Genesis 38 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 38:1-30

Yuda ndi Tamara

1Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira. 2Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi. 3Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri. 4Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani. 5Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.

6Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara. 7Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.

8Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.” 9Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake. 10Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.

11Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.

12Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.

13Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa, 14iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.

15Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope. 16Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake.

Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”

17Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.”

Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”

18Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?”

Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi. 19Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.

20Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo. 21Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?”

Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”

22Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’ ”

23Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”

24Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.”

Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”

25Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”

26Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.

27Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa. 28Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.” 29Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi. 30Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 38:1-30

يهودا و تامار

1در همان روزها بود كه يهودا خانهٔ پدر خود را ترک نموده، به عدولام رفت و نزد شخصی به نام حيره ساكن شد. 2در آنجا او دختر مردی كنعانی به نام شوعا را به زنی گرفت 3و از او صاحب پسری شد كه او را عير ناميد. 4شوعا بار ديگر حامله شد و پسری زاييد و او را اونان نام نهاد. 5وقتی آنها در كزيب بودند، زن يهودا پسر سوم خود را به دنيا آورد و او را شيله ناميد.

6وقتی عير، پسر ارشد يهودا، بزرگ شد پدرش دختری را به نام تامار برای او به زنی گرفت. 7اما چون عير شخص شروری بود، خداوند او را كُشت.

8آنگاه يهودا به اونان برادر عير گفت: «مطابق رسم ما، تو بايد با زن برادرت تامار ازدواج كنی تا نسل برادرت از بين نرود.» 9اونان با تامار ازدواج كرد، اما چون نمی‌خواست فرزندش از آنِ كس ديگری باشد، هر وقت با او نزديكی می‌كرد، جلوگيری نموده، نمی‌گذاشت تامار بچه‌ای داشته باشد كه از آنِ برادر مرده‌اش شود. 10اين كار اونان در نظر خداوند ناپسند آمد و خدا او را نيز كشت. 11يهودا به عروس خود تامار گفت: «به خانهٔ پدرت برو و بيوه بمان تا اين كه پسر كوچكم شيله بزرگ شود. آن وقت می‌توانی با او ازدواج كنی.» (ولی يهودا قلباً راضی به اين كار نبود، چون می‌ترسيد شيله نيز مثل دو برادر ديگرش هلاک شود.) پس تامار به خانه پدرش رفت.

12پس از مدتی، زن يهودا مُرد. وقتی كه روزهای سوگواری سپری شد، يهودا با دوستش حيرهٔ عدولامی برای نظارت بر پشمچينی گوسفندان به تمنه رفت.

13به تامار خبر دادند كه پدر شوهرش برای چيدنِ پشمِ گوسفندان به طرف تمنه حركت كرده است. 14تامار لباس بيوگی خود را از تن درآورد و برای اين كه شناخته نشود چادری بر سر انداخته، دم دروازهٔ عينايم سر راه تمنه نشست، زيرا او ديد كه هر چند شيله بزرگ شده ولی او را به عقد وی در نياورده‌اند.

15يهودا او را ديد، ولی چون او روی خود را پوشانيده بود، او را نشناخت و پنداشت زن بدكاره‌ای است. 16پس به كنار جاده به طرف او رفته، به او پيشنهاد كرد كه با وی همبستر شود، غافل از اين كه عروس خودش می‌باشد. تامار به او گفت: «چقدر می‌خواهی به من بدهی؟»

17يهودا گفت: «بزغاله‌ای از گله‌ام برايت خواهم فرستاد.»

زن گفت: «برای اين كه مطمئن شوم كه بزغاله را می‌فرستی بايد چيزی نزد من گرو بگذاری.»

18يهودا گفت: «چه چيزی را گرو بگذارم؟»

زن جواب داد: «مُهر و عصايت را.» پس يهودا آنها را به او داد و با وی همبستر شد و در نتيجه تامار آبستن شد. 19پس از اين واقعه تامار بازگشت و دوباره لباس بيوِگی خود را پوشيد.

20يهودا بزغاله را به دوستش حيرهٔ عدولامی سپرد تا آن را برای آن زن ببرد و اشیا گرويی را پس بگيرد، اما حيره آن زن را نيافت. 21پس، از مردم آنجا پرسيد: «آن زن بدكاره‌ای كه دمِ دروازه، سر راه نشسته بود كجاست؟»

به او جواب دادند: «ما هرگز چنين زنی در اينجا نديده‌ايم.»

22حيره نزد يهودا بازگشت و به او گفت: «او را نيافتم و مردمان آنجا هم می‌گويند چنين زنی را در آنجا نديده‌اند.»

23يهودا گفت: «بگذار آن اشیا مال او باشد، مبادا رسوا شويم. به هر حال من بزغاله را برای او فرستادم، ولی تو نتوانستی او را پيدا كنی.»

24حدود سه ماه بعد از اين واقعه، به يهودا خبر دادند كه عروسش تامار زنا كرده و حامله است. يهودا گفت: «او را بيرون آوريد و بسوزانيد.»

25در حالی كه تامار را بيرون می‌آوردند تا او را بكشند اين پيغام را برای پدر شوهرش فرستاد: «مردی كه صاحب اين مُهر و عصا می‌باشد، پدر بچهٔ من است، آيا او را می‌شناسی؟»

26يهودا مُهر و عصا را شناخت و گفت: «او تقصيری ندارد، زيرا من به قول خود وفا نكردم و او را برای پسرم شيله نگرفتم.» يهودا ديگر با او همبستر نشد.

27چون وقت وضع حمل تامار رسيد، دوقلو زاييد. 28در موقع زايمان، يكی از پسرها دستش را بيرون آورد و قابله نخ قرمزی به مچ دست او بست. 29اما او دست خود را عقب كشيد و پسر ديگر، اول به دنيا آمد. قابله گفت: «چگونه بيرون آمدی؟» پس او را فارص (يعنی «بيرون آمدن») ناميدند. 30اندكی بعد، پسری كه نخ قرمز به دستش بسته شده بود متولد شد و او را زارح (يعنی «قرمز») ناميدند.