Ezekieli 30 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

New International Reader’s Version

Ezekiel 30:1-26

1A message from the Lord came to me. The Lord said, 2“Son of man, prophesy. Say, ‘The Lord and King says,

“ ‘ “Cry out,

‘A terrible day is coming!’

3The day is near.

The day of the Lord is coming.

It will be a cloudy day.

The nations have been sentenced to die.

4I will send Nebuchadnezzar’s sword against Egypt.

Cush will suffer terribly.

Many will die in Egypt.

Then its wealth will be carried away.

Its foundations will be torn down.

5The people of Cush, Libya, Lydia, Kub and the whole land of Arabia will be killed by swords. So will the Jews who live in Egypt. They went there from the covenant land of Israel. And the Egyptians will die too.” ’ ”

6The Lord says,

“Those who were going to help Egypt will die.

The strength Egypt was so proud of will fail.

Its people will be killed by swords

from Migdol all the way to Aswan,”

announces the Lord and King.

7“Egypt will be more empty than any other land.

Its cities will be completely destroyed.

8I will set Egypt on fire.

All those who came to help it will be crushed.

Then they will know that I am the Lord.

9“At that time I will send messengers out in ships. They will terrify the people of Cush who are so contented. Cush will suffer greatly when Egypt falls. And you can be sure it will fall.”

10The Lord and King says,

“I will put an end to the huge armies of Egypt.

I will use Nebuchadnezzar, the king of Babylon, to do this.

11He and his armies will attack the land and destroy it.

They will not show its people any pity at all.

They will use their swords against Egypt.

They will fill the land with dead bodies.

12I will dry up the waters of the Nile River.

I will sell the land to an evil nation.

I will use the power of outsiders

to destroy the land and everything in it.

I have spoken. I am the Lord.”

13The Lord and King says,

“I will destroy the statues of Egypt’s gods.

I will put an end to the gods

the people in Memphis worship.

Egypt will not have princes anymore.

I will spread fear all through the land.

14I will completely destroy Upper Egypt.

I will set Zoan on fire.

I will punish Thebes.

15I will pour out my burning anger on Pelusium.

It is a fort in eastern Egypt.

I will wipe out the huge army of Thebes.

16I will set Egypt on fire.

Pelusium will groan with terrible pain.

Thebes will be ripped apart.

Memphis will suffer greatly

because of everything that happens.

17The young men of Heliopolis and Bubastis

will be killed by swords.

Their people will be taken away as prisoners.

18I will break Egypt’s power over other lands.

That will be a dark day for Tahpanhes.

There the strength Egypt was so proud of

will come to an end.

Egypt will be covered with clouds.

The people in its villages

will be taken away as prisoners.

19So I will punish Egypt.

Then they will know that I am the Lord.”

20It was the 11th year since King Jehoiachin had been brought to Babylon as a prisoner. On the seventh day of the first month, a message from the Lord came to me. The Lord said, 21“Son of man, I have broken the powerful arm of Pharaoh Hophra, the king of Egypt. No bandages have been put on his arm to heal it. It has not been put in a cast. So his arm will not be strong enough to use a sword. 22I am against Pharaoh, the king of Egypt. I will break both his arms. I will break his healthy arm and his broken one. His sword will fall from his hand. 23I will scatter the people of Egypt among the nations. I will send them to other countries. 24I will make the arms of the king of Babylon stronger. I will put my sword in his hand. But I will break the arms of Pharaoh. And he will groan in front of Nebuchadnezzar. He will cry out like someone dying from his wounds. 25I will make the arms of the king of Babylon stronger. But the arms of Pharaoh will not be able to help Egypt. I will put my sword in Nebuchadnezzar’s hand. He will get ready to use it against Egypt. Then they will know that I am the Lord. 26I will scatter the Egyptians among the nations. I will send them to other countries. Then they will know that I am the Lord.”