Habakuku 2 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 2:1-20

1Ndidzakhala pa malo anga aulonda,

ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo;

ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze,

ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.

Yankho la Yehova

2Tsono Yehova anandiyankha, nati:

“Lemba masomphenyawa

ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale

kuti wowerenga awawerenge mosavuta.

3Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake;

masomphenyawa akunena zamʼtsogolo

ndipo sizidzalephera kuchitika.

Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere;

zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.

4“Taona, mdani wadzitukumula;

zokhumba zake sizowongoka,

koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.

5Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo;

ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika.

Pakuti ngodzikonda ngati manda,

ngosakhutitsidwa ngati imfa,

wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu

ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse.

6“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti,

“Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake

ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda!

Kodi izi zidzachitika mpaka liti?

7Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi?

Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha?

Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.

8Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu,

mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo.

Pakuti wakhetsa magazi a anthu;

wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

9“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo,

kukweza malo ake okhalapo,

kuthawa mavuto!

10Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu,

kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.

11Mwala pa khoma udzafuwula,

ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.

12“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi

ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!

13Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize

kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto,

ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?

14Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova,

monga momwe madzi amadzazira nyanja.

15“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa,

kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera,

kuti aone umaliseche wawo.

16Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero.

Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere!

Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe,

ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.

17Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni,

ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga.

Pakuti wakhetsa magazi a anthu;

wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

18“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu,

kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza?

Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake;

amapanga mafano amene samatha kuyankhula.

19Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’

Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’

Kodi zimenezi zingathe kulangiza?

Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva;

mʼkati mwake mulibe mpweya.

20Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika;

dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Habakuki 2:1-20

12:1 Isa 21:8; Za 48:13; 85:8; Eze 3:17; Za 73:16, 17; 5:3Nitasimama katika zamu yangu,

na kujiweka mwenyewe juu ya maboma;

nitatazama nione atakaloniambia,

na ni jibu gani nitakalotoa kuhusu lalamiko hili.

Jibu La Bwana

22:2 Isa 8:1; 30:8; Kum 27:8; Rum 4:24; 15:4; Yer 36:2; Eze 24:2; Ufu 1:19Kisha Bwana akajibu:

“Andika ufunuo huu,

na ukaufanye wazi juu ya vibao,

ili mpiga mbiu akimbie nao.

32:3 Dan 10:14; 11:27; 8:17; Za 27:14; Eze 12:25Kwa kuwa ufunuo huu unasubiri wakati uliokubalika;

unazungumzia mambo ya mwisho,

na kamwe hautakosea.

Iwapo utakawia, wewe usubiri;

kwa hakika utakuja na hautachelewa.

42:4 Eze 18:9; Yn 3:36; 2Kor 5:7; Rum 1:17; Gal 3:11; Ebr 10:37-38“Tazama, amejaa majivuno;

anavyovitamani si vya unyofu:

lakini mwenye haki ataishi kwa imani yake:

52:5 Mit 20:1; Isa 2:11; Mit 27:20; 30:15-16; Hab 1:9hakika mvinyo humsaliti;

ni mwenye kiburi na hana amani.

Kwa sababu ni mlafi kama kuzimu

na kama kifo kamwe hatosheki;

anajikusanyia mataifa yote

na kuchukua watu wote mateka.

62:6 Isa 14:4; Amo 2:8“Je, watu wote hawatamsuta kwa dhihaka na kumbeza, wakisema,

“ ‘Ole wake yeye akusanyaye bidhaa zilizoibwa

na kujifanyia utajiri kwa kutoza kwa nguvu!

Ataendelea hivi kwa muda gani?’

72:7 Mit 29:1Je, wadai wako hawatainuka ghafula?

Je, hawataamka na kukufanya utetemeke?

Kisha utakuwa mhanga kwao.

82:8 Zek 1:122:8 Isa 33:1; Yer 50:17-18; Oba 1:15; Zek 2:8-9; Eze 39:10Kwa kuwa umeteka nyara mataifa mengi,

watu waliobaki watakuteka nyara wewe.

Kwa kuwa umemwaga damu ya mtu;

umeharibu nchi na miji, na kila mmoja ndani yake.

92:9 Yer 22:13; 51:13; Ay 39:27; Isa 10:14“Ole wake yeye ajengaye milki yake kwa mapato ya udhalimu,

awekaye kiota chake juu,

ili kukimbia makucha ya uharibifu!

102:10 Yer 26:19; Nah 3:6Umefanya shauri la maangamizi ya watu wengi,

ukiaibisha nyumba yako mwenyewe, na kupotewa na maisha yako.

112:11 Yos 24:27; Zek 5:4; Lk 19:40Mawe ya kuta yatapiga kelele,

na mihimili ya kazi ya mbao itarudisha mwangwi wake.

122:12 Eze 22:2; Mik 3:10“Ole wake yeye ajengaye mji kwa kumwaga

damu na kuusimamisha mji kwa uhalifu!

132:13 Isa 50:11; 47:13Je, Bwana Mwenye Nguvu Zote hakuonyesha

kwamba kazi ya wanadamu ni mafuta tu kwa ajili ya moto,

na kwamba mataifa

yanajichosha bure?

142:14 Kut 16:7; Hes 14:21; Isa 11:9Kwa kuwa dunia itajazwa na maarifa ya utukufu wa Bwana,

kama maji yaifunikavyo bahari.

152:15 Mit 23:20“Ole wake yeye awapaye jirani zake kileo,

akiimimina kutoka kwenye kiriba

cha mvinyo mpaka wamelewa,

ili apate kutazama miili yao iliyo uchi.

162:16 Eze 23:32-34; Hos 4:7; Law 10:9; Mao 4:21; Za 16:5; Isa 51:22Utajazwa na aibu badala ya utukufu.

Sasa ni zamu yako! Kunywa na ujifunue!

Kikombe kutoka kwenye mkono wa kuume wa Bwana kinakujia,

na aibu itafunika utukufu wako.

172:17 Yer 50:33; 51:35; 50:15Ukatili ulioifanyia Lebanoni utakufunika,

na uharibifu uliowafanyia wanyama utakutisha.

Kwa sababu umemwaga damu ya mtu;

umeharibu nchi na miji na kila mmoja aliyeko ndani yake.

182:18 1Sam 12:21; Amu 10:14; Isa 40:19; Yer 5:21; 14:22; 10:14; 1Kor 12:2“Sanamu ina thamani gani,

kwani mwanadamu ndiye alichonga?

Ama kinyago kinachofundisha uongo?

Kwa kuwa yeye aliyekitengeneza

hutegemea kazi ya mikono yake mwenyewe;

hutengeneza sanamu zisizoweza kuzungumza.

192:19 1Fal 18:27; Yer 10:4; Hos 4:12; Dan 5:4, 23Ole wake yeye auambiaye mti, ‘Uwe hai!’

Ama asemaye na jiwe lisilo na uhai, ‘Amka!’

Je, linaweza kuongoza?

Limefunikwa kwa dhahabu na fedha;

hakuna pumzi ndani yake.

202:20 Za 11:4; Isa 41:1Lakini Bwana yuko katika Hekalu lake takatifu;

dunia yote na inyamaze mbele yake.”