み干すがいい。

よろめいて倒れよ。

17おまえはレバノンの森を切り倒した。

今度はおまえが切り倒される。

おまえは罠で捕らえた野獣を恐ろしい目に会わせた。

今度はおまえが恐ろしい目に会う。

至るところの町々で、殺人と暴虐を行ったからだ。

18人間が造った偶像を拝んで、何の得があったのか。

そんな物が助けになるなど、全く愚かなうそだ。

自分で造った物を信頼していたとは、

なんと愚かな者か。

19いのちのない木の偶像に、

起きて自分たちを救えと命じる者、物言わぬ石に、

何をすべきか教えてほしいと呼びかける者は災いだ。

偶像は、神の代わりに語ることができるのか。

金銀で覆われているが、その中にいのちは全くない。

20しかし主は、ご自分の聖なる神殿にいる。

全地はその御前に静まれ。」