Genesis 37 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 37:1-36

Maloto a Yosefe

1Yakobo ankakhala mʼdziko la Kanaani kumene abambo ake ankakhala.

2Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi:

Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake.

3Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali. 4Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.

5Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda. 6Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota: 7Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”

8Abale ake aja anamufunsa nati, “Kodi ukuyesa kuti ungakhale mfumu yathu? Ungadzatilamuliredi iweyo?” Ndipo anamuda kuposa kale chifukwa cha maloto ake ndi zimene ankakonda kunena kwa abambo awo.

9Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”

10Atawuza abambo ake ndi abale ake malotowa, abambo ake anamukalipira nati, “Ndi maloto anji umalotawa? Kodi uganiza kuti ine, amayi ako pamodzi ndi abale ako onsewa tingadzabwere kudzakugwandira iwe?” 11Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.

Yosefe Agulitsidwa ndi Abale Ake

12Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu, 13ndipo Israeli anati kwa Yosefe, “Tsono, ndikufuna kukutuma kwa abale ako.”

Iye anayankha nati, “Chabwino.”

14Choncho anati kwa iye, “Pita ukaone ngati abale ako ali bwino. Ukaonenso nkhosa ngati zili bwino. Kenaka ubwere udzandiwuze.” Choncho Israeli anatuma Yosefe kuchokera ku chigwa cha Hebroni.

Yosefe atafika ku Sekemu, 15munthu wina anamupeza akungozungulirazungulira mʼmunda ndipo anamufunsa, “Ukufunafuna chiyani?”

16Iye anayankha, “Ndikufuna abale anga. Mungandiwuze kumene akudyetsa ziweto zawo?”

17Munthuyo anayankha nati, “Anasamukako kuno. Ndinawamva akuti, ‘Tiyeni tipite ku Dotani.’ ”

Choncho Yosefe analondola abale ake ndipo anakawapeza ku Dotani. 18Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.

19Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja. 20Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”

21Koma Rubeni atamva izi, anapulumutsa Yosefe. Iye anati kwa abale ake, “Ayi, tisamuphe, 22tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”

23Choncho Yosefe atafika kwa abale ake, iwo anamuvula mkanjo wake wamanja aatali uja umene anavala 24ndipo anamutenga namuponya mʼchitsime chopanda madzi komanso mopanda chilichonse.

25Atakhala pansi kuti adye chakudya, anatukula maso naona gulu la Aismaeli akubwera kuchokera ku Giliyadi. Ngamira zawo zinanyamula zonunkhiritsa bwino zakudya zamitundumitundu, ndipo zimenezi ankapita nazo ku Igupto.

26Yuda anafunsa abale ake nati, “Kodi tidzapindula chiyani tikapha mʼbale wathuyu ndi kuphimbitsa magazi ake? 27Bwanji timugulitse kwa Aismaeliwa, koma ife tisamuchite kanthu kalikonse. Ameneyu ndi mʼbale wathu thupi limodzi ndi ife.” Abale ake anavomereza zimenezi.

28Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.

29Rubeni atabwerera ku chitsime kuja anapeza kuti Yosefe mulibe mʼchitsimemo. Pamenepo iye anangʼamba zovala zake 30nabwerera kwa abale ake nati, “Mnyamata uja mulibemo! Nanga ndilowere kuti ine tsopano?”

31Tsono anapha kamwana ka mbuzi, natenga mkanjo wa Yosefe ndi kuwunyika mʼmagazi ake. 32Iwo anatenga mkanjo uja nabwerera nawo kwa abambo awo nati, “Ife tapeza mkanjowu. Tawuyangʼanitsitsani muone ngati uli wa mwana wanu.”

33Iye anawuzindikira ndipo anati, “Ndi mkanjo wa mwana wanga umenewu! Nyama yakuthengo yolusa yamudya. Mosakayika, mwana wanga Yosefe wakhadzulidwa.”

34Pamenepo Yakobo anangʼamba zovala zake, navala chisaka mʼchiwuno mwake. Iye analira maliro a mwana wake masiku ambiri. 35Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake.

36Amidiyani aja anagulitsa Yosefe kwa Potifara, mmodzi mwa nduna za Farao ku Igupto. Potifarayu anali mkulu wa asilikali olonda nyumba ya Farao.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 37:1-36

خوابهای يوسف

1يعقوب بار ديگر در كنعان يعنی سرزمينی كه پدرش در آن اقامت كرده بود، ساكن شد. 2در اين زمان يوسف پسر يعقوب هفده ساله بود. او برادران ناتنی خود را كه فرزندان بلهه و زلفه كنيزان پدرش بودند، در چرانيدن گوسفندان پدرش كمک می‌كرد. يوسف كارهای ناپسندی را كه از آنان سر می‌زد به پدرش خبر می‌داد. 3يعقوب يوسف را بيش از ساير پسرانش دوست می‌داشت، زيرا يوسف در سالهای آخر عمرش به دنيا آمده بود، پس جامه‌ای رنگارنگ به يوسف داد. 4برادرانش متوجه شدند كه پدرشان او را بيشتر از آنها دوست می‌دارد؛ در نتيجه آنقدر از يوسف متنفر شدند كه نمی‌توانستند به نرمی با او سخن بگويند. 5يک شب يوسف خوابی ديد و آن را برای برادرانش شرح داد. اين موضوع باعث شد كينهٔ آنها نسبت به يوسف بيشتر شود.

