Zefaniya 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 1:1-18

1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse

pa dziko lapansi,”

akutero Yehova.

3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;

ndidzawononga mbalame zamlengalenga

ndi nsomba za mʼnyanja.

Ndidzawononga anthu oyipa,

ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda

ndi onse okhala mu Yerusalemu.

Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,

mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:

5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo

kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,

amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,

komanso mʼdzina la Moleki,

6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,

osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.

7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,

chifukwa tsiku la Yehova layandikira.

Yehova wakonzekera kupereka nsembe;

wapatula iwo amene wawayitana.

8Pa tsiku la nsembe ya Yehova

ndidzalanga akalonga

ndi ana aamuna a mfumu

ndi onse amene amavala

zovala zachilendo.

9Pa tsiku limenelo ndidzalanga

onse amene safuna kuponda pa chiwundo,

amene amadzaza nyumba ya ambuye awo

ndi chiwawa ndi chinyengo.

10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,

“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,

kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,

ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.

11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;

a malonda anu onse adzapululidwa,

ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.

12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale

ndi kulanga onse amene sakulabadira,

amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,

amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,

chabwino kaya choyipa.’

13Chuma chawo chidzafunkhidwa,

nyumba zawo zidzagwetsedwa.

Adzamanga nyumba,

koma osakhalamo;

adzadzala minda ya mpesa

koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,

layandikira ndipo lifika msanga.

Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,

ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.

15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,

tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,

tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,

tsiku la mdima ndi lachisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,

tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa

ndi nsanja za pa ngodya.

17Ndidzabweretsa msautso pa anthu

ndipo adzayenda ngati anthu osaona,

chifukwa achimwira Yehova,

magazi awo adzamwazika ngati fumbi

ndi mnofu wawo ngati ndowe.

18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo

sadzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Dziko lonse lapansi lidzanyeka

mʼmoto wa nsanje yake

chifukwa adzakantha modzidzimutsa

onse okhala pa dziko lapansi.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Sefania 1:1-18

11:1 2Fal 22:1; 2Tim 3:16; 2Pet 1:21; 1Nya 3:14Neno la Bwana lililomjia Sefania mwana wa Kushi, mwana wa Gedalia, mwana wa Amaria, mwana wa Hezekia, wakati wa utawala wa Yosia mwana wa Amoni mfalme wa Yuda:

Onyo La Maangamizi Yanayokuja

21:2 Mwa 6:7Bwana asema,

“Nitafagia kila kitu

kutoka kwenye uso wa dunia.”

31:3 Yer 4:25; 50:3; Hos 4:3; Eze 14:17“Nitafagilia mbali watu na wanyama;

nitafagilia mbali ndege wa angani

na samaki wa baharini.

Wafanyao maovu watapata tu kokoto,

nami nitamkatilia mbali mwanadamu atoke katika dunia,”

asema Bwana.

Dhidi Ya Yuda

41:4 Yer 6:12; 15:6; Mik 5:13; Sef 2:11; Hos 10:5“Nitaiadhibu Yuda

na wote wakaao Yerusalemu.

Kutoka mahali hapa nitakatilia mbali

kila mabaki ya Baali,

majina ya wapagani na makuhani

waabuduo sanamu:

51:5 Yer 5:7; 8:2; 1Fal 11:33; Law 18:21wale ambao husujudu juu ya mapaa

kuabudu jeshi la vitu vya angani,

wale ambao husujudu na kuapa kwa Bwana

na ambao pia huapa kwa Malkamu,

61:6 Yer 2:13; Isa 9:13; Hos 7:7wale wanaoacha kumfuata Bwana,

wala hawamtafuti Bwana

wala kutaka shauri lake.

71:7 Isa 13:6; 41:1; Eze 7:19; Yoe 3:14; Amo 5:18-20; Yer 46:10Nyamazeni mbele za Bwana Mwenyezi,

kwa maana siku ya Bwana iko karibu.

Bwana ameandaa dhabihu,

amewaweka wakfu wale aliowaalika.

81:8 Isa 24:21; Yer 39:6Katika siku ya dhabihu ya Bwana

nitawaadhibu wakuu

na wana wa mfalme

na wale wote wanaovaa

nguo za kigeni.

91:9 1Sam 5:5; Amo 3:10Katika siku hiyo nitaadhibu wote ambao

hukwepa kukanyaga kizingiti,

ambao hujaza hekalu la miungu yao

kwa dhuluma na udanganyifu.”

101:10 Isa 22:5; Neh 3:13; 2Nya 33:14; Amo 5:16Bwana asema, “Katika siku hiyo

kilio kitapanda juu kutoka lango la Samaki,

maombolezo kutoka mtaa wa pili,

na mshindo mkubwa kutoka vilimani.

111:11 Yak 5:1; Hos 9:6; Ufu 18:11, 12Ombolezeni, ninyi mnaoishi katika eneo la sokoni;

wafanyabiashara wenu wote wameangamizwa,

wote ambao wanafanya biashara ya fedha

wataangamizwa.

121:12 Amo 6:1; Ay 21:15; Za 10:11-13; Yer 48:11; Eze 8:12; 2Fal 21:16; Ay 22:13Wakati huo nitasaka mji wa Yerusalemu kwa taa,

na kuwaadhibu wale ambao

wanakaa katika hali ya kuridhika,

ambao ni kama divai

iliyobaki kwenye machicha,

ambao hudhani, ‘Bwana hatafanya lolote,

jema au baya.’

131:13 2Fal 24:13; Yer 15:13; Mik 6:15; Kum 28:30-39; Mao 5:2; Amo 5:11Utajiri wao utatekwa nyara,

nyumba zao zitabomolewa.

Watajenga nyumba,

lakini hawataishi ndani yake;

watapanda mizabibu

lakini hawatakunywa divai yake.

Siku Kubwa Ya Bwana

141:14 Yer 30:7; Ufu 6:17; Yoe 1:15; 2:1; Mal 4:5; Eze 7:7; Dan 7:13“Siku kubwa ya Bwana iko karibu:

iko karibu na inakuja haraka.

Sikilizeni! Kilio katika siku ya Bwana

kitakuwa kichungu,

hata shujaa atapiga kelele.

151:15 1Sam 2:9; Mk 13:24-25; Yoe 2:2Siku ile ni siku ya ghadhabu,

siku ya fadhaa na dhiki,

siku ya uharibifu na ukiwa,

siku ya giza na utusitusi,

siku ya mawingu na giza nene,

161:16 Yer 4:19; 8:16; Hos 5:8; Amo 3:6; Kum 28:52; Isa 2:15siku ya tarumbeta na mlio wa vita

dhidi ya miji yenye ngome

na dhidi ya minara mirefu.

171:17 Kum 28:52; Isa 59:10; Yer 9:22; Za 79:3; 83:10Nitawaletea watu dhiki,

nao watatembea kama vipofu,

kwa sababu wametenda dhambi

dhidi ya Bwana.

Damu yao itamwagwa kama vumbi

na matumbo yao kama taka.

181:18 Ay 20:20; 40:11; Eze 7:11; 7:19; Kum 29:20; Sef 3:8; Mwa 6:7Fedha yao wala dhahabu yao

hazitaweza kuwaokoa

katika siku hiyo ya ghadhabu ya Bwana.

Katika moto wa wivu wake

dunia yote itateketezwa,

kwa maana ataleta mwisho

wa wote wanaoishi katika dunia ghafula.”