Habakuku 3 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 3:1-19

Pemphero la Habakuku

1Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

2Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;

Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.

Muzichitenso masiku athu ano,

masiku athu ano zidziwike;

mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

3Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,

Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.

Sela

Ulemerero wake unaphimba mlengalenga

ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.

4Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;

kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,

mʼmene anabisamo mphamvu zake.

5Patsogolo pake pankagwa mliri;

nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.

6Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;

anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.

Mapiri okhazikika anagumuka

ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.

Njira zake ndi zachikhalire.

7Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,

mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

8Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?

Kodi munakalipira timitsinje?

Kodi munapsera mtima nyanja

pamene munakwera pa akavalo anu

ndiponso magaleta anu achipulumutso?

9Munasolola uta wanu mʼchimake,

munayitanitsa mivi yambiri.

Sela

Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;

10mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.

Madzi amphamvu anasefukira;

nyanja yozama inakokoma

ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,

pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,

pa kunyezimira kwa mkondo wanu.

12Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,

ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.

13Munapita kukalanditsa anthu anu,

kukapulumutsa wodzozedwa wanu.

Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,

munawononga anthu ake onse.

Sela

14Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake

pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,

ankasangalala ngati kuti akudzawononga

osauka amene akubisala.

15Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,

kuvundula madzi amphamvu.

16Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,

milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;

mafupa anga anaguluka,

ndipo mawondo anga anawombana.

Komabe ndikuyembekezera mofatsa,

tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.

17Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,

ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.

Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,

ndipo mʼminda musatuluke kanthu.

Ngakhale nkhosa

ndi ngʼombe zithe mʼkhola,

18komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;

amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,

amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

La Bible du Semeur

Habaquq 3:1-19

Psaume

Dieu interviendra

1Prière d’Habaquq le prophète, sur le mode des complaintes3.1 Terme hébreu de sens inconnu..

2O Eternel, j’ai entendu ╵ce que tu viens de proclamer,

et je suis effrayé ╵devant ton œuvre, ô Eternel.

Dans le cours des années, ╵accomplis-la3.2 Voir 2.3. !

Dans le cours des années, ╵fais-la connaître !

Dans ta colère cependant, ╵pense à être clément !

3Dieu viendra de Témân,

le Saint viendra du mont Parân.

Pause

Sa majesté ╵couvre le ciel,

et sa louange ╵remplit la terre.

4Il a l’éclat de la lumière,

et, de sa main, ╵jaillissent deux rayons ;

c’est là qu’est le réservoir de sa force.

5La peste meurtrière ╵chemine devant lui,

et la fièvre brûlante ╵marche à sa suite.

6S’il vient à s’arrêter, ╵il fait vibrer3.6 Autre traduction : il mesure. la terre.

Quand il regarde, ╵il ébranle les peuples,

les montagnes antiques ╵sont disloquées,

et les collines ╵des anciens temps s’effondrent.

Il parcourt à nouveau ╵les antiques sentiers.

7J’ai vu les tentes de Koushân3.7 Probablement une peuplade nomade du désert du Sinaï. ╵réduites à néant ;

les abris de Madian ╵tremblaient, épouvantés.

L’Eternel sort pour délivrer son peuple

8Est-ce contre les fleuves ╵que l’Eternel s’irrite,

est-ce contre les fleuves ╵que ton courroux s’enflamme ?

Est-ce contre la mer ╵que ta fureur s’exerce,

pour que tu viennes ainsi ╵monté sur tes chevaux,

sur tes chars victorieux ?

9Ton arc est mis à nu,

tes traits sont les serments ╵que tu as prononcés3.9 Autre traduction : tes traits sont ceux que tu as juré d’utiliser..

Pause

Tu crevasses la terre, ╵livrant passage aux fleuves.

10Les montagnes t’ont vu, ╵et elles tremblent.

Des trombes d’eau s’abattent,

l’abîme se met à mugir,

lançant bien haut ses vagues.

11Le soleil et la lune ╵restent dans leur demeure

devant l’éclat ╵de tes flèches qui partent

et la clarté ╵des éclairs de ta lance.

12Avec colère, tu parcours la terre,

tu foules les peuples aux pieds ╵dans ton indignation.

13Oui, tu t’es mis en route ╵pour délivrer ton peuple,

et pour sauver ton roi ╵qui a reçu l’onction.

Tu as décapité ╵la maison du méchant,

et tu l’as démolie ╵de fond en comble.

Pause

14Tu transperces la tête ╵de l’ennemi ╵avec ses propres flèches,

alors qu’il arrivait ╵comme un vent d’ouragan ╵dans le but de nous disperser.

Déjà nos ennemis ╵se réjouissaient,

comptant bien dévorer ╵l’opprimé en secret3.14 Sens incertain. Autre traduction : dans sa cachette..

15Tu as lancé ╵tes chevaux dans la mer,

dans le bouillonnement ╵des eaux puissantes.

L’Eternel est ma force

16J’ai entendu cette nouvelle :

j’en suis tout bouleversé.

Mes lèvres balbutient

et mes os se dissolvent,

je reste là, tremblant.

Puisqu’il me faut attendre sans bouger, ╵le jour où la détresse

fondra sur l’ennemi ╵qui doit nous assaillir.

17Car le figuier ╵ne bourgeonnera plus,

et il n’y aura plus ╵de raisins dans les vignes,

le fruit de l’olivier ╵trompera les espoirs,

les champs ne produiront ╵plus de pain à manger.

Les moutons et les chèvres ╵disparaîtront de leurs enclos,

et les bovins de leurs étables.

18Mais moi, c’est à cause de l’Eternel ╵que je veux me réjouir,

j’exulterai de joie ╵à cause du Dieu qui me sauve.

19L’Eternel, le Seigneur, ╵c’est lui ma force :

il rend mes pieds pareils ╵à ceux des biches,

il me fait cheminer ╵sur les lieux élevés.

Pour le chef des musiciens. A chanter avec accompagnement d’instruments à cordes.