6او به ايشان گفت: «گوش كنيد تا خوابی را كه ديده‌ام برای شما تعريف كنم. 7در خواب ديدم كه ما در مزرعه بافه‌ها را می‌بستيم. ناگاه بافهٔ من بر پا شد و ايستاد و بافه‌های شما دور بافهٔ من جمع شدند و به آن تعظيم كردند.»

8برادرانش به وی گفتند: «آيا می‌خواهی پادشاه شوی و بر ما سلطنت كنی!» پس خواب و سخنان يوسف بر كينه برادران او افزود.

9يوسف بار ديگر خوابی ديد و آن را برای برادرانش چنين تعريف كرد: «خواب ديدم كه آفتاب و ماه و يازده ستاره به من تعظيم می‌كردند.»

10اين بار خوابش را برای پدرش هم تعريف كرد؛ ولی پدرش او را سرزنش نموده، گفت: «اين چه خوابی است كه ديده‌ای؟ آيا واقعاً من و مادرت و برادرانت آمده، پيش تو تعظيم خواهيم كرد؟» 11برادرانش به او حسادت می‌كردند، ولی پدرش درباره خوابی كه يوسف ديده بود، می‌انديشيد.

فروخته شدن يوسف

12برادران يوسف گله‌های پدرشان را برای چرانيدن به شكيم برده بودند. 13‏-14يعقوب به يوسف گفت: «برادرانت در شكيم مشغول چرانيدن گله‌ها هستند. برو و ببين اوضاع چگونه است؛ آنگاه برگرد و به من خبر بده.»

يوسف اطاعت كرد و از دره حبرون به شكيم رفت. 15در آنجا شخصی به او برخورد و ديد كه وی در صحرا سرگردان است. او از يوسف پرسيد: «در جستجوی چه هستی؟»

16يوسف گفت: «در جستجوی برادران خود و گله‌هايشان می‌باشم. آيا تو آنها را ديده‌ای؟»

17آن مرد پاسخ داد: «بلی، من آنها را ديدم كه از اينجا رفتند و شنيدم كه می‌گفتند به دوتان می‌روند.» پس يوسف به دوتان رفت و ايشان را در آنجا يافت. 18همين كه برادرانش از دور ديدند يوسف می‌آيد، تصميم گرفتند او را بكشند.

19‏-20آنها به يكديگر گفتند: «خواب بيننده بزرگ می‌آيد! بياييد او را بكشيم و در يكی از اين چاهها بيندازيم و به پدرمان بگوييم جانور درنده‌ای او را خورده است. آن وقت ببينيم خوابهايش چه می‌شوند.»

21‏-22اما رئوبين چون اين را شنيد، به اميد اين كه جان او را نجات بدهد، گفت: «او را نكشيم. خون او را نريزيم، بلكه وی را در اين چاه بيندازيم. با اين كار بدون اين كه به او دستی بزنيم خودش خواهد مرد.» (رئوبين در نظر داشت بعداً او را از چاه بيرون آورد و نزد پدرش بازگرداند.)

23به محض اين كه يوسف نزد برادرانش رسيد، آنها بر او هجوم برده، جامهٔ رنگارنگی را كه پدرشان به او داده بود، از تنش بيرون آوردند. 24سپس او را در چاهی كه آب نداشت انداختند 25و خودشان مشغول خوردن غذا شدند. ناگاه از دور كاروان شتری را ديدند كه به طرف ايشان می‌آيد. آنها تاجران اسماعيلی بودند كه كتيرا و ادويه از جلعاد به مصر می‌بردند.

26‏-27يهودا به سايرين گفت: «نگاه كنيد، كاروان اسماعيليان می‌آيد. بياييد يوسف را به آنها بفروشيم. كُشتن او و مخفی كردن اين موضوع چه نفعی برای ما دارد؟ به هر حال او برادر ماست؛ نبايد به دست ما كشته شود.» برادرانش با پيشنهاد او موافقت كردند.

28وقتی تاجران رسيدند، برادران يوسف او را از چاه بيرون آورده، به بيست سكه نقره به آنها فروختند. آنها هم يوسف را با خود به مصر بردند. 29رئوبين كه هنگام آمدن كاروان در آنجا نبود، وقتی به سر چاه آمد و ديد كه يوسف در چاه نيست، از شدت ناراحتی جامهٔ خود را چاک زد. 30آنگاه نزد برادرانش آمده، به آنها گفت: «يوسف را برده‌اند و من نمی‌دانم كجا به دنبالش بروم؟»

31پس برادرانش بزی را سر بريده جامه زيبای يوسف را به خون بز آغشته نمودند. 32سپس جامهٔ آغشته به خون را نزد يعقوب برده، گفتند: «آيا اين همان جامه يوسف نيست؟ آن را در صحرا يافته‌ايم.»

33يعقوب آن را شناخت و فرياد زد: «آری، اين جامه پسرم است. حتماً جانور درنده‌ای او را دريده و خورده است.»

34آنگاه يعقوب جامهٔ خود را پاره كرده، پلاس پوشيد و روزهای زيادی برای پسرش ماتم گرفت. 35تمامی اهل خانواده‌اش سعی كردند وی را دلداری دهند، ولی سودی نداشت. او می‌گفت: «تا روز مرگم غم يوسف را نمی‌توانم فراموش كنم.» و همچنان از غم فرزندش می‌گريست.

36اما تاجران پس از اين كه به مصر رسيدند، يوسف را به فوطيفار، يكی از افسران فرعون فروختند. فوطيفار رئيس محافظان دربار بود.