1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi
2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse
pa dziko lapansi,”
akutero Yehova.
3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;
ndidzawononga mbalame zamlengalenga
ndi nsomba za mʼnyanja.
Ndidzawononga anthu oyipa,
ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”
akutero Yehova.
Chenjezo kwa Yuda
4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda
ndi onse okhala mu Yerusalemu.
Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,
mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo
kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,
amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,
komanso mʼdzina la Moleki,
6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,
osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,
chifukwa tsiku la Yehova layandikira.
Yehova wakonzekera kupereka nsembe;
wapatula iwo amene wawayitana.
8Pa tsiku la nsembe ya Yehova
ndidzalanga akalonga
ndi ana aamuna a mfumu
ndi onse amene amavala
zovala zachilendo.
9Pa tsiku limenelo ndidzalanga
onse amene safuna kuponda pa chiwundo,
amene amadzaza nyumba ya ambuye awo
ndi chiwawa ndi chinyengo.
10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,
“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,
kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,
ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;
a malonda anu onse adzapululidwa,
ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale
ndi kulanga onse amene sakulabadira,
amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,
amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,
chabwino kaya choyipa.’
13Chuma chawo chidzafunkhidwa,
nyumba zawo zidzagwetsedwa.
Adzamanga nyumba,
koma osakhalamo;
adzadzala minda ya mpesa
koma sadzamwako vinyo wake.”
Tsiku Lalikulu la Yehova
14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,
layandikira ndipo lifika msanga.
Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,
ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,
tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,
tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,
tsiku la mdima ndi lachisoni,
tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,
tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa
ndi nsanja za pa ngodya.
17Ndidzabweretsa msautso pa anthu
ndipo adzayenda ngati anthu osaona,
chifukwa achimwira Yehova,
magazi awo adzamwazika ngati fumbi
ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo
sadzatha kuwapulumutsa
pa tsiku la ukali wa Yehova.
Dziko lonse lapansi lidzanyeka
mʼmoto wa nsanje yake
chifukwa adzakantha modzidzimutsa
onse okhala pa dziko lapansi.
1Parole que l’Eternel adressa sous le règne de Josias, fils d’Amôn, roi de Juda, à Sophonie, fils de Koushi, fils de Guedalia, descendant d’Amaria et d’Ezéchias1.1 Josias a régné de 640 à 609 av. J.-C. (2 R 22.1 à 23.30 ; 2 Ch 34 et 35)..
L’annonce du jugement
Le jugement universel
2Je vais tout balayer ╵de la surface de la terre,
l’Eternel le déclare.
3Je balaierai les hommes ╵de même que les bêtes,
je balaierai aussi ╵les oiseaux dans le ciel ╵et les poissons des mers,
tout ce qui fait ╵trébucher les méchants ;
je retrancherai les humains ╵de la surface de la terre,
l’Eternel le déclare.
Contre les idolâtres
4Je vais lever la main ╵contre le peuple de Juda
et contre tous ceux qui habitent ╵Jérusalem,
je supprimerai de ce lieu ╵ce qui subsiste de Baal.
Je ferai disparaître ╵le souvenir ╵de ses desservants effrénés1.4 Le terme hébreu correspondant désigne toujours des prêtres cananéens ou idolâtres (voir 2 R 23.5 ; Os 10.5).
avec ses prêtres,
5je ferai disparaître ╵tous ceux qui se prosternent ╵devant l’armée du ciel1.5 Les astres auxquels certains Juifs rendaient un culte (2 R 21.3-5, 21-22). ╵sur les toits des maisons,
et ceux qui se prosternent ╵devant l’Eternel et jurent par lui
tout en prêtant serment ╵au nom du dieu Molok1.5 Autre traduction : de leur roi. Les versions ont : Milkom, dieu des Ammonites, divinité à caractère politique (1 R 11.5, 33).,
6et ceux qui se détournent ╵de l’Eternel,
qui ne se soucient pas de lui
et qui ne le consultent pas.
