Ezekieli 32 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 32:1-32

Nyimbo ya Maliro a Farao

1Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti,

“Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu.

Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja.

Umakhuvula mʼmitsinje yako,

kuvundula madzi ndi mapazi ako

ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.

3“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri,

ndidzakuponyera khoka langa

ndi kukugwira mu ukonde wanga.

4Ndidzakuponya ku mtunda

ndi kukutayira pansi.

Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe,

ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.

5Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri

ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.

6Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako,

mpaka kumapiri komwe,

ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.

7Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba

ndikudetsa nyenyezi zake.

Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo,

ndipo mwezi sudzawala.

8Zowala zonse zamumlengalenga

ndidzazizimitsa;

ndidzachititsa mdima pa dziko lako,

akutero Ambuye Yehova.

9Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri

pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,

ku mayiko amene iwe sunawadziwe.

10Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe,

ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe

pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo.

Pa nthawi ya kugwa kwako,

aliyense wa iwo adzanjenjemera

moyo wake wonse.

11“ ‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti,

“ ‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni

lidzabwera kudzalimbana nawe.

12Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe

ndi lupanga la anthu amphamvu,

anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu.

Adzathetsa kunyada kwa Igupto,

ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.

13Ndidzawononga ziweto zake zonse

zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri.

Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu

kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.

14Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake

ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta,

akutero Ambuye Yehova.

15Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja;

ndikadzawononga dziko lonse

ndi kukantha onse okhala kumeneko,

adzadziwa kuti ndine Yehova.’

16“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”

17Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti: 18“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa. 19Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’ 20Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo. 21Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’

22“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo. 23Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.

24“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. 25Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.

26“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. 27Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo.

28“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.

29“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.

30“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.

31“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 32Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 32:1-32

为法老唱哀歌

1第十二年十二月一日,耶和华对我说: 2“人子啊,你要为埃及王法老唱哀歌,对他说,

“‘你自认为是列邦中的雄狮,

其实你像激荡江河、

用脚把江河搅浑的海怪。

3主耶和华说,

我要差遣多国组成的大军,

用我的网把你拉上来,

4抛在地上,丢在田野,

给天上的飞鸟吃,

让地上的走兽饱餐。

5我要把你的肉丢在山间,

把你的尸首填满山谷,

6用你的血浇灌大地,

漫过群山,溢满沟壑。

7当我消灭你的时候,

我要用云遮蔽天空,

使日月无光,星辰昏暗。

8我要遮蔽天上所有的光,

使黑暗笼罩你的四境。

这是主耶和华说的。

9“‘我把你灭亡的消息带到你不认识的列邦时,必使许多人惶恐不安。 10我在他们面前挥刀攻击你的时候,各国的人都必因你而惊骇,他们的君王必胆战心惊。在你倾覆那天,他们都必时刻为自己的性命战战兢兢。’

11“主耶和华这样说,‘巴比伦王的刀必来攻击你。 12我要使你的人民丧身在各国中最残暴的勇士刀下。

“‘他们必摧毁埃及的骄傲,

消灭她的人民。

13我要杀尽她河边的牲畜,

使人足兽蹄不再搅浑河水。

14我要使埃及的河流清澈见底,

像油一样缓缓流淌。

这是主耶和华说的。

15我要使埃及的土地荒凉,

毁灭其中的居民,

那时他们就知道我是耶和华。

16“‘这是列国为埃及唱的哀歌,各国的妇女要为埃及和她的人民唱这哀歌。这是主耶和华说的。’”

17第十二年十二月十五日,耶和华对我说: 18“人子啊,为埃及的百姓哀哭吧!我要把她与各强国的人民一同送入阴间。

19埃及啊,你比谁更美呢?

你下去跟未受割礼的人躺在一起吧!

20埃及人要倒毙在丧身刀下的人当中。刀已出鞘,她和她的国民要被拖走。 21英勇的统领要在阴间谈论埃及王和他的盟友说,‘这些丧身刀下、未受割礼的人下来长眠了。’

22亚述和她的大军都在那里,她周围是她大军的坟墓。他们都是丧身刀下的人。 23他们的坟墓在阴间的最深处,她的大军躺卧在她坟墓的周围。他们生前曾使人恐惧,如今却丧身刀下。 24以拦在那里,她的百姓在她坟墓的周围。他们都未受割礼,丧身刀下,下到了阴间。他们生前曾使人恐惧,如今却和下坟墓的人一同抱愧蒙羞。 25以拦躺卧在被杀的人当中,周围是她百姓的坟墓。他们都未受割礼、丧身刀下。他们生前曾使人恐惧,如今却和丧身刀下的人在一起,与下坟墓的人一同抱愧蒙羞。

26米设土巴都在那里,周围是她们百姓的坟墓。他们都未受割礼,生前曾使人恐惧,如今却丧身刀下。 27他们没有古代32:27 古代”有古卷作“未受割礼的”。勇士的荣耀葬礼,那些勇士带着兵器下到阴间,头枕着刀,尸骨上盖着盾,生前曾使人恐惧。

28“法老啊,你要被毁灭,跟那些未受割礼、丧身刀下的人躺在一起。

29以东也在那里,她的王侯尽管力量强大,却和丧身刀下的人在一起,与那些未受割礼、下坟墓的人躺在一起。

30“北方的诸王和所有的西顿人也在那里,虽然他们力量强大,令人恐惧,却羞辱地与被杀的人下到了阴间。他们未受割礼,与丧身刀下的人躺在一起,与下坟墓的人一同蒙羞。

31“法老看见这些人,便得到了安慰,因为并非只有他的军队被杀。这是主耶和华说的。 32我使法老生前给人带来恐惧,但他和他的百姓最后还是要躺卧在未受割礼、丧身刀下的人当中。这是主耶和华说的。”