Habakuku 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 1:1-17

1Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.

Dandawulo la Habakuku

2Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani,

koma wosayankha?

Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!”

koma wosatipulumutsa?

3Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa?

Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa?

Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa;

pali ndewu ndi kukangana kwambiri.

4Kotero malamulo anu atha mphamvu,

ndipo chilungamo sichikugwira ntchito.

Anthu oyipa aposa olungama,

kotero apotoza chilungamo.

Yankho la Yehova

5“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani,

ndipo muthedwe nazo nzeru.

Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu

zimene inu simudzazikhulupirira,

ngakhale wina atakufotokozerani.

6Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni,

anthu ankhanza ndiponso amphamvu,

amene amapita pa dziko lonse lapansi

kukalanda malo amene si awo.

7Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa;

amadzipangira okha malamulo

ndi kudzipezera okha ulemu.

8Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku

ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo.

Okwerapo awo akuthamanga molunjika;

a pa akavalo awo ndi ochokera kutali,

akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;

9onse akubwera atakonzekera zachiwawa.

Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu

ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.

10Akunyoza mafumu

ndiponso kuchitira chipongwe olamulira.

Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa;

akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.

11Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe,

anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”

Dandawulo Lachiwiri la Habakuku

12Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire?

Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa.

Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo;

Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.

13Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa;

Inu simulekerera cholakwa.

Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa?

Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa

akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?

14Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,

ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.

15Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza,

amawakola mu ukonde wake,

amawasonkhanitsa mu khoka lake;

kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.

16Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake

ndiponso kufukizira lubani khoka lake,

popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba

ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.

17Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo,

kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Habakuki 1:1-17

11:1 Nah 1:1Neno alilopokea nabii Habakuki.

Lalamiko La Habakuki

21:2 Za 13:1-2; 22:1-2; 6:3; 27:7; Yer 14:9Ee Bwana, hata lini nitakuomba msaada,

lakini wewe husikilizi?

Au kukulilia, “Udhalimu!”

Lakini hutaki kuokoa?

31:3 Ay 9:23; Yer 20:8; Za 55:9Kwa nini unanifanya nitazame dhuluma?

Kwa nini unavumilia makosa?

Uharibifu na udhalimu viko mbele yangu;

kuna mabishano na mapambano kwa wingi.

41:4 Ay 12:6; Za 12:8; 58:2Kwa hiyo sheria imepotoshwa,

nayo haki haipo kabisa.

Waovu wanawazunguka wenye haki,

kwa hiyo haki imepotoshwa.

Jibu La Bwana

5“Yatazame mataifa,

uangalie na ushangae kabisa.

Kwa sababu katika siku zako nitafanya kitu

ambacho hungeamini,

hata kama ungeambiwa.

6Nitawainua Wakaldayo,

watu hao wakatili na wenye haraka,

ambao hupita dunia yote

kuteka mahali pa kuishi pasipo pao wenyewe.

7Ni watu wanoogopwa na wanaotisha;

wenyewe ndio sheria yao,

na huinua heshima yao wenyewe.

8Farasi wao ni wepesi kuliko chui,

na wakali kuliko mbwa mwitu wakati wa machweo.

Askari wapanda farasi wao huenda mbio;

waendesha farasi wao wanatoka mbali.

Wanaruka kasi kama tai ili kurarua;

91:9 Hab 2:5wote wanakuja tayari kwa fujo.

Makundi yao ya wajeuri yanasonga mbele

kama upepo wa jangwani,

na kukusanya wafungwa

kama mchanga.

101:10 2Nya 36:6; Yer 33:4Wanawabeza wafalme,

na kuwadhihaki watawala.

Wanaicheka miji yote iliyozungushiwa maboma;

wanafanya malundo ya udongo na kuiteka hiyo miji.

111:11 Yer 4:11-12; Dan 4:30Kisha wanapita kasi kama upepo na kusonga mbele:

watu wenye hatia, ambao nguvu zao ndio mungu wao.”

Lalamiko La Pili La Habakuki

121:12 Mwa 21:33; Isa 31:1; 37:23; Kut 33:22; Isa 10:6; Mwa 49:24; Za 118:17Ee Bwana, je, wewe sio wa tangu milele?

Mungu wangu, Uliye Mtakatifu wangu, hatutakufa.

Ee Bwana, umewachagua wao ili watekeleze hukumu;

Ee Mwamba, umewaamuru watuadhibu.

131:13 Za 18:26; Mao 3:34-36; Za 25:3; Ay 21:7Macho yako ni safi mno hata yasiweze kuutazama uovu,

wala huwezi kuvumilia makosa.

Kwa nini basi unawavumilia wadanganyifu?

Kwa nini unakuwa kimya wakati waovu

wanawameza wale wenye haki

kuliko wao wenyewe?

14Umewafanya watu kama samaki baharini,

kama viumbe wa bahari wasio na mtawala.

151:15 Yer 5:26; Isa 19:8; Ay 18:8; Yer 16:16Adui mwovu anawavuta wote kwa ndoana,

anawakamata katika wavu wake,

anawakusanya katika juya lake;

kwa hiyo anashangilia na anafurahi.

161:16 Yer 44:8Kwa hiyo anatoa kafara kwa wavu wake,

na kuchoma uvumba kwa juya lake,

kwa kuwa kwa wavu wake anaishi kwa starehe,

na anafurahia chakula kizuri.

171:17 Isa 14:6; 19:8Je, aendelee kuwatoa walio katika wavu wake,

akiangamiza mataifa bila huruma?