Contre les grands
7Que l’on fasse silence ╵devant le Seigneur, l’Eternel !
Car il est proche, ╵le jour de l’Eternel1.7 Voir Es 13.6-9 ; Ez 20.2-3 ; Am 5.18 ; Ab 15 ; Jl 1.15 ; 2.1-2, 10-11 ; 3.3-4 ; 4.14-16..
L’Eternel a prévu ╵un sacrifice
et il a convoqué ╵ceux qui sont invités.
8Au jour du sacrifice ╵de l’Eternel,
j’interviendrai moi-même ╵contre les ministres du roi, ╵contre la cour
et contre tous ceux qui s’habillent ╵à la mode étrangère.
9En ce jour-là, j’interviendrai
contre ceux qui sautillent ╵sur les marches du trône,
contre ceux qui remplissent ╵de violence et de fraude ╵la maison de leur maître1.9 Allusion à l’empressement des courtisans. Certains traduisent sur les marches du trône par : par-dessus le seuil, ce qui renverrait à une pratique païenne (voir 1 S 5.5). maître: autre traduction : le temple de leur dieu..
Contre les trafiquants
10On entendra, en ce jour-là,
l’Eternel le déclare,
près de la porte des Poissons1.10 Porte de l’ancienne Jérusalem, au nord-ouest., ╵des cris retentissants,
des hurlements ╵dans le nouveau quartier1.10 Au nord-ouest de l’ancienne ville.
et, venant des collines, ╵un fracas formidable.
11Habitants de la ville basse1.11 Autre traduction : du quartier du Mortier. Ce quartier se trouvait dans la vallée du Tyropéon, juste au sud du mont Morija ; des marchands y vivaient., ╵hurlez,
parce qu’il est anéanti ╵le peuple des marchands,
tous ceux qui croulent sous l’argent1.11 Autre traduction : tous les peseurs d’argent. ╵vont être exterminés.
Contre les parvenus
12En ce temps-là,
je fouillerai Jérusalem ╵avec des torches
et je châtierai tous les hommes
qui croupissent tel un vin sur sa lie,
se disant en eux-mêmes
que l’Eternel ne fait ╵ni du bien ni du mal.
13Leurs richesses seront pillées,
leurs maisons dévastées.
Ils auront bâti des demeures
mais ils n’y habiteront pas ;
ils auront planté des vignobles
mais ils n’en boiront pas le vin.
Le jour de l’Eternel
14Car voici qu’il est proche, ╵le jour de l’Eternel,
oui, ce grand jour est proche, ╵il arrive à grands pas,
on entendra des cris amers ╵au jour de l’Eternel.
Le guerrier le plus brave ╵poussera de grands cris.
15En effet, ce jour-là ╵est un jour de colère,
c’est un jour de détresse ╵et de malheur,
un jour de destruction ╵et de désolation,
un jour d’obscurité ╵et d’épaisses ténèbres,
c’est un jour de nuages ╵et de brouillards épais,
16jour où retentiront ╵la sonnerie du cor ╵et des clameurs de guerre
contre les villes fortes
et les hautes tours d’angle.
17Je plongerai les hommes ╵dans la détresse,
et, comme des aveugles, ╵ils marcheront en tâtonnant
parce qu’ils ont péché ╵contre moi, l’Eternel.
Leur sang sera versé ╵comme de la poussière
et, comme des ordures, ╵leurs corps seront jetés1.17 Autre traduction : leurs entrailles seront répandues..
18Leur argent et leur or ╵ne pourront les sauver
au jour de la colère ╵de l’Eternel,
lorsqu’il consumera ╵la terre tout entière1.18 Autre traduction : le pays tout entier.
par le feu de son amour bafoué1.18 Voir 3.8..
Car il provoquera, ╵ – et ce sera épouvantable –
la destruction totale ╵de tous ceux qui habitent sur la terre1.18 Autre traduction : dans le pays..