Ezekieli 33 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 33:1-33

Ezekieli Akhala Mlonda

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda. 3Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo. 4Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha. 5Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka. 6Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’

7“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze. 8Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 9Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.

10“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’ ” 11Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?

12“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’ 13Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake. 14Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna, 15monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa. 16Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.

17“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama. 18Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo. 19Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo. 20Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”

Mbiri ya Kuwonongeka kwa Yerusalemu

21Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!” 22Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.

23Ndipo Yehova anandiyankhula kuti: 24“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’ 25Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli? 26Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’

27“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri. 28Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako. 29Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’

30“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’ 31Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo. 32Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.

33“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 33:1-33

耶和华立以西结为守望者

1耶和华对我说: 2“人子啊,你要告诉你的同胞,‘我若使战争降临某地,那地方的百姓就应选一人做守望者。 3守望者发现敌人来攻打,便吹号警告百姓。 4凡听见号声而不接受警告的,敌人来把他杀了,这流血的罪就要由他自己承担。 5因为他听见号声,却不接受警告,他的死是咎由自取。他若接受警告,就不至于死了。 6但如果守望者看见敌人来攻打而不吹号警告百姓,以致有人被敌人杀了,那人固然是因自己的罪恶而被杀,我却要向这守望者追讨那人被杀的血债。’

7“人子啊,现在我立你为以色列人的守望者,你要听我的信息,代我警告他们。 8如果我说恶人必定要死,你却不警告他离开罪恶的行径,他必因自己的罪而死,我却要向你追讨他丧命的血债。 9如果你警告恶人离开罪恶的行径,他却不听,他必因自己的罪恶而死,他的死与你无关。

10“人子啊,你要对以色列人说,‘你们说,我们背负过犯和罪恶,正因此而灭亡。我们怎能存活下去呢? 11你要告诉他们,主耶和华说,“我凭我的永恒起誓,我绝不喜欢恶人死亡,我更愿意恶人改邪归正,得以存活。以色列人啊,回头吧!回头吧!改邪归正吧!何必自取灭亡呢?”’ 12人子啊,你要对你的同胞说,‘当义人犯罪时,他以往的义救不了他;当恶人悔改时,他以往的恶不会使他灭没。义人若犯罪,他以往的义不能使他存活。’ 13我虽对义人说他必能存活,但如果他仗着自己的义而犯罪,他的义将不会被记念,他必因犯罪而死亡。 14我虽对恶人说他必定要死,但他若改邪归正,行事公正仁义, 15偿还抵押,归还赃物,遵行生命之律例,不再犯罪,就必存活,不致死亡。 16他犯的罪不会被追究,因为他行事公正仁义,所以必得存活。

17“你的同胞却说,主这样做不公平。其实是他们自己行事不公。 18义人离义行恶,必因恶行而死亡。 19恶人弃恶行义,必因义行而存活。 20可是你们却说,主这样做不公平。以色列人啊,我必按你们各人的行为审判你们。”

21在我们被掳后第十二年十月五日,有人从耶路撒冷逃出来对我说:“城已经沦陷了。” 22逃难的人来的前一晚,耶和华的灵降在我身上,开了我的口。当那人早上来到我这里时,我就开了口,不再沉默。

23耶和华对我说: 24“人子啊,那些住在以色列废墟中的人说,‘亚伯拉罕一人尚且能拥有这片土地,我们这么多人更能拥有这片土地为业。’ 25但你要告诉他们,主耶和华这样说,‘你们吃带血的肉,仰赖偶像,又杀人流血,怎能拥有这片土地呢? 26你们靠刀剑行可憎之事,个个玷污别人的妻子,你们怎能拥有这片土地呢?’ 27你要告诉他们,主耶和华这样说,‘我凭我的永恒起誓,那些住在废墟中的必死于刀下,逃到田野的必被野兽吞吃,躲进堡垒和洞穴的必死于瘟疫。 28我要使这片土地荒凉不堪,使她所夸耀的势力消逝。以色列的山必荒凉,杳无人迹。 29因为他们所行的一切可憎之事,我必使这地方荒凉不堪,那时他们就知道我是耶和华。’

30“人子啊,你的同胞在墙边和门口彼此议论你说,‘来,听听耶和华要他传什么信息。’ 31他们随着人群来到你面前,坐着聆听你的话,俨然像我的子民。但他们不付诸实行,嘴里说的是甜言蜜语,心中却追求不义之财。 32他们只听不做,你在他们眼中只不过是善唱情歌、长于弹奏乐器的人。 33看吧,我所说的必定应验。当一切应验的时候,他们就知道有先知在他们当中